< Yesaya 23 >

1 Uthenga wonena za Turo: Lirani mofuwula, inu oyendetsa sitima za pa madzi za ku Tarisisi: pakuti mzinda wa Turo wawonongedwa ndipo mulibe nyumba kapena dooko. Zimenezi anazimva pochokera ku Kitimu.
Breme [naselbine] Tir. Tulite, ve ladje iz Taršíša, kajti ta je opustošena, tako da tam ni nobene hiše niti vhoda vanjo; od dežele Kitéjcev jim je razodeto.
2 Khalani chete inu anthu okhala mʼmbali mwa nyanja, inu amalonda a ku Sidoni, iwe amene unalemera ndi anthu oyenda pa nyanja.
Bodite mirni, vi prebivalci otoka, vi, ki so jih sidónski trgovci, ki prečkajo morje, na novo napolnili.
3 Pa nyanja zazikulu panabwera tirigu wa ku Sihori; zokolola za ku Nailo, ndipo munachita malonda ndi anthu a mitundu ina.
Ob velikih vodah je seme Šihórja, žetev reke, njeno poplačilo in ona je dobiček narodom.
4 Chita manyazi, iwe Sidimu pakuti nyanja yayankhula, linga la ku nyanja (Turo) layankhula kuti, “Sindinamvepo zowawa za kubereka kapena kuberekapo mwana; sindinalerepo ana aamuna kapena kulera ana aakazi.”
Bodi osramočen, oh Sidón, kajti morje je spregovorilo, celó moč morja, rekoč: »Ne mučim se, niti ne rojevam otrok, niti ne negujem mladeničev, niti ne vzgajam devic.
5 Mawuwa akadzamveka ku Igupto, iwo adzachita mantha akadzamva kuti Turo wawonongeka.
Kakor ob poročilu glede Egipta, tako bodo boleče zaskrbljeni ob poročilu iz [naselbine] Tir.
6 Wolokerani ku Tarisisi, lirani mofuwula, inu anthu okhala mʼmbali mwa nyanja.
Prepeljite se v Taršíš; tulite, vi prebivalci otoka.
7 Kodi uwu si mzinda wachisangalalo uja, mzinda wakalekale, umene anthu ake ankapita kukakhala ku mayiko akutali?
Ali je to vaše radostno mesto, katerega starodavnost je od starodavnih dni? Njegova lastna stopala ga bodo odnesla daleč, da začasno biva.
8 Kodi ndani anakonza zimenezi kuti zigwere Turo, mzinda umene unakhazikitsa mizinda ina, mzinda umene amalonda ake ndi akalonga ndi otchuka pa dziko lapansi?
Kdo je sprejel ta nasvet zoper [naselbino] Tir, obkrožujoče mesto, čigar trgovci so princi, čigar preprodajalci so častitljivi [ljudje] zemlje?
9 Yehova Wamphamvuzonse anakonza zimenezi kuti athetse kunyada kwawo ndi kutsitsa anthu otchuka a pa dziko lapansi.
Gospod nad bojevniki je to namenil, da omadežuje ponos vse slave in da privede v zaničevanje vse častitljive [ljudi] zemlje.
10 Mubalalike mʼdziko mwanu ngati mtsinje wa Nailo inu anthu a ku Tarisisi, pakuti mulibenso chokutetezani.
Prečkaj skozi svojo deželo kakor reka, oh taršíška hči. Tam ni več nobene moči.
11 Yehova watambasula dzanja lake kuloza ku nyanja ndipo wagwedeza maufumu ake. Iye walamula kuti Kanaani agwetse malinga ake.
Svojo roko je iztegnil nad morje, stresel je kraljestva. Gospod je izdal zapoved zoper trgovsko mesto, da uniči njegova močna oporišča.
12 Iye anati, “Simudzakondwanso konse, inu anthu opanikizidwa a ku Sidoni, tsopano wamphwanyidwa! “Ngakhale muwolokere ku Kitimu, kumeneko simukapezako mpumulo.”
Rekel je: »Ne boš se več razveseljevala, oh ti zatirana devica, hči sidónska. Vstani, prečkaj h Kitéjcem; tudi tam ne boš imela počitka.
13 Onani dziko la Ababuloni, anthu amenewa tsopano atheratu! Asiriya asandutsa Turo kukhala malo a zirombo za ku chipululu; anamanga nsanja zawo za nkhondo, anagumula malinga ake ndipo anawasandutsa bwinja.
Glej, dežela Kaldejcev; tega ljudstva ni bilo, dokler ga ni Asirec osnoval za tiste, ki prebivajo v divjini. Postavili so njegove stolpe, vzdignili so njegove palače; in privedel ga je do ruševin.
14 Lirani mofuwula, inu anthu oyendetsa sitima za pa madzi za ku Tarisisi; chifukwa malinga ako agwetsedwa!
Tulite ve ladje iz Taršíša, kajti vaša moč je opustošena.
15 Pa nthawi imeneyo Turo adzayiwalika pa zaka 70, amene ndi masiku a moyo wa mfumu. Koma potsiriza pa zaka 70 zimenezi, Turo adzakhala ngati mkazi wachiwerewere woyimbidwa mu nyimbo:
Na tisti dan se bo zgodilo, da bo [naselbina] Tir pozabljena sedemdeset let, glede na dneve enega kralja. Po koncu sedemdesetih let bo [naselbina] Tir pela kakor pocestnica.
16 “Tenga zeze wako uzungulire mzinda, iwe mkazi wachiwerewere woyiwalika; imba zeze mokometsera, imba nyimbo zambiri, kuti anthu akukumbukire.”
Vzemi harfo, pojdi okoli mesta, ti pocestnica, ki si bila pozabljena; naredi prijetno melodijo, poj mnoge pesmi, da se te bodo lahko spomnili.
17 Pakutha pa zaka 70, Yehova adzachitapo kanthu pa Turo. Iye adzabwerera ku ntchito yake yakale monga mkazi wachiwerewere ndipo adzachita zachiwerewere ndi maufumu onse a dziko lapansi.
Po koncu sedemdesetih let se bo zgodilo, da bo Gospod obiskal [naselbino] Tir in se obrnil k njenemu plačilu in zagrešila bo prešuštvovanje, z vsemi kraljestvi sveta, na obličju zemlje.
18 Koma phindu lake ndi malipiro ake adzazipereka kwa Yehova; sadzazikundika kapena kuzisunga. Phindu lake lidzapita kwa mtumiki wa Yehova kuti agule zakudya zambiri ndi zovala zokongola.
Njeno trgovsko blago in njena nagrada bosta sveta Gospodu. To ne bo več shranjeno niti kopičeno, kajti njen trgovski dobiček bo za tiste, ki prebivajo pred Gospodom, da bodo zadostno jedli in za trpežno oblačilo.

< Yesaya 23 >