< Yesaya 26 >

1 Tsiku limenelo anthu a mʼdziko la Yuda adzayimba nyimbo iyi. Tili ndi mzinda wolimba. Mulungu amawuteteza ndi zipupa ndi malinga.
In that day this song shall be sung in the land of Judah: We have a strong city. He will appoint salvation for walls and bulwarks.
2 Tsekulani zipata za mzinda kuti mtundu wolungama ndi wokhulupirika ulowemo.
Open ye the gates, that the righteous nation which keeps faith may enter in.
3 Inu mudzamupatsa munthu wa mtima wokhazikika mtendere weniweni.
Thou will keep him in perfect peace, whose mind is stayed on thee, because he trusts in thee.
4 Mudalireni Yehova mpaka muyaya, chifukwa Yehova Mulungu ndiye Thanthwe losatha.
Trust ye in Jehovah forever, for in Jehovah, even Jehovah, is an everlasting rock.
5 Iye amatsitsa anthu amene amadziyika pamwamba, iye amagwetsa pansi mzinda wodzitukumula, amagumula makoma ake ndi kuwagwetsa pansi pa fumbi penipeni.
For he has brought down those who dwell on high. The lofty city, he lays it low. He lays it low even to the ground. He brings it even to the dust.
6 Mapazi a anthu akuwupondereza, mapazi a anthu oponderezedwa, mapazi anthu osauka.
The foot shall tread it down, even the feet of the poor, and the steps of the needy.
7 Njira ya munthu wolungama ndi yosalaza, Inu Wolungamayo, mumasalaza njira ya wolungama.
The way of the just is uprightness. Thou who are upright directs the path of the just.
8 Inde Yehova, timayenda mʼnjira zanu zolungama, ife timayembekezera Inu; mitima yathu imakhumba kukumbukira ndi kulemekeza dzina lanu.
Yea, in the way of thy judgments, O Jehovah, we have waited for thee, to thy name. Even to thy memorial, is the desire of our soul.
9 Moyo wanga umalakalaka Inu usiku wonse; nthawi yammawa ndimafunafuna Inu. Pamene muweruza dziko lapansi anthu amaphunzira kuchita chilungamo.
With my soul I have desired thee in the night. Yea, with my spirit within me I will seek thee earnestly. For when thy judgments are in the earth, the inhabitants of the world learn righteousness.
10 Ngakhale mukomere mtima anthu oyipa, saphunzira chilungamo. Amachita zoyipa mʼdziko la chilungamo, ndipo sazindikira ululu wa Yehova.
Let favor be shown to a wicked man, yet he will not learn righteousness. In the land of uprightness he will deal wrongfully, and will not behold the majesty of Jehovah.
11 Inu Yehova, mwatukula dzanja lanu kuti muwalange, koma iwo sakuliona dzanjalo. Aloleni anthu aone ndi kuchita manyazi poona mmene mukondera anthu anu; ndipo moto umene mwasonkhera adani anu uwapsereze.
Jehovah, thy hand is lifted up, yet they do not see. But they shall see thy zeal for the people, and be put to shame. Yea, fire shall devour thine adversaries.
12 Yehova, mumatipatsa mtendere; ndipo zonse zimene ife tinazichita munatichitira ndinu.
Jehovah, thou will ordain peace for us, for thou have also wrought all our works for us.
13 Inu Yehova Mulungu wathu, ngakhale takhala tikulamulidwa ndi ena mʼmalo mwanu, koma ife timalemekeza dzina lanu lokha.
O Jehovah our God, other lords besides thee have had dominion over us, but by thee only we will make mention of thy name.
14 Iwo tsopano sadzadzukanso; mizimu yawo sidzabwera kudzativutitsa pakuti mwawalanga ndipo mwawawononga; palibenso amene amawakumbukira.
Being dead, they shall not live. Being deceased, they shall not rise. Therefore thou have visited and destroyed them, and made all remembrance of them to perish.
15 Inu Yehova, mwaukulitsa mtundu wathu; mwauchulukitsa ndithu ndipo mwalandirapo ulemu; mwaukuza mbali zonse za dziko.
Thou have increased the nation, O Jehovah, thou have increased the nation. Thou are glorified. Thou have enlarged all the borders of the land.
16 Yehova, anthu anu anabwera kwa Inu pamene anali mʼmasautso; pamene munawalanga, iwo anapemphera kwa Inu.
Jehovah, in trouble they have visited thee, they poured out a prayer when thy chastening was upon them.
17 Monga mayi woyembekezera pamene nthawi yake yobereka yayandikira amamva kupweteka ndipo amalira ndi ululu, ifenso tinali chimodzimodzi pamaso panu, Inu Yehova.
As a woman with child, who draws near the time of her delivery, is in pain and cries out in her pangs, so we have been before thee, O Jehovah.
18 Ife chimodzimodzi tinamva ululu, ngati mayi pa nthawi yobala mwana, koma sitinapindulepo kanthu, kapena kupulumutsa dziko lapansi; sitinabadwitse anthu atsopano pa dziko pano.
We have been with child. We have been in pain. We have as it were brought forth wind. We have not wrought any deliverance in the earth, nor have the inhabitants of the world fallen.
19 Koma anthu anu amene anafa adzakhalanso ndi moyo; matupi awo adzadzuka. Iwo amene ali ku fumbi tsopano adzadzuka ndi kuyimba mosangalala. Monga mame amafewetsa pansi kutsitsimutsa zomera, momwenso Yehova adzaukitsa anthu amene anafa kale.
Thy dead shall live. My dead bodies shall arise. Awake and sing, ye who dwell in the dust, for thy dew is as the dew of herbs, and the earth shall cast forth the dead.
20 Abale anga, pitani mukalowe mʼnyumba zanu ndipo mukadzitsekere; mukabisale kwa kanthawi kochepa mpaka ukali wake utatha.
Come, my people, enter thou into thy chambers, and shut thy doors around thee. Hide thyself for a little moment until the indignation be passed over.
21 Taonani, Yehova akubwera kuchokera kumene amakhala; akubwera kudzalanga anthu a dziko lapansi chifukwa cha machimo awo. Dziko lapansi lidzawulula magazi amene anakhetsedwa pa dzikolo; dziko lapansi silidzabisanso mitembo ya anthu ophedwa.
For, behold, Jehovah comes forth out of his place to punish the inhabitants of the earth for their iniquity. The earth also shall disclose her blood, and shall no more cover her slain.

< Yesaya 26 >