< Yesaya 23 >

1 Uthenga wonena za Turo: Lirani mofuwula, inu oyendetsa sitima za pa madzi za ku Tarisisi: pakuti mzinda wa Turo wawonongedwa ndipo mulibe nyumba kapena dooko. Zimenezi anazimva pochokera ku Kitimu.
The prophecy concerning Tyre. Howl, ye ships of Tarshish! For it is laid waste; No house, no entrance is left! From the land of the Chittaeans were the tidings brought to them.
2 Khalani chete inu anthu okhala mʼmbali mwa nyanja, inu amalonda a ku Sidoni, iwe amene unalemera ndi anthu oyenda pa nyanja.
Be amazed, ye inhabitants of the sea-coast, Which the merchants of Sidon, that pass over the sea, did crowd!
3 Pa nyanja zazikulu panabwera tirigu wa ku Sihori; zokolola za ku Nailo, ndipo munachita malonda ndi anthu a mitundu ina.
Upon the wide waters, the corn of the Nile, The harvest of the river, was her revenue; She was the mart of the nations.
4 Chita manyazi, iwe Sidimu pakuti nyanja yayankhula, linga la ku nyanja (Turo) layankhula kuti, “Sindinamvepo zowawa za kubereka kapena kuberekapo mwana; sindinalerepo ana aamuna kapena kulera ana aakazi.”
Be thou ashamed, O Sidon, for the sea hath spoken, The fortress of the sea hath spoken thus: “I have not travailed, nor brought forth children; I have not nourished youths, nor brought up virgins.”
5 Mawuwa akadzamveka ku Igupto, iwo adzachita mantha akadzamva kuti Turo wawonongeka.
When the tidings shall reach Egypt, They shall be filled with anguish at the tidings concerning Tyre.
6 Wolokerani ku Tarisisi, lirani mofuwula, inu anthu okhala mʼmbali mwa nyanja.
Pass ye over to Tarshish; Howl, ye inhabitants of the sea-coast!
7 Kodi uwu si mzinda wachisangalalo uja, mzinda wakalekale, umene anthu ake ankapita kukakhala ku mayiko akutali?
Is this your joyous city, Whose antiquity is of ancient days? Now her own feet bear her To sojourn far away.
8 Kodi ndani anakonza zimenezi kuti zigwere Turo, mzinda umene unakhazikitsa mizinda ina, mzinda umene amalonda ake ndi akalonga ndi otchuka pa dziko lapansi?
Who hath purposed this against Tyre, The dispenser of crowns, Whose merchants are princes, Whose traders the nobles of the earth?
9 Yehova Wamphamvuzonse anakonza zimenezi kuti athetse kunyada kwawo ndi kutsitsa anthu otchuka a pa dziko lapansi.
Jehovah of hosts hath purposed it, To bring down the pride of all glory, To humble the nobles of the earth.
10 Mubalalike mʼdziko mwanu ngati mtsinje wa Nailo inu anthu a ku Tarisisi, pakuti mulibenso chokutetezani.
Go over thy land like the Nile, O daughter of Tarshish! Now thy bonds are broken.
11 Yehova watambasula dzanja lake kuloza ku nyanja ndipo wagwedeza maufumu ake. Iye walamula kuti Kanaani agwetse malinga ake.
He hath stretched out his hand over the sea, He hath made the kingdoms tremble; Jehovah hath given commandment concerning Canaan To destroy her strong holds.
12 Iye anati, “Simudzakondwanso konse, inu anthu opanikizidwa a ku Sidoni, tsopano wamphwanyidwa! “Ngakhale muwolokere ku Kitimu, kumeneko simukapezako mpumulo.”
He hath said, Thou shalt no more rejoice, Thou ravished virgin, daughter of Sidon! Arise, pass over to the Chittaeans; Yet even there shalt thou have no rest.
13 Onani dziko la Ababuloni, anthu amenewa tsopano atheratu! Asiriya asandutsa Turo kukhala malo a zirombo za ku chipululu; anamanga nsanja zawo za nkhondo, anagumula malinga ake ndipo anawasandutsa bwinja.
Behold the land of the Chaldaeans, Who, not long ago, were not a people, —The Assyrian assigned it to the inhabitants of the wilderness, —They raise their watch-towers; They destroy her palaces; They make her a heap of ruins.
14 Lirani mofuwula, inu anthu oyendetsa sitima za pa madzi za ku Tarisisi; chifukwa malinga ako agwetsedwa!
Howl, ye ships of Tarshish! For your stronghold is destroyed.
15 Pa nthawi imeneyo Turo adzayiwalika pa zaka 70, amene ndi masiku a moyo wa mfumu. Koma potsiriza pa zaka 70 zimenezi, Turo adzakhala ngati mkazi wachiwerewere woyimbidwa mu nyimbo:
And it shall come to pass in that day, That Tyre shall be forgotten seventy years, According to the days of one king; But at the end of seventy years It shall be with Tyre as in the song of the harlot:
16 “Tenga zeze wako uzungulire mzinda, iwe mkazi wachiwerewere woyiwalika; imba zeze mokometsera, imba nyimbo zambiri, kuti anthu akukumbukire.”
“Take thy lyre, go about the city, O harlot, long forgotten; Make sweet melody; sing many songs, That thou mayst again be remembered!”
17 Pakutha pa zaka 70, Yehova adzachitapo kanthu pa Turo. Iye adzabwerera ku ntchito yake yakale monga mkazi wachiwerewere ndipo adzachita zachiwerewere ndi maufumu onse a dziko lapansi.
At the end of seventy years shall Jehovah show regard to Tyre, And she shall return to her hire, And play the harlot with all the kingdoms of the world, That are upon the face of the earth.
18 Koma phindu lake ndi malipiro ake adzazipereka kwa Yehova; sadzazikundika kapena kuzisunga. Phindu lake lidzapita kwa mtumiki wa Yehova kuti agule zakudya zambiri ndi zovala zokongola.
But her gain and her hire shall be holy to Jehovah; It shall not be treasured, nor laid up in store; But it shall be for them that dwell before Jehovah, For abundant food, and for splendid clothing.

< Yesaya 23 >