< Yesaya 26 >

1 Tsiku limenelo anthu a mʼdziko la Yuda adzayimba nyimbo iyi. Tili ndi mzinda wolimba. Mulungu amawuteteza ndi zipupa ndi malinga.
Some day, [people in] Judah will sing this song: Our city [of Jerusalem] is strong! Yahweh protects our city; He is like [MET] a wall that surrounds it.
2 Tsekulani zipata za mzinda kuti mtundu wolungama ndi wokhulupirika ulowemo.
Open the gates of the city for people who are righteous; allow people who faithfully [obey Yahweh] to enter the city.
3 Inu mudzamupatsa munthu wa mtima wokhazikika mtendere weniweni.
Yahweh, those who trust in you, those who firmly resolve to never doubt you, you will enable them to feel perfectly peaceful.
4 Mudalireni Yehova mpaka muyaya, chifukwa Yehova Mulungu ndiye Thanthwe losatha.
[So] always trust in Yahweh, because Yahweh, [our God], is forever [like] [MET] a huge rock [under which we are sheltered/protected/safe].
5 Iye amatsitsa anthu amene amadziyika pamwamba, iye amagwetsa pansi mzinda wodzitukumula, amagumula makoma ake ndi kuwagwetsa pansi pa fumbi penipeni.
He humbles proud people and destroys cities whose people are arrogant. He causes those cities to collapse into the dust/dirt.
6 Mapazi a anthu akuwupondereza, mapazi a anthu oponderezedwa, mapazi anthu osauka.
[When that happens], poor and oppressed people will trample on the ruins.
7 Njira ya munthu wolungama ndi yosalaza, Inu Wolungamayo, mumasalaza njira ya wolungama.
[But as for] righteous people, Yahweh, you do what is right; [it is as though] you cause the paths where they walk to be level and smooth.
8 Inde Yehova, timayenda mʼnjira zanu zolungama, ife timayembekezera Inu; mitima yathu imakhumba kukumbukira ndi kulemekeza dzina lanu.
Yahweh, by obeying your laws we show that we trust you to help us; and what we desire is that you will be honored/praised/exalted.
9 Moyo wanga umalakalaka Inu usiku wonse; nthawi yammawa ndimafunafuna Inu. Pamene muweruza dziko lapansi anthu amaphunzira kuchita chilungamo.
[All] through the night I [SYN] desire to know you better, and each morning I still want to be with you. [Only] when you come to judge [and punish] people who live on the earth will they learn to do what is right.
10 Ngakhale mukomere mtima anthu oyipa, saphunzira chilungamo. Amachita zoyipa mʼdziko la chilungamo, ndipo sazindikira ululu wa Yehova.
[But] your acting kindly toward wicked people does not cause them to do what is good. [Even] in places where people do what is right, the wicked people continue to do what is evil, and they do not realize that you, Yahweh, are great.
11 Inu Yehova, mwatukula dzanja lanu kuti muwalange, koma iwo sakuliona dzanjalo. Aloleni anthu aone ndi kuchita manyazi poona mmene mukondera anthu anu; ndipo moto umene mwasonkhera adani anu uwapsereze.
Yahweh, [it is as though] your fist is raised up [ready to strike them], but they do not realize that. Show them that you are very eager to help your people. If your enemies would realize that, they would be ashamed; allow your fire to burn them up [because they are] your enemies.
12 Yehova, mumatipatsa mtendere; ndipo zonse zimene ife tinazichita munatichitira ndinu.
Yahweh, [we desire that] you will allow things to go well for us; everything that we have done is what you have enabled us to do.
13 Inu Yehova Mulungu wathu, ngakhale takhala tikulamulidwa ndi ena mʼmalo mwanu, koma ife timalemekeza dzina lanu lokha.
Yahweh, our God, others have ruled over us, but you [MTY] are the only one whom we honor.
14 Iwo tsopano sadzadzukanso; mizimu yawo sidzabwera kudzativutitsa pakuti mwawalanga ndipo mwawawononga; palibenso amene amawakumbukira.
Those who ruled us are [now] gone; they are dead; their spirits have left this earth, and they will not become alive [again]. You punished those rulers and got rid of them, and people do not even remember them any more.
15 Inu Yehova, mwaukulitsa mtundu wathu; mwauchulukitsa ndithu ndipo mwalandirapo ulemu; mwaukuza mbali zonse za dziko.
Yahweh, you have enabled our nation to become great; we are more in [now], and we have more land, [so we] thank/praise you.
16 Yehova, anthu anu anabwera kwa Inu pamene anali mʼmasautso; pamene munawalanga, iwo anapemphera kwa Inu.
Yahweh, when we were distressed, we asked you [to help us]; when you disciplined/punished us, we were able only to whisper when we prayed to you.
17 Monga mayi woyembekezera pamene nthawi yake yobereka yayandikira amamva kupweteka ndipo amalira ndi ululu, ifenso tinali chimodzimodzi pamaso panu, Inu Yehova.
Like pregnant women writhe and cry out when they are giving birth, we suffered very much, too.
18 Ife chimodzimodzi tinamva ululu, ngati mayi pa nthawi yobala mwana, koma sitinapindulepo kanthu, kapena kupulumutsa dziko lapansi; sitinabadwitse anthu atsopano pa dziko pano.
We had severe pain, but nothing good resulted [MET] from it. We have not rescued our people [from being conquered by our enemies], and we have not given birth to children [who will rule the world correctly] (OR, not defeated the armies [that have attacked other nations].
19 Koma anthu anu amene anafa adzakhalanso ndi moyo; matupi awo adzadzuka. Iwo amene ali ku fumbi tsopano adzadzuka ndi kuyimba mosangalala. Monga mame amafewetsa pansi kutsitsimutsa zomera, momwenso Yehova adzaukitsa anthu amene anafa kale.
But Yahweh’s people who have died will become alive [again], their corpses will become alive! Those whose bodies lie in graves will rise and shout joyfully! His light will be [like] dew that falls on his people who have died, who are [now] in the place where the dead people are, [and will cause them to become alive again].
20 Abale anga, pitani mukalowe mʼnyumba zanu ndipo mukadzitsekere; mukabisale kwa kanthawi kochepa mpaka ukali wake utatha.
But now, my people/fellow-citizens, go home and lock your doors! Hide for a short time, until [Yahweh] is no longer angry.
21 Taonani, Yehova akubwera kuchokera kumene amakhala; akubwera kudzalanga anthu a dziko lapansi chifukwa cha machimo awo. Dziko lapansi lidzawulula magazi amene anakhetsedwa pa dzikolo; dziko lapansi silidzabisanso mitembo ya anthu ophedwa.
Listen to this: Yahweh will come from heaven to punish [all] the people on the earth for the sins that they have committed. People will be able to see [PRS] the (blood of those/the people) who have been murdered; their murderers will no longer be able to hide.

< Yesaya 26 >