< Yesaya 26 >
1 Tsiku limenelo anthu a mʼdziko la Yuda adzayimba nyimbo iyi. Tili ndi mzinda wolimba. Mulungu amawuteteza ndi zipupa ndi malinga.
En ce jour-là ce Cantique sera chanté au pays de Juda; nous avons une ville forte; la délivrance y sera mise pour muraille et pour avant-mur.
2 Tsekulani zipata za mzinda kuti mtundu wolungama ndi wokhulupirika ulowemo.
Ouvrez les portes, et la nation juste, celle qui garde la fidélité, y entrera.
3 Inu mudzamupatsa munthu wa mtima wokhazikika mtendere weniweni.
C'est une délibération arrêtée, que tu conserveras la vraie paix; car on se confie en toi.
4 Mudalireni Yehova mpaka muyaya, chifukwa Yehova Mulungu ndiye Thanthwe losatha.
Confiez-vous en l'Eternel à perpétuité; car le rocher des siècles est en l'Eternel Dieu.
5 Iye amatsitsa anthu amene amadziyika pamwamba, iye amagwetsa pansi mzinda wodzitukumula, amagumula makoma ake ndi kuwagwetsa pansi pa fumbi penipeni.
Car il abaissera ceux qui habitent aux lieux haut élevés, il renversera la ville de haute retraite, il la renversera jusqu'en terre, il la réduira jusqu'à la poussière.
6 Mapazi a anthu akuwupondereza, mapazi a anthu oponderezedwa, mapazi anthu osauka.
Le pied marchera dessus; les pieds, [dis-je], des affligés, les plantes des chétifs [marcheront dessus].
7 Njira ya munthu wolungama ndi yosalaza, Inu Wolungamayo, mumasalaza njira ya wolungama.
Le sentier est uni au juste; tu dresses au niveau le chemin du juste.
8 Inde Yehova, timayenda mʼnjira zanu zolungama, ife timayembekezera Inu; mitima yathu imakhumba kukumbukira ndi kulemekeza dzina lanu.
Aussi t'avons-nous attendu, ô Eternel! dans le sentier de tes jugements, et le désir de notre âme tend vers ton Nom, et vers ton mémorial.
9 Moyo wanga umalakalaka Inu usiku wonse; nthawi yammawa ndimafunafuna Inu. Pamene muweruza dziko lapansi anthu amaphunzira kuchita chilungamo.
De nuit je t'ai désiré [de] mon âme, et dès le point du jour je te rechercherai de mon esprit, qui est au dedans de moi; car lorsque tes jugements sont en la terre, les habitants de la terre habitable apprennent la justice.
10 Ngakhale mukomere mtima anthu oyipa, saphunzira chilungamo. Amachita zoyipa mʼdziko la chilungamo, ndipo sazindikira ululu wa Yehova.
Est-il fait grâce au méchant? il n'en apprend point la justice, mais il agira méchamment en la terre de la droiture, et il ne regardera point à la majesté de l'Eternel.
11 Inu Yehova, mwatukula dzanja lanu kuti muwalange, koma iwo sakuliona dzanjalo. Aloleni anthu aone ndi kuchita manyazi poona mmene mukondera anthu anu; ndipo moto umene mwasonkhera adani anu uwapsereze.
Eternel, ta main est-elle haut élevée? ils ne [l']aperçoivent point; [mais] ils [l']apercevront, et ils seront honteux à cause de la jalousie [que tu montres] en faveur de ton peuple; et le feu dont tu punis tes ennemis les dévorera.
12 Yehova, mumatipatsa mtendere; ndipo zonse zimene ife tinazichita munatichitira ndinu.
Eternel! tu nous procureras la paix: car aussi c'est toi qui prends soin de tout ce qui nous regarde.
13 Inu Yehova Mulungu wathu, ngakhale takhala tikulamulidwa ndi ena mʼmalo mwanu, koma ife timalemekeza dzina lanu lokha.
Eternel notre Dieu, d'autres Seigneurs que toi nous ont maîtrisés, [mais] c'est par toi [seul] que nous faisons mention de ton Nom.
14 Iwo tsopano sadzadzukanso; mizimu yawo sidzabwera kudzativutitsa pakuti mwawalanga ndipo mwawawononga; palibenso amene amawakumbukira.
Ils sont morts, ils ne vivront plus; ils sont trépassés, ils ne se relèveront point, parce que tu les as visités et exterminés, et que tu as fait périr toute mémoire d'eux.
15 Inu Yehova, mwaukulitsa mtundu wathu; mwauchulukitsa ndithu ndipo mwalandirapo ulemu; mwaukuza mbali zonse za dziko.
Eternel, tu avais accru la nation, tu avais accru la nation, tu as été glorifié, [mais] tu les as jetés loin dans tous les bouts de la terre.
16 Yehova, anthu anu anabwera kwa Inu pamene anali mʼmasautso; pamene munawalanga, iwo anapemphera kwa Inu.
Eternel, étant en détresse ils se sont rendus auprès de toi, ils ont supprimé leur humble requête quand ton châtiment a été sur eux.
17 Monga mayi woyembekezera pamene nthawi yake yobereka yayandikira amamva kupweteka ndipo amalira ndi ululu, ifenso tinali chimodzimodzi pamaso panu, Inu Yehova.
Comme celle qui est enceinte est en travail, et crie dans ses tranchées, lorsqu'elle est prête d'enfanter; tels avons-nous été à cause de ton courroux, ô Eternel!
18 Ife chimodzimodzi tinamva ululu, ngati mayi pa nthawi yobala mwana, koma sitinapindulepo kanthu, kapena kupulumutsa dziko lapansi; sitinabadwitse anthu atsopano pa dziko pano.
Nous avons conçu, et nous avons été en travail; nous avons comme enfanté du vent, nous ne saurions en aucune manière délivrer le pays, et les habitants de la terre habitable ne tomberaient point [par notre force].
19 Koma anthu anu amene anafa adzakhalanso ndi moyo; matupi awo adzadzuka. Iwo amene ali ku fumbi tsopano adzadzuka ndi kuyimba mosangalala. Monga mame amafewetsa pansi kutsitsimutsa zomera, momwenso Yehova adzaukitsa anthu amene anafa kale.
Tes morts vivront, [même] mon corps mort [vivra]; ils se relèveront. Réveillez-vous et vous réjouissez avec chant de triomphe, vous habitants de la poussière; car ta rosée est comme la rosée des herbes, et la terre jettera dehors les trépassés.
20 Abale anga, pitani mukalowe mʼnyumba zanu ndipo mukadzitsekere; mukabisale kwa kanthawi kochepa mpaka ukali wake utatha.
Va, mon peuple, entre dans tes cabinets, et ferme ta porte sur toi; cache-toi pour un petit moment, jusques à ce que l'indignation soit passée.
21 Taonani, Yehova akubwera kuchokera kumene amakhala; akubwera kudzalanga anthu a dziko lapansi chifukwa cha machimo awo. Dziko lapansi lidzawulula magazi amene anakhetsedwa pa dzikolo; dziko lapansi silidzabisanso mitembo ya anthu ophedwa.
Car voici, l'Eternel s'en va sortir de son lieu pour visiter l'iniquité des habitants de la terre, [commise] contre lui; alors la terre découvrira le sang qu'elle aura reçu, et ne couvrira plus ceux qu'on a mis à mort.