< Yesaya 24 >

1 Taonani, Yehova adzawononga dziko lapansi ndi kulisandutsa chipululu; Iye adzasakaza maonekedwe ake ndi kumwaza anthu ake onse.
Voici, l’Eternel fait le vide et la solitude sur la terre, il en bouleverse la face et en disperse les habitants.
2 Aliyense zidzamuchitikira mofanana: wansembe chimodzimodzi munthu wamba, antchito aamuna mofanananso ndi ambuye awo aamuna, antchito aakazi chimodzimodzi ambuye awo aakazi, wogula chimodzimodzi wogulitsa, wobwereka chimodzimodzi wobwereketsa, okongola chimodzimodzi okongoza.
Un même sort atteint peuple et prêtre, esclave et maître, servante et maîtresse, acheteur et vendeur, prêteur et emprunteur, créancier et débiteur.
3 Dziko lapansi lidzawonongedwa kwathunthu ndi kusakazikiratu. Yehova wanena mawu awa.
Elle est vidée à fond, la terre, complètement dépouillée: c’est l’Eternel qui a rendu cet arrêt.
4 Dziko lapansi likulira ndipo likufota, dziko lonse likuvutika ndipo likuwuma, anthu omveka a dziko lapansi akuvutika.
La terre est attristée et flétrie, le monde est désolé et languissant, l’élite de la population est abattue.
5 Anthu ayipitsa dziko lapansi; posamvera malangizo ake; pophwanya mawu ake ndi pangano lake lamuyaya.
C’Est que la terre a été souillée par ses habitants: ils ont transgressé les lois, violé les statuts, rompu le pacte antique.
6 Nʼchifukwa chake matemberero akuwononga dziko lapansi; anthu a mʼdzikomo akuzunzika chifukwa cha kulakwa kwawo, iwo asakazika ndipo atsala ochepa okha.
Aussi une malédiction dévore la terre, et ceux qui la peuplent, subissent le châtiment; les habitants de la terre sont consumés, et de rares mortels échappent.
7 Vinyo watsopano watha ndipo mphesa zikufota; onse okonda zosangalatsa ali ndi chisoni.
Le vin est en deuil, la vigne est contristée, tous ceux qui avaient le cœur joyeux soupirent.
8 Kulira kokometsera kwa matambolini kwatha, phokoso la anthu osangalala latha, zeze wosangalatsa wati zii.
Adieu les gais tambourins, adieu la joie bruyante de ceux qui s’amusaient, adieu le plaisir de la harpe!
9 Anthu sadzayimbanso akumwa vinyo; akadzamwa zaukali zidzakhala zowawa mʼkamwa mwawo.
On ne boit plus de vin en chantant, les liqueurs fortes ont un goût amer pour les buveurs.
10 Mzinda wachisokonezo uja wawonongeka; nyumba iliyonse yatsekedwa.
Elle est brisée la cité promise au désordre, toute demeure est close, rendue inaccessible.
11 Anthu akulira mʼmisewu kufuna vinyo; chimwemwe chonse chatheratu, palibenso chisangalalo pa dziko lapansi.
Les cris, au sujet du vin, retentissent dans les rues, tout plaisir est voilé de tristesse, la gaieté est bannie de la terre.
12 Mzinda wasanduka bwinja zipata zake zagumuka.
Dans la ville, il ne reste que désolation, les portes sont fracassées et réduites en ruine.
13 Zimenezi ndizo zidzachitikire mitundu yonse ya dziko lapansi ndiponso pakati pa mitundu ya anthu. Zidzakhala ngati pamene mitengo ya olivi yayoyoledwa, kapena ngati nthawi ya kunkha la mphesa atatsiriza kukolola.
Aussi il en sera de la terre, au sein des nations, comme des oliviers, après la récolte, comme des grappes oubliées, après vendanges faites.
14 Koma otsala onse akufuwula ndi kuyimba mwachimwemwe; anthu akumadzulo akutamanda ukulu wa Yehova.
Ceux-là élèveront la voix pour chanter, et, du côté de l’Ouest, éclateront en cris de joie devant la grandeur de l’Eternel.
15 Nʼchifukwa chake inu akummawa, tamandani Yehova; ndi inu okhala mʼmphepete mwa nyanja kwezani dzina la Yehova, Mulungu wa Israeli.
Oui, rendez hommage à l’Eternel dans les régions lumineuses, et, sur les côtes de la mer, proclamez le nom de l’Eternel, Dieu d’Israël.
16 Kuchokera kumalekezero a dziko lapansi tikumva kuyimba kotamanda “Wolungamayo.” Koma ine ndinati, “Ndatheratu, ndatheratu! Tsoka kwa ine! Anthu achinyengo akupitirizabe kuchita zachinyengo, inde chinyengo chawo chikunkerankera mʼtsogolo.”
Du bout de la terre nous entendons des cantiques: "Gloire au juste!" Mais moi je dis: "La misère est mon lot, la misère est mon lot! Malheur à moi! Les violents exercent leurs violences, ils poussent au comble leurs violences.
17 Inu anthu adziko lapansi, zoopsa, dzenje ndi msampha zikukudikirani.
Epouvante, fosse et piège vous menacent, habitants de la terre.
18 Aliyense wothawa phokoso la zoopsa adzagwa mʼdzenje; ndipo aliyense wotuluka mʼdzenjemo adzakodwa ndi msampha. Zitseko zakumwamba zatsekulidwa, ndipo maziko a dziko lapansi agwedezeka.
Quiconque prend la fuite devant les cris, de l’épouvante tombe dans la fosse, et, s’il remonte du fond de la fosse, il est pris dans le filet: les écluses s’ouvrent dans les hauteurs célestes et les fondements de la—terre sont ébranlés.
19 Dziko lapansi lathyokathyoka, ndipo lagawika pakati, dziko lapansi lagwedezeka kotheratu.
La terre éclate en se brisant, la terre tombe en pièces, la terre vacille étrangement.
20 Dziko lapansi likudzandira ngati munthu woledzera likugwedezeka ndi mphepo ngati chisimba; lalemedwa ndi machimo ake. Lidzagwa ndipo silidzadzukanso.
La terre chancelle comme un homme ivre, elle est secouée comme une hutte; elle est écrasée sous le poids de son iniquité, elle tombe et ne peut plus se relever.
21 Tsiku limenelo Yehova adzalanga amphamvu a kumwamba ndiponso mafumu apansi pano.
En ce jour, l’Eternel châtiera les milices du ciel au ciel et les rois de la terre sur la terre.
22 Mulungu adzawasonkhanitsa pamodzi ngati amʼndende amene ali mʼdzenje. Adzawatsekera mʼndende ndipo adzalangidwa patapita nthawi yayitali.
Ceux-ci seront réunis en tas comme des prisonniers au bord d’une fosse, ils seront enfermés dans la geôle; seulement, après de longs jours, on pensera à eux.
23 Mwezi udzanyazitsidwa, dzuwa lidzachita manyazi; pakuti Yehova Wamphamvuzonse adzakhala mfumu ndipo adzalamulira; pa Phiri la Ziyoni ndi ku Yerusalemu, ndipo adzaonetsa ulemerero wake pamaso pa akuluakulu.
Et la lune sera couverte de honte, le soleil de confusion, car l’Eternel-Cebaot régnera alors sur la montagne de Sion et à Jérusalem, et sa gloire brillera aux yeux de ses anciens.

< Yesaya 24 >