< Yesaya 26 >
1 Tsiku limenelo anthu a mʼdziko la Yuda adzayimba nyimbo iyi. Tili ndi mzinda wolimba. Mulungu amawuteteza ndi zipupa ndi malinga.
In that day shall this song be sung in the land of Judah: “We have a strong city; His aid doth God appoint for walls and bulwarks.
2 Tsekulani zipata za mzinda kuti mtundu wolungama ndi wokhulupirika ulowemo.
Open ye the gates, That the righteous nation may enter in, The nation that keepeth the truth.
3 Inu mudzamupatsa munthu wa mtima wokhazikika mtendere weniweni.
Him that is of a steadfast mind Thou wilt keep in continual peace, Because he trusteth in thee.
4 Mudalireni Yehova mpaka muyaya, chifukwa Yehova Mulungu ndiye Thanthwe losatha.
Trust ye in Jehovah forever, For the Lord Jehovah is an everlasting rock.
5 Iye amatsitsa anthu amene amadziyika pamwamba, iye amagwetsa pansi mzinda wodzitukumula, amagumula makoma ake ndi kuwagwetsa pansi pa fumbi penipeni.
For he hath brought down the inhabitants of the fortress; The lofty city he hath laid low; He hath laid her low even to the ground; He hath levelled her with the dust.
6 Mapazi a anthu akuwupondereza, mapazi a anthu oponderezedwa, mapazi anthu osauka.
The foot trampleth upon her, The feet of the poor, the steps of the needy.
7 Njira ya munthu wolungama ndi yosalaza, Inu Wolungamayo, mumasalaza njira ya wolungama.
The way of the upright is a smooth way; Thou, O most righteous, doth level the path of the upright!
8 Inde Yehova, timayenda mʼnjira zanu zolungama, ife timayembekezera Inu; mitima yathu imakhumba kukumbukira ndi kulemekeza dzina lanu.
In the way of thy judgments, O Jehovah, we have waited for thee; The desire of our souls is to thy name, and to the remembrance of thee.
9 Moyo wanga umalakalaka Inu usiku wonse; nthawi yammawa ndimafunafuna Inu. Pamene muweruza dziko lapansi anthu amaphunzira kuchita chilungamo.
My soul longeth for thee in the night, And my spirit within me seeketh thee in the morning; For when thy judgments are in the earth, The inhabitants of the world learn righteousness.
10 Ngakhale mukomere mtima anthu oyipa, saphunzira chilungamo. Amachita zoyipa mʼdziko la chilungamo, ndipo sazindikira ululu wa Yehova.
Though favor be shown to the wicked, He will not learn righteousness; In the land of uprightness will he deal unjustly, And have no regard to the majesty of Jehovah.
11 Inu Yehova, mwatukula dzanja lanu kuti muwalange, koma iwo sakuliona dzanjalo. Aloleni anthu aone ndi kuchita manyazi poona mmene mukondera anthu anu; ndipo moto umene mwasonkhera adani anu uwapsereze.
Thy hand, O Jehovah, is lifted up, yet do they not see; But they shall see with shame thy zeal for thy people; Yea, fire shall devour thine adversaries.
12 Yehova, mumatipatsa mtendere; ndipo zonse zimene ife tinazichita munatichitira ndinu.
Thou, O Jehovah, wilt give us peace; For all our works thou doest for us.
13 Inu Yehova Mulungu wathu, ngakhale takhala tikulamulidwa ndi ena mʼmalo mwanu, koma ife timalemekeza dzina lanu lokha.
O Jehovah, our God, other lords have had dominion over us besides thee; Only through thee do we call upon thy name.
14 Iwo tsopano sadzadzukanso; mizimu yawo sidzabwera kudzativutitsa pakuti mwawalanga ndipo mwawawononga; palibenso amene amawakumbukira.
They are dead, they shall not live; They are shades, they shall not rise. For thou hast visited and destroyed them, And caused all the memory of them to perish.
15 Inu Yehova, mwaukulitsa mtundu wathu; mwauchulukitsa ndithu ndipo mwalandirapo ulemu; mwaukuza mbali zonse za dziko.
“Thou wilt enlarge the nation, O Jehovah! Thou wilt enlarge the nation; thou wilt glorify thyself; Thou wilt widely extend all the borders of the land.
16 Yehova, anthu anu anabwera kwa Inu pamene anali mʼmasautso; pamene munawalanga, iwo anapemphera kwa Inu.
O Jehovah, in affliction they sought thee; They poured out their prayer, when thy chastisement was upon them.
17 Monga mayi woyembekezera pamene nthawi yake yobereka yayandikira amamva kupweteka ndipo amalira ndi ululu, ifenso tinali chimodzimodzi pamaso panu, Inu Yehova.
As a woman with child, when her delivery is near, Is in anguish, and crieth aloud in her pangs, So have we been, far from thy presence, O Jehovah!
18 Ife chimodzimodzi tinamva ululu, ngati mayi pa nthawi yobala mwana, koma sitinapindulepo kanthu, kapena kupulumutsa dziko lapansi; sitinabadwitse anthu atsopano pa dziko pano.
We have been with child; we have been in anguish, Yet have, as it were, brought forth wind. To the land we bring no deliverance; Nor are the inhabitants of the land born.
19 Koma anthu anu amene anafa adzakhalanso ndi moyo; matupi awo adzadzuka. Iwo amene ali ku fumbi tsopano adzadzuka ndi kuyimba mosangalala. Monga mame amafewetsa pansi kutsitsimutsa zomera, momwenso Yehova adzaukitsa anthu amene anafa kale.
O might thy dead live again, Might the dead bodies of my people arise! Awake, and sing, ye that dwell in the dust! For thy dew is like the dew upon plants, And the earth shall bring forth her dead.”
20 Abale anga, pitani mukalowe mʼnyumba zanu ndipo mukadzitsekere; mukabisale kwa kanthawi kochepa mpaka ukali wake utatha.
Come, my people, enter into thy chambers, And shut thy doors behind thee; Hide thyself for a little moment, Until the indignation be overpast!
21 Taonani, Yehova akubwera kuchokera kumene amakhala; akubwera kudzalanga anthu a dziko lapansi chifukwa cha machimo awo. Dziko lapansi lidzawulula magazi amene anakhetsedwa pa dzikolo; dziko lapansi silidzabisanso mitembo ya anthu ophedwa.
For behold, Jehovah cometh forth from his place, To punish the inhabitants of the earth for their iniquity; And the earth shall disclose her blood, And shall no longer cover her slain.