< Yesaya 24 >

1 Taonani, Yehova adzawononga dziko lapansi ndi kulisandutsa chipululu; Iye adzasakaza maonekedwe ake ndi kumwaza anthu ake onse.
Voici, l'Éternel va rendre le pays vide et le dépouiller; il en bouleversera la face et en dispersera les habitants.
2 Aliyense zidzamuchitikira mofanana: wansembe chimodzimodzi munthu wamba, antchito aamuna mofanananso ndi ambuye awo aamuna, antchito aakazi chimodzimodzi ambuye awo aakazi, wogula chimodzimodzi wogulitsa, wobwereka chimodzimodzi wobwereketsa, okongola chimodzimodzi okongoza.
Et il en sera du sacrificateur comme du peuple, du maître comme de son serviteur, de la maîtresse comme de la servante, du vendeur comme de l'acheteur, du prêteur comme de l'emprunteur, du créancier comme du débiteur.
3 Dziko lapansi lidzawonongedwa kwathunthu ndi kusakazikiratu. Yehova wanena mawu awa.
Le pays sera entièrement vidé et mis au pillage, car l'Éternel a prononcé cet arrêt.
4 Dziko lapansi likulira ndipo likufota, dziko lonse likuvutika ndipo likuwuma, anthu omveka a dziko lapansi akuvutika.
Le pays est triste et mort; la terre est morte et languissante; les grands du peuple du pays sont languissants.
5 Anthu ayipitsa dziko lapansi; posamvera malangizo ake; pophwanya mawu ake ndi pangano lake lamuyaya.
Le pays était profané par ses habitants; car ils ont transgressé les lois, ils ont violé l'ordonnance, ils ont enfreint l'alliance éternelle.
6 Nʼchifukwa chake matemberero akuwononga dziko lapansi; anthu a mʼdzikomo akuzunzika chifukwa cha kulakwa kwawo, iwo asakazika ndipo atsala ochepa okha.
C'est pourquoi la malédiction dévore le pays, et ses habitants portent leur peine; c'est pourquoi les habitants du pays ont été consumés, et il n'est resté que très peu d'hommes.
7 Vinyo watsopano watha ndipo mphesa zikufota; onse okonda zosangalatsa ali ndi chisoni.
Le vin doux pleure, la vigne languit, tous ceux qui avaient le cœur joyeux soupirent;
8 Kulira kokometsera kwa matambolini kwatha, phokoso la anthu osangalala latha, zeze wosangalatsa wati zii.
Le son joyeux des tambourins a cessé, le bruit de la gaieté a pris fin, le son joyeux de la harpe a cessé;
9 Anthu sadzayimbanso akumwa vinyo; akadzamwa zaukali zidzakhala zowawa mʼkamwa mwawo.
On ne boit plus de vin en chantant; la boisson forte est amère à ceux qui la boivent.
10 Mzinda wachisokonezo uja wawonongeka; nyumba iliyonse yatsekedwa.
Elle est détruite, la cité déserte; toute maison est fermée, on n'y entre plus.
11 Anthu akulira mʼmisewu kufuna vinyo; chimwemwe chonse chatheratu, palibenso chisangalalo pa dziko lapansi.
On crie dans les rues parce que le vin manque; toute joie a disparu; l'allégresse du pays s'en est allée!
12 Mzinda wasanduka bwinja zipata zake zagumuka.
Il ne reste dans la ville que désolation; la porte tombe en débris sous les coups!
13 Zimenezi ndizo zidzachitikire mitundu yonse ya dziko lapansi ndiponso pakati pa mitundu ya anthu. Zidzakhala ngati pamene mitengo ya olivi yayoyoledwa, kapena ngati nthawi ya kunkha la mphesa atatsiriza kukolola.
Car il en est, au milieu du pays, parmi les peuples, comme lorsqu'on bat l'olivier, comme au grappillage après la vendange.
14 Koma otsala onse akufuwula ndi kuyimba mwachimwemwe; anthu akumadzulo akutamanda ukulu wa Yehova.
Mais ceux-ci élèvent la voix, ils jettent des cris de joie; des bords de la mer ils chantent la majesté de l'Éternel:
15 Nʼchifukwa chake inu akummawa, tamandani Yehova; ndi inu okhala mʼmphepete mwa nyanja kwezani dzina la Yehova, Mulungu wa Israeli.
Glorifiez donc l'Éternel aux lieux où naît la lumière; glorifiez le nom de l'Éternel, le Dieu d'Israël, dans les îles de la mer!
16 Kuchokera kumalekezero a dziko lapansi tikumva kuyimba kotamanda “Wolungamayo.” Koma ine ndinati, “Ndatheratu, ndatheratu! Tsoka kwa ine! Anthu achinyengo akupitirizabe kuchita zachinyengo, inde chinyengo chawo chikunkerankera mʼtsogolo.”
Du bout de la terre nous entendons chanter: Honneur au juste! Mais j'ai dit: Je suis perdu, je suis perdu! Malheur à moi! Les pillards pillent, les pillards s'acharnent au pillage!
17 Inu anthu adziko lapansi, zoopsa, dzenje ndi msampha zikukudikirani.
La terreur, la fosse et le filet vont t'atteindre, habitant du pays!
18 Aliyense wothawa phokoso la zoopsa adzagwa mʼdzenje; ndipo aliyense wotuluka mʼdzenjemo adzakodwa ndi msampha. Zitseko zakumwamba zatsekulidwa, ndipo maziko a dziko lapansi agwedezeka.
Et celui qui fuira au bruit de la terreur, tombera dans la fosse; et qui sera remonté de la fosse, tombera dans le filet. Car les écluses d'en haut s'ouvrent, et les fondements de la terre tremblent.
19 Dziko lapansi lathyokathyoka, ndipo lagawika pakati, dziko lapansi lagwedezeka kotheratu.
La terre se brise, la terre se rompt, la terre chancelle.
20 Dziko lapansi likudzandira ngati munthu woledzera likugwedezeka ndi mphepo ngati chisimba; lalemedwa ndi machimo ake. Lidzagwa ndipo silidzadzukanso.
La terre chancelle comme un homme ivre; elle vacille comme une cabane; son péché pèse sur elle; elle tombe, et ne se relèvera plus!
21 Tsiku limenelo Yehova adzalanga amphamvu a kumwamba ndiponso mafumu apansi pano.
En ce jour-là, l'Éternel châtiera, en haut, l'armée d'en haut, et sur la terre, les rois de la terre.
22 Mulungu adzawasonkhanitsa pamodzi ngati amʼndende amene ali mʼdzenje. Adzawatsekera mʼndende ndipo adzalangidwa patapita nthawi yayitali.
Et ils seront rassemblés captifs dans un cachot, et enfermés dans la prison; et après un grand nombre de jours ils seront châtiés.
23 Mwezi udzanyazitsidwa, dzuwa lidzachita manyazi; pakuti Yehova Wamphamvuzonse adzakhala mfumu ndipo adzalamulira; pa Phiri la Ziyoni ndi ku Yerusalemu, ndipo adzaonetsa ulemerero wake pamaso pa akuluakulu.
La lune rougira, et le soleil sera honteux, quand l'Éternel des armées régnera sur la montagne de Sion, à Jérusalem; et devant ses anciens resplendira la gloire.

< Yesaya 24 >