< Yesaya 24 >

1 Taonani, Yehova adzawononga dziko lapansi ndi kulisandutsa chipululu; Iye adzasakaza maonekedwe ake ndi kumwaza anthu ake onse.
Гле, Господ ће испразнити земљу и опустети је, преврнуће је и расејаће становнике њене.
2 Aliyense zidzamuchitikira mofanana: wansembe chimodzimodzi munthu wamba, antchito aamuna mofanananso ndi ambuye awo aamuna, antchito aakazi chimodzimodzi ambuye awo aakazi, wogula chimodzimodzi wogulitsa, wobwereka chimodzimodzi wobwereketsa, okongola chimodzimodzi okongoza.
И биће свештеник као народ, господар као слуга, госпођа као слушкиња, продавац као купац, који даје у зајам као који узима у зајам, који узима добит као који даје.
3 Dziko lapansi lidzawonongedwa kwathunthu ndi kusakazikiratu. Yehova wanena mawu awa.
Сасвим ће се испразнити земља, и сасвим ће се опленити. Јер Господ рече ову реч.
4 Dziko lapansi likulira ndipo likufota, dziko lonse likuvutika ndipo likuwuma, anthu omveka a dziko lapansi akuvutika.
Тужиће земља и опасти, изнемоћи ће васиљена и опасти; изнемоћи ће главари народа земаљског.
5 Anthu ayipitsa dziko lapansi; posamvera malangizo ake; pophwanya mawu ake ndi pangano lake lamuyaya.
Јер се земља оскврни под становницима својим, јер преступише законе, изменише уредбе, раскидоше завет вечни.
6 Nʼchifukwa chake matemberero akuwononga dziko lapansi; anthu a mʼdzikomo akuzunzika chifukwa cha kulakwa kwawo, iwo asakazika ndipo atsala ochepa okha.
Зато ће проклетство прождрети земљу, и затрће се становници њени; зато ће изгорети становници земаљски, и мало ће људи остати.
7 Vinyo watsopano watha ndipo mphesa zikufota; onse okonda zosangalatsa ali ndi chisoni.
Тужиће вино, увенуће лоза винова, уздисаће сви који су веселог срца.
8 Kulira kokometsera kwa matambolini kwatha, phokoso la anthu osangalala latha, zeze wosangalatsa wati zii.
Престаће весеље уз бубње, нестаће граја оних који се веселе, престаће весеље уз гусле.
9 Anthu sadzayimbanso akumwa vinyo; akadzamwa zaukali zidzakhala zowawa mʼkamwa mwawo.
Неће пити вино уз песме, огорчаће силовито пиће онима који га пију.
10 Mzinda wachisokonezo uja wawonongeka; nyumba iliyonse yatsekedwa.
Разбиће се пусти град, затворене ће бити све куће да нико не улази.
11 Anthu akulira mʼmisewu kufuna vinyo; chimwemwe chonse chatheratu, palibenso chisangalalo pa dziko lapansi.
Тужњава ће бити по улицама ради вина, проћи ће свако весеље, отићи ће радост земаљска.
12 Mzinda wasanduka bwinja zipata zake zagumuka.
Пустош ће остати у граду, и врата ће се развалити.
13 Zimenezi ndizo zidzachitikire mitundu yonse ya dziko lapansi ndiponso pakati pa mitundu ya anthu. Zidzakhala ngati pamene mitengo ya olivi yayoyoledwa, kapena ngati nthawi ya kunkha la mphesa atatsiriza kukolola.
Јер ће бити у земљи и у народима као кад се оберу маслине, и као кад се паљеткује после бербе.
14 Koma otsala onse akufuwula ndi kuyimba mwachimwemwe; anthu akumadzulo akutamanda ukulu wa Yehova.
Ови ће подигнути глас свој и певаће, ради величанства Господњег подвикиваће од мора.
15 Nʼchifukwa chake inu akummawa, tamandani Yehova; ndi inu okhala mʼmphepete mwa nyanja kwezani dzina la Yehova, Mulungu wa Israeli.
Зато славите Господа у долинама, на острвима морским име Господа Бога Израиљевог.
16 Kuchokera kumalekezero a dziko lapansi tikumva kuyimba kotamanda “Wolungamayo.” Koma ine ndinati, “Ndatheratu, ndatheratu! Tsoka kwa ine! Anthu achinyengo akupitirizabe kuchita zachinyengo, inde chinyengo chawo chikunkerankera mʼtsogolo.”
С краја земље чусмо песме у славу Праведном; али рекох: Олошах! Олошах! Тешко мени! Неверници неверу чине, баш неверници неверу чине.
17 Inu anthu adziko lapansi, zoopsa, dzenje ndi msampha zikukudikirani.
Страхота и јама и замка пред тобом је, становниче земаљски!
18 Aliyense wothawa phokoso la zoopsa adzagwa mʼdzenje; ndipo aliyense wotuluka mʼdzenjemo adzakodwa ndi msampha. Zitseko zakumwamba zatsekulidwa, ndipo maziko a dziko lapansi agwedezeka.
И ко утече чувши за страхоту, пашће у јаму; а ко изађе из јаме, ухватиће се у замку; јер ће се уставе на висини отворити и затрешће се темељи земље.
19 Dziko lapansi lathyokathyoka, ndipo lagawika pakati, dziko lapansi lagwedezeka kotheratu.
Сва ће се земља разбити, сва ће се земља распасти, сва ће се земља усколебати.
20 Dziko lapansi likudzandira ngati munthu woledzera likugwedezeka ndi mphepo ngati chisimba; lalemedwa ndi machimo ake. Lidzagwa ndipo silidzadzukanso.
Сва ће се земља љуљати као пијан човек, и преместиће се као колиба, јер ће јој отежати безакоње њено, те ће пасти и неће више устати.
21 Tsiku limenelo Yehova adzalanga amphamvu a kumwamba ndiponso mafumu apansi pano.
И у то ће време походити Господ на висини војску високу и на земљи све цареве земаљске.
22 Mulungu adzawasonkhanitsa pamodzi ngati amʼndende amene ali mʼdzenje. Adzawatsekera mʼndende ndipo adzalangidwa patapita nthawi yayitali.
И скупиће се као што се скупљају сужњи у јаму, и биће затворени у тамницу, и после много времена биће похођени.
23 Mwezi udzanyazitsidwa, dzuwa lidzachita manyazi; pakuti Yehova Wamphamvuzonse adzakhala mfumu ndipo adzalamulira; pa Phiri la Ziyoni ndi ku Yerusalemu, ndipo adzaonetsa ulemerero wake pamaso pa akuluakulu.
И посрамиће се месец и сунце ће се застидети кад Господ над војскама стане царовати на гори Сиону и у Јерусалиму, и пред старешинама својим прослави се.

< Yesaya 24 >