< Yesaya 23 >

1 Uthenga wonena za Turo: Lirani mofuwula, inu oyendetsa sitima za pa madzi za ku Tarisisi: pakuti mzinda wa Turo wawonongedwa ndipo mulibe nyumba kapena dooko. Zimenezi anazimva pochokera ku Kitimu.
The burden of Tyre. Howl, ye ships of the sea, for the house is destroyed, from whence they were wont to come: from the land of Cethim it is revealed to them.
2 Khalani chete inu anthu okhala mʼmbali mwa nyanja, inu amalonda a ku Sidoni, iwe amene unalemera ndi anthu oyenda pa nyanja.
Be silent, you that dwell in the island: the merchants of Sidon passing over the sea, have filled thee.
3 Pa nyanja zazikulu panabwera tirigu wa ku Sihori; zokolola za ku Nailo, ndipo munachita malonda ndi anthu a mitundu ina.
The seed of the Nile in many waters, the harvest of the river is her revenue: and she is become the mart of the nations.
4 Chita manyazi, iwe Sidimu pakuti nyanja yayankhula, linga la ku nyanja (Turo) layankhula kuti, “Sindinamvepo zowawa za kubereka kapena kuberekapo mwana; sindinalerepo ana aamuna kapena kulera ana aakazi.”
Be thou ashamed, O Sidon: for the sea speaketh, even the strength of the sea, saying: I have not been in labour, nor have I brought forth, nor have I nourished up young men, nor brought up virgins.
5 Mawuwa akadzamveka ku Igupto, iwo adzachita mantha akadzamva kuti Turo wawonongeka.
When it shall be heard in Egypt, they will be sorry when they shall hear of Tyre:
6 Wolokerani ku Tarisisi, lirani mofuwula, inu anthu okhala mʼmbali mwa nyanja.
Pass over the seas, howl, ye inhabitants of the island.
7 Kodi uwu si mzinda wachisangalalo uja, mzinda wakalekale, umene anthu ake ankapita kukakhala ku mayiko akutali?
Is not this your city, which gloried from of old in her antiquity? her feet shall carry her afar off to sojourn.
8 Kodi ndani anakonza zimenezi kuti zigwere Turo, mzinda umene unakhazikitsa mizinda ina, mzinda umene amalonda ake ndi akalonga ndi otchuka pa dziko lapansi?
Who hath taken this counsel against Tyre, that was formerly crowned, whose merchants were princes, and her traders the nobles of the earth?
9 Yehova Wamphamvuzonse anakonza zimenezi kuti athetse kunyada kwawo ndi kutsitsa anthu otchuka a pa dziko lapansi.
The Lord of hosts hath designed it, to pull down the pride of all glory, and bring to disgrace all the glorious ones of the earth.
10 Mubalalike mʼdziko mwanu ngati mtsinje wa Nailo inu anthu a ku Tarisisi, pakuti mulibenso chokutetezani.
Pass thy land as a river, O daughter of the sea, thou hast a girdle no more.
11 Yehova watambasula dzanja lake kuloza ku nyanja ndipo wagwedeza maufumu ake. Iye walamula kuti Kanaani agwetse malinga ake.
He stretched out his hand over the sea, he troubled kingdoms: the Lord hath given a charge against Chanaan, to destroy the strong ones thereof.
12 Iye anati, “Simudzakondwanso konse, inu anthu opanikizidwa a ku Sidoni, tsopano wamphwanyidwa! “Ngakhale muwolokere ku Kitimu, kumeneko simukapezako mpumulo.”
And he said: Thou shalt glory no more, O virgin daughter of Sidon, who art oppressed: arise and sail over to Cethim, there also thou shalt have no, rest.
13 Onani dziko la Ababuloni, anthu amenewa tsopano atheratu! Asiriya asandutsa Turo kukhala malo a zirombo za ku chipululu; anamanga nsanja zawo za nkhondo, anagumula malinga ake ndipo anawasandutsa bwinja.
Behold the land of the Chaldeans, there was not such a people, the Assyrian founded it: they have led away the strong ones thereof into captivity, they have destroyed the houses thereof, they have brought it to ruin.
14 Lirani mofuwula, inu anthu oyendetsa sitima za pa madzi za ku Tarisisi; chifukwa malinga ako agwetsedwa!
Howl, O ye ships of the sea, for your strength is laid waste.
15 Pa nthawi imeneyo Turo adzayiwalika pa zaka 70, amene ndi masiku a moyo wa mfumu. Koma potsiriza pa zaka 70 zimenezi, Turo adzakhala ngati mkazi wachiwerewere woyimbidwa mu nyimbo:
And it shall come to pass in that day that thou, O Tyre, shalt be forgotten, seventy years, according to the days of one king: but after seventy years, there shall be unto Tyre as the song of a harlot.
16 “Tenga zeze wako uzungulire mzinda, iwe mkazi wachiwerewere woyiwalika; imba zeze mokometsera, imba nyimbo zambiri, kuti anthu akukumbukire.”
Take a harp, go about the city, thou harlot that hast been forgotten: sing well, sing many a song, that thou mayst be remembered.
17 Pakutha pa zaka 70, Yehova adzachitapo kanthu pa Turo. Iye adzabwerera ku ntchito yake yakale monga mkazi wachiwerewere ndipo adzachita zachiwerewere ndi maufumu onse a dziko lapansi.
And it shall come to pass after seventy years, that the Lord will visit Tyre, and will bring her back again to her traffic: and she shall commit fornication again with all the kingdoms of the world upon the face of the earth.
18 Koma phindu lake ndi malipiro ake adzazipereka kwa Yehova; sadzazikundika kapena kuzisunga. Phindu lake lidzapita kwa mtumiki wa Yehova kuti agule zakudya zambiri ndi zovala zokongola.
And her merchandise and her hire shall be sanctified to the Lord: they shall not be kept in store, nor laid up: for her merchandise shall be for them that shall dwell before the Lord, that they may eat unto fulness, and be clothed for a continuance.

< Yesaya 23 >