< Yesaya 24 >
1 Taonani, Yehova adzawononga dziko lapansi ndi kulisandutsa chipululu; Iye adzasakaza maonekedwe ake ndi kumwaza anthu ake onse.
Voici, l’Éternel rend le pays vide et le dévaste; et il bouleverse sa face, et il disperse ses habitants.
2 Aliyense zidzamuchitikira mofanana: wansembe chimodzimodzi munthu wamba, antchito aamuna mofanananso ndi ambuye awo aamuna, antchito aakazi chimodzimodzi ambuye awo aakazi, wogula chimodzimodzi wogulitsa, wobwereka chimodzimodzi wobwereketsa, okongola chimodzimodzi okongoza.
Et il en sera, comme du peuple, ainsi du sacrificateur; comme du serviteur, ainsi de son maître; comme de la servante, ainsi de sa maîtresse; comme de l’acheteur, ainsi du vendeur; comme du prêteur, ainsi de l’emprunteur; de celui qui prête à usure, comme de celui à qui est fait un prêt à usure.
3 Dziko lapansi lidzawonongedwa kwathunthu ndi kusakazikiratu. Yehova wanena mawu awa.
Le pays sera entièrement vidé et entièrement pillé; car l’Éternel a dit cette parole.
4 Dziko lapansi likulira ndipo likufota, dziko lonse likuvutika ndipo likuwuma, anthu omveka a dziko lapansi akuvutika.
Le pays mène deuil et se fane, le monde languit et se fane; ils languissent, – le peuple haut élevé du pays.
5 Anthu ayipitsa dziko lapansi; posamvera malangizo ake; pophwanya mawu ake ndi pangano lake lamuyaya.
Et le pays est souillé sous ceux qui l’habitent; car ils ont transgressé les lois, changé le statut, violé l’alliance éternelle.
6 Nʼchifukwa chake matemberero akuwononga dziko lapansi; anthu a mʼdzikomo akuzunzika chifukwa cha kulakwa kwawo, iwo asakazika ndipo atsala ochepa okha.
C’est pourquoi la malédiction a dévoré le pays, et ceux qui l’habitent subissent la peine de leur culpabilité; c’est pourquoi les habitants du pays sont consumés et il ne reste que peu d’hommes.
7 Vinyo watsopano watha ndipo mphesa zikufota; onse okonda zosangalatsa ali ndi chisoni.
Le moût mène deuil, la vigne languit; tous ceux qui étaient joyeux de cœur soupirent;
8 Kulira kokometsera kwa matambolini kwatha, phokoso la anthu osangalala latha, zeze wosangalatsa wati zii.
la joie des tambourins a cessé, le bruit tumultueux de ceux qui se réjouissent a pris fin, la joie de la harpe a cessé;
9 Anthu sadzayimbanso akumwa vinyo; akadzamwa zaukali zidzakhala zowawa mʼkamwa mwawo.
ils ne boivent pas le vin en chantant, les boissons fortes sont amères pour ceux qui les boivent.
10 Mzinda wachisokonezo uja wawonongeka; nyumba iliyonse yatsekedwa.
La cité de désolation est ruinée; toute maison est fermée, de sorte que personne n’y entre.
11 Anthu akulira mʼmisewu kufuna vinyo; chimwemwe chonse chatheratu, palibenso chisangalalo pa dziko lapansi.
Il y a un cri dans les rues au sujet du vin. Toute joie est assombrie, l’allégresse est bannie du pays;
12 Mzinda wasanduka bwinja zipata zake zagumuka.
la désolation reste dans la ville, et la porte est brisée, – une ruine.
13 Zimenezi ndizo zidzachitikire mitundu yonse ya dziko lapansi ndiponso pakati pa mitundu ya anthu. Zidzakhala ngati pamene mitengo ya olivi yayoyoledwa, kapena ngati nthawi ya kunkha la mphesa atatsiriza kukolola.
Car il en sera ainsi au milieu du pays, parmi les peuples, – comme quand on secoue l’olivier, comme le grappillage quand la vendange est achevée.
14 Koma otsala onse akufuwula ndi kuyimba mwachimwemwe; anthu akumadzulo akutamanda ukulu wa Yehova.
Ceux-ci élèveront leur voix, ils exulteront, ils pousseront des cris de joie depuis la mer, à cause de la majesté de l’Éternel.
15 Nʼchifukwa chake inu akummawa, tamandani Yehova; ndi inu okhala mʼmphepete mwa nyanja kwezani dzina la Yehova, Mulungu wa Israeli.
C’est pourquoi glorifiez l’Éternel dans les pays de l’aurore, – le nom de l’Éternel, le Dieu d’Israël, dans les îles de l’occident.
16 Kuchokera kumalekezero a dziko lapansi tikumva kuyimba kotamanda “Wolungamayo.” Koma ine ndinati, “Ndatheratu, ndatheratu! Tsoka kwa ine! Anthu achinyengo akupitirizabe kuchita zachinyengo, inde chinyengo chawo chikunkerankera mʼtsogolo.”
Du bout du pays nous avons entendu des chants: Gloire au juste! Et j’ai dit: Ma maigreur, ma maigreur, malheur à moi! Les perfides ont agi perfidement, les perfides ont agi avec une insigne perfidie.
17 Inu anthu adziko lapansi, zoopsa, dzenje ndi msampha zikukudikirani.
La frayeur, et la fosse, et le piège, sont sur toi, habitant du pays.
18 Aliyense wothawa phokoso la zoopsa adzagwa mʼdzenje; ndipo aliyense wotuluka mʼdzenjemo adzakodwa ndi msampha. Zitseko zakumwamba zatsekulidwa, ndipo maziko a dziko lapansi agwedezeka.
Et il arrivera que celui qui s’enfuit de devant le cri de la frayeur tombera dans la fosse, et celui qui monte du milieu de la fosse sera pris dans le piège; car les fenêtres d’en haut sont ouvertes, et les fondements de la terre sont ébranlés.
19 Dziko lapansi lathyokathyoka, ndipo lagawika pakati, dziko lapansi lagwedezeka kotheratu.
La terre est entièrement brisée, la terre se dissout, la terre est violemment remuée;
20 Dziko lapansi likudzandira ngati munthu woledzera likugwedezeka ndi mphepo ngati chisimba; lalemedwa ndi machimo ake. Lidzagwa ndipo silidzadzukanso.
la terre chancelle, elle chancelle comme un homme ivre; elle est ébranlée deçà et delà comme une cabane pour la nuit; sa transgression pèse sur elle: elle tombera et ne se relèvera pas.
21 Tsiku limenelo Yehova adzalanga amphamvu a kumwamba ndiponso mafumu apansi pano.
Et il arrivera, en ce jour-là, que l’Éternel visitera l’armée d’en haut, en haut, et les rois de la terre, sur la terre.
22 Mulungu adzawasonkhanitsa pamodzi ngati amʼndende amene ali mʼdzenje. Adzawatsekera mʼndende ndipo adzalangidwa patapita nthawi yayitali.
Et ils seront assemblés dans la fosse, comme on assemble des prisonniers, et ils seront renfermés dans la prison; et après beaucoup de jours ils seront visités.
23 Mwezi udzanyazitsidwa, dzuwa lidzachita manyazi; pakuti Yehova Wamphamvuzonse adzakhala mfumu ndipo adzalamulira; pa Phiri la Ziyoni ndi ku Yerusalemu, ndipo adzaonetsa ulemerero wake pamaso pa akuluakulu.
Et la lune rougira, et le soleil aura honte; car l’Éternel des armées régnera en la montagne de Sion et à Jérusalem, et devant ses anciens, en gloire.