< Yesaya 24 >

1 Taonani, Yehova adzawononga dziko lapansi ndi kulisandutsa chipululu; Iye adzasakaza maonekedwe ake ndi kumwaza anthu ake onse.
behold LORD to empty [the] land: country/planet and to waste her and to twist face: surface her and to scatter to dwell her
2 Aliyense zidzamuchitikira mofanana: wansembe chimodzimodzi munthu wamba, antchito aamuna mofanananso ndi ambuye awo aamuna, antchito aakazi chimodzimodzi ambuye awo aakazi, wogula chimodzimodzi wogulitsa, wobwereka chimodzimodzi wobwereketsa, okongola chimodzimodzi okongoza.
and to be like/as people like/as priest like/as servant/slave like/as lord his like/as maidservant like/as lady her like/as to buy like/as to sell like/as to borrow like/as to borrow like/as to lend like/as as which to exact in/on/with him
3 Dziko lapansi lidzawonongedwa kwathunthu ndi kusakazikiratu. Yehova wanena mawu awa.
to empty to empty [the] land: country/planet and to plunder to plunder for LORD to speak: speak [obj] [the] word [the] this
4 Dziko lapansi likulira ndipo likufota, dziko lonse likuvutika ndipo likuwuma, anthu omveka a dziko lapansi akuvutika.
to mourn to wither [the] land: country/planet to weaken to wither world to weaken height people [the] land: country/planet
5 Anthu ayipitsa dziko lapansi; posamvera malangizo ake; pophwanya mawu ake ndi pangano lake lamuyaya.
and [the] land: country/planet to pollute underneath: under to dwell her for to pass: trespass instruction to pass statute: decree to break covenant forever: enduring
6 Nʼchifukwa chake matemberero akuwononga dziko lapansi; anthu a mʼdzikomo akuzunzika chifukwa cha kulakwa kwawo, iwo asakazika ndipo atsala ochepa okha.
upon so oath to eat land: country/planet and be guilty to dwell in/on/with her upon so to scorch to dwell land: country/planet and to remain human little
7 Vinyo watsopano watha ndipo mphesa zikufota; onse okonda zosangalatsa ali ndi chisoni.
to mourn new wine to weaken vine to sigh all glad heart
8 Kulira kokometsera kwa matambolini kwatha, phokoso la anthu osangalala latha, zeze wosangalatsa wati zii.
to cease rejoicing tambourine to cease roar jubilant to cease rejoicing lyre
9 Anthu sadzayimbanso akumwa vinyo; akadzamwa zaukali zidzakhala zowawa mʼkamwa mwawo.
in/on/with song not to drink wine to provoke strong drink to/for to drink him
10 Mzinda wachisokonezo uja wawonongeka; nyumba iliyonse yatsekedwa.
to break town formlessness to shut all house: home from to come (in): come
11 Anthu akulira mʼmisewu kufuna vinyo; chimwemwe chonse chatheratu, palibenso chisangalalo pa dziko lapansi.
outcry upon [the] wine in/on/with outside to grow dark all joy to reveal: remove rejoicing [the] land: country/planet
12 Mzinda wasanduka bwinja zipata zake zagumuka.
to remain in/on/with city horror: destroyed and ruin to crush gate
13 Zimenezi ndizo zidzachitikire mitundu yonse ya dziko lapansi ndiponso pakati pa mitundu ya anthu. Zidzakhala ngati pamene mitengo ya olivi yayoyoledwa, kapena ngati nthawi ya kunkha la mphesa atatsiriza kukolola.
for thus to be in/on/with entrails: among [the] land: country/planet in/on/with midst [the] people like/as shaking olive like/as gleaning if: until to end: finish vintage
14 Koma otsala onse akufuwula ndi kuyimba mwachimwemwe; anthu akumadzulo akutamanda ukulu wa Yehova.
they(masc.) to lift: loud voice their to sing in/on/with pride LORD to cry out from sea: west
15 Nʼchifukwa chake inu akummawa, tamandani Yehova; ndi inu okhala mʼmphepete mwa nyanja kwezani dzina la Yehova, Mulungu wa Israeli.
upon so in/on/with flame to honor: honour LORD in/on/with coastland [the] sea name LORD God Israel
16 Kuchokera kumalekezero a dziko lapansi tikumva kuyimba kotamanda “Wolungamayo.” Koma ine ndinati, “Ndatheratu, ndatheratu! Tsoka kwa ine! Anthu achinyengo akupitirizabe kuchita zachinyengo, inde chinyengo chawo chikunkerankera mʼtsogolo.”
from wing [the] land: country/planet song to hear: hear beauty to/for righteous and to say wasting to/for me wasting to/for me woe! to/for me to act treacherously to act treacherously and treachery to act treacherously to act treacherously
17 Inu anthu adziko lapansi, zoopsa, dzenje ndi msampha zikukudikirani.
dread and pit and snare upon you to dwell [the] land: country/planet
18 Aliyense wothawa phokoso la zoopsa adzagwa mʼdzenje; ndipo aliyense wotuluka mʼdzenjemo adzakodwa ndi msampha. Zitseko zakumwamba zatsekulidwa, ndipo maziko a dziko lapansi agwedezeka.
and to be [the] to flee from voice: sound [the] dread to fall: fall to(wards) [the] pit and [the] to ascend: rise from midst [the] pit to capture in/on/with snare for window from height to open and to shake foundation land: country/planet
19 Dziko lapansi lathyokathyoka, ndipo lagawika pakati, dziko lapansi lagwedezeka kotheratu.
to shatter to shatter [the] land: country/planet to split to split land: country/planet to shake to shake land: country/planet
20 Dziko lapansi likudzandira ngati munthu woledzera likugwedezeka ndi mphepo ngati chisimba; lalemedwa ndi machimo ake. Lidzagwa ndipo silidzadzukanso.
to shake to shake land: country/planet like/as drunken and to wander like/as lodge and to honor: heavy upon her transgression her and to fall: fall and not to add: again to arise: rise
21 Tsiku limenelo Yehova adzalanga amphamvu a kumwamba ndiponso mafumu apansi pano.
and to be in/on/with day [the] he/she/it to reckon: punish LORD upon army [the] height in/on/with height and upon king [the] land: planet upon [the] land: planet
22 Mulungu adzawasonkhanitsa pamodzi ngati amʼndende amene ali mʼdzenje. Adzawatsekera mʼndende ndipo adzalangidwa patapita nthawi yayitali.
and to gather collecting prisoner upon pit and to shut upon locksmith and from abundance day to reckon: punish
23 Mwezi udzanyazitsidwa, dzuwa lidzachita manyazi; pakuti Yehova Wamphamvuzonse adzakhala mfumu ndipo adzalamulira; pa Phiri la Ziyoni ndi ku Yerusalemu, ndipo adzaonetsa ulemerero wake pamaso pa akuluakulu.
and be ashamed [the] moon and be ashamed [the] heat for to reign LORD Hosts in/on/with mountain: mount Zion and in/on/with Jerusalem and before old: elder his glory

< Yesaya 24 >