< Yesaya 23 >

1 Uthenga wonena za Turo: Lirani mofuwula, inu oyendetsa sitima za pa madzi za ku Tarisisi: pakuti mzinda wa Turo wawonongedwa ndipo mulibe nyumba kapena dooko. Zimenezi anazimva pochokera ku Kitimu.
Бреме Тиру. Ридајте лађе тарсиске, јер је раскопан, да нема куће нити ко долази. Из земље китимске јави им се.
2 Khalani chete inu anthu okhala mʼmbali mwa nyanja, inu amalonda a ku Sidoni, iwe amene unalemera ndi anthu oyenda pa nyanja.
Умукните који живите на острву, које трговци сидонски поморци пунише.
3 Pa nyanja zazikulu panabwera tirigu wa ku Sihori; zokolola za ku Nailo, ndipo munachita malonda ndi anthu a mitundu ina.
И доходи му беху по великим водама семе сиорско, жетва с реке, и беше трг народима.
4 Chita manyazi, iwe Sidimu pakuti nyanja yayankhula, linga la ku nyanja (Turo) layankhula kuti, “Sindinamvepo zowawa za kubereka kapena kuberekapo mwana; sindinalerepo ana aamuna kapena kulera ana aakazi.”
Стиди се, Сидоне, јер говори море, сила морска вели: Не мучим се порођајем, не рађам, не одгајам момке, не подижем девојке.
5 Mawuwa akadzamveka ku Igupto, iwo adzachita mantha akadzamva kuti Turo wawonongeka.
Као што се ожалостише кад чуше за Мисир, тако ће се ожалостити кад чују за Тир.
6 Wolokerani ku Tarisisi, lirani mofuwula, inu anthu okhala mʼmbali mwa nyanja.
Идите у Тарсис, ридајте острвљани!
7 Kodi uwu si mzinda wachisangalalo uja, mzinda wakalekale, umene anthu ake ankapita kukakhala ku mayiko akutali?
Је ли то ваш весели град, чија је старина од давнина? Његове ће га ноге занети далеко у туђинство.
8 Kodi ndani anakonza zimenezi kuti zigwere Turo, mzinda umene unakhazikitsa mizinda ina, mzinda umene amalonda ake ndi akalonga ndi otchuka pa dziko lapansi?
Ко је то смислио на Тир, који раздаваше венце, чији трговци беху кнезови, и прекупци славни на земљи?
9 Yehova Wamphamvuzonse anakonza zimenezi kuti athetse kunyada kwawo ndi kutsitsa anthu otchuka a pa dziko lapansi.
Господ је над војскама то смислио, да осрамоти понос сваке славе и да поништи све славне на земљи.
10 Mubalalike mʼdziko mwanu ngati mtsinje wa Nailo inu anthu a ku Tarisisi, pakuti mulibenso chokutetezani.
Пређи преко земље своје као поток, кћери тарсиска; нема више појаса.
11 Yehova watambasula dzanja lake kuloza ku nyanja ndipo wagwedeza maufumu ake. Iye walamula kuti Kanaani agwetse malinga ake.
Руку своју подиже на море, задрма царства; Господ је заповедио за Ханан да се раскопају градови његови.
12 Iye anati, “Simudzakondwanso konse, inu anthu opanikizidwa a ku Sidoni, tsopano wamphwanyidwa! “Ngakhale muwolokere ku Kitimu, kumeneko simukapezako mpumulo.”
И вели: Нећеш се више веселити, осрамоћена девојко, кћери сидонска. Устани, иди у Китим, ни онде нећеш имати мира.
13 Onani dziko la Ababuloni, anthu amenewa tsopano atheratu! Asiriya asandutsa Turo kukhala malo a zirombo za ku chipululu; anamanga nsanja zawo za nkhondo, anagumula malinga ake ndipo anawasandutsa bwinja.
Ето земље халдејске; тог народа није било; Асур је основа за оне који живеху у пустињама, подигоше куле у њој, поградише дворове; и обрати се у развалине.
14 Lirani mofuwula, inu anthu oyendetsa sitima za pa madzi za ku Tarisisi; chifukwa malinga ako agwetsedwa!
Ридајте лађе тарсиске, јер је раскопан ваш град.
15 Pa nthawi imeneyo Turo adzayiwalika pa zaka 70, amene ndi masiku a moyo wa mfumu. Koma potsiriza pa zaka 70 zimenezi, Turo adzakhala ngati mkazi wachiwerewere woyimbidwa mu nyimbo:
И тада ће Тир бити заробљен седамдесет година, за век једног цара, а после седамдесет година певаће се Тиру као курви:
16 “Tenga zeze wako uzungulire mzinda, iwe mkazi wachiwerewere woyiwalika; imba zeze mokometsera, imba nyimbo zambiri, kuti anthu akukumbukire.”
Узми гусле, иди по граду, заборављена курво; добро ударај, певај и попевај, еда би те се опет опоменули.
17 Pakutha pa zaka 70, Yehova adzachitapo kanthu pa Turo. Iye adzabwerera ku ntchito yake yakale monga mkazi wachiwerewere ndipo adzachita zachiwerewere ndi maufumu onse a dziko lapansi.
Јер после седамдесет година Господ ће походити Тир, а он ће се вратити на курварску заслугу своју, и курваће се са свим царствима на земљи.
18 Koma phindu lake ndi malipiro ake adzazipereka kwa Yehova; sadzazikundika kapena kuzisunga. Phindu lake lidzapita kwa mtumiki wa Yehova kuti agule zakudya zambiri ndi zovala zokongola.
Али ће трговина његова и заслуга његова бити посвећена Господу, неће се остављати ни чувати, него ће трговина његова бити онима који наставају пред Господом да једу до ситости и имају одело добро.

< Yesaya 23 >