< Yesaya 23 >

1 Uthenga wonena za Turo: Lirani mofuwula, inu oyendetsa sitima za pa madzi za ku Tarisisi: pakuti mzinda wa Turo wawonongedwa ndipo mulibe nyumba kapena dooko. Zimenezi anazimva pochokera ku Kitimu.
Наложено за Тир пророчество: Лелекайте, тарсийски кораби, Защото той се разруши, Та няма за вас къща или вход. (От Китимската земя им се извести това).
2 Khalani chete inu anthu okhala mʼmbali mwa nyanja, inu amalonda a ku Sidoni, iwe amene unalemera ndi anthu oyenda pa nyanja.
Млъкнете, вие жители на крайморието, Да! ти, когото сидонските търговци, Минаващи през морето, са обогатили
3 Pa nyanja zazikulu panabwera tirigu wa ku Sihori; zokolola za ku Nailo, ndipo munachita malonda ndi anthu a mitundu ina.
Доходът му, идещ през големи води, Бе житото на Нил, жетвата на реката Тъй щото той беше тържище на народите.
4 Chita manyazi, iwe Sidimu pakuti nyanja yayankhula, linga la ku nyanja (Turo) layankhula kuti, “Sindinamvepo zowawa za kubereka kapena kuberekapo mwana; sindinalerepo ana aamuna kapena kulera ana aakazi.”
Засрами се, Сидоне, защото морето проговори; Морската крепост рече: Не съм в болки, нито раждам, Нито момци отхранвам, нито девици отглеждам.
5 Mawuwa akadzamveka ku Igupto, iwo adzachita mantha akadzamva kuti Turo wawonongeka.
Когато се чуе това в Египет, Ще се мъчат много поради известието за Тир
6 Wolokerani ku Tarisisi, lirani mofuwula, inu anthu okhala mʼmbali mwa nyanja.
Заминете в Тарсис; Възридайте, жители на крайморието.
7 Kodi uwu si mzinda wachisangalalo uja, mzinda wakalekale, umene anthu ake ankapita kukakhala ku mayiko akutali?
Това ли е вашият весел град, Чиято древност е от стари времена? Нозете му ще го занесат далеч да странствува.
8 Kodi ndani anakonza zimenezi kuti zigwere Turo, mzinda umene unakhazikitsa mizinda ina, mzinda umene amalonda ake ndi akalonga ndi otchuka pa dziko lapansi?
Кой намисли това против Тир, Който раздаваше корони, Чиито търговци бяха князе, Чиито покупатели бяха знаменитите на света?
9 Yehova Wamphamvuzonse anakonza zimenezi kuti athetse kunyada kwawo ndi kutsitsa anthu otchuka a pa dziko lapansi.
Господ на Силите намисли това, За да посрами всяко гордеене със слава И да унижи всичките знаменити на света.
10 Mubalalike mʼdziko mwanu ngati mtsinje wa Nailo inu anthu a ku Tarisisi, pakuti mulibenso chokutetezani.
Залей земята си като Нил, тарсийска дъщерьо; Няма вече ограничение за тебе.
11 Yehova watambasula dzanja lake kuloza ku nyanja ndipo wagwedeza maufumu ake. Iye walamula kuti Kanaani agwetse malinga ake.
Господ простря ръката Си над морето. Потресе царствата; Господ даде заповед на Ханаан Да се съборят крепостите му.
12 Iye anati, “Simudzakondwanso konse, inu anthu opanikizidwa a ku Sidoni, tsopano wamphwanyidwa! “Ngakhale muwolokere ku Kitimu, kumeneko simukapezako mpumulo.”
Рече още: Не ще се радваш вече, О угнетена девице, сидонова дъщерьо: Стани да замини в Китим; Нито там ще имаш почивка,
13 Onani dziko la Ababuloni, anthu amenewa tsopano atheratu! Asiriya asandutsa Turo kukhala malo a zirombo za ku chipululu; anamanga nsanja zawo za nkhondo, anagumula malinga ake ndipo anawasandutsa bwinja.
Ето земята на халдеите; Тия люде не съществуват вече; Асириецът определи земята им за пустинни зверове; Издигнаха кулите си, събориха палатите му, И той ги обърна на развалини.
14 Lirani mofuwula, inu anthu oyendetsa sitima za pa madzi za ku Tarisisi; chifukwa malinga ako agwetsedwa!
Лелекайте, тарсийски кораби, Защото запустя крепостта ви.
15 Pa nthawi imeneyo Turo adzayiwalika pa zaka 70, amene ndi masiku a moyo wa mfumu. Koma potsiriza pa zaka 70 zimenezi, Turo adzakhala ngati mkazi wachiwerewere woyimbidwa mu nyimbo:
В оня ден Тир ще бъде забравен седемдесет години, Колкото са годините на един цар; А след седемдесетте години Ще бъде на Тир както в песента на блудницата се казва:
16 “Tenga zeze wako uzungulire mzinda, iwe mkazi wachiwerewere woyiwalika; imba zeze mokometsera, imba nyimbo zambiri, kuti anthu akukumbukire.”
Вземи арфа, обходи града, Забравена блуднице; Свири сладко, пей много песни, За да те помнят.
17 Pakutha pa zaka 70, Yehova adzachitapo kanthu pa Turo. Iye adzabwerera ku ntchito yake yakale monga mkazi wachiwerewere ndipo adzachita zachiwerewere ndi maufumu onse a dziko lapansi.
И след седемдесет години Господ ще посети дъщерята на Тир; И тя ще се наема пак, И ще блудствува с всичките царства на света по лицето на земята.
18 Koma phindu lake ndi malipiro ake adzazipereka kwa Yehova; sadzazikundika kapena kuzisunga. Phindu lake lidzapita kwa mtumiki wa Yehova kuti agule zakudya zambiri ndi zovala zokongola.
Но търговията и наемът й ще се посветят на Господа, Няма да се вложат в съкровище нито в склад; Защото търговията й ще бъде за живеещите пред Господа, За да ядат до ситост и да имат трайно облекло.

< Yesaya 23 >