< Yesaya 22 >

1 Uthenga wonena za Chigwa cha Masomphenya: Kodi chachitika nʼchiyani, kuti nonsenu mukwere pa madenga?
وحی درباره وادی رویا: الان تو را چه شد که کلیه بر بامهابرآمدی؟۱
2 Iwe mzinda wodzaza ndi chisangalalo chodzaza tsaya, iwe mzinda waphokoso ndi wosokonekera? Anthu ako ophedwa aja sanaphedwe ndi lupanga, kapena kufera pa nkhondo.
‌ای که پر از شورشها هستی و‌ای شهرپرغوغا و‌ای قریه مفتخر. کشتگانت کشته شمشیر نیستند و در جنگ هلاک نشده‌اند.۲
3 Atsogoleri ako onse ngakhale anathawa limodzi; koma anagwidwa osadziteteza nʼkomwe. Inu munapezeka ndipo nonse pamodzi munatengedwa ukapolo, ngakhale munathawa pamene mdani akanali patali.
جمیع سرورانت با هم گریختند و بدون تیراندازان اسیر گشتند. همگانی که در تو یافت شدند با هم اسیر گردیدند و به‌جای دور فرارکردند.۳
4 Nʼchifukwa chake Ine ndinati, “Chokani pamaso panga; ndilekeni ndilire ndi mtima wowawa. Musayesere kunditonthoza chifukwa cha kuwonongeka kwa anthu anga.”
بنابراین گفتم نظر خود را از من بگردانیدزیرا که با تلخی گریه می‌کنم. برای تسلی من درباره خرابی دختر قومم الحاح مکنید.۴
5 Lero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse walola kuti tione mavuto ndi kugonjetsedwa ndiponso chisokonezo mʼChigwa cha Masomphenya. Malinga agumuka, komanso anthu akanalira mofuwula ku mapiri.
زیرا خداوند یهوه صبایوت روز آشفتگی وپایمالی و پریشانی‌ای در وادی رویا دارد. دیوارها را منهدم می‌سازند و صدای استغاثه تا به کوهها می‌رسد.۵
6 Ankhondo a ku Elamu anadza pa magaleta ndi akavalo ali ndi mivi mʼmanja. Ankhondo a ku Kiri anakonzeka ndi zishango.
و عیلام با افواج مردان و سواران ترکش را برداشته است و قیر سپر را مکشوف نموده است،۶
7 Zigwa zanu zachonde ndi zodzaza ndi magaleta, ndipo asilikali okwera pa akavalo ayikidwa pa zipata za mzinda;
و وادیهای بهترینت از ارابه‌ها پرشده، سواران پیش دروازه هایت صف آرایی می‌نمایند،۷
8 zonse zoteteza Yuda zachotsedwa. Ndipo tsiku limenelo munayangʼanayangʼana zida zankhondo zomwe zinali mʼnyumba yaufumu ya nkhalango;
و پوشش یهودا برداشته می‌شود ودر آن روز به اسلحه خانه جنگل نگاه خواهیدکرد.۸
9 inu munaona kuti makoma ambiri a mzinda wa Davide anali ndi malo ambiri ogumuka; munasunga madzi mu chidziwe chakumunsi.
و رخنه های شهر داود را که بسیارندخواهید دید و آب برکه تحتانی را جمع خواهیدنمود.۹
10 Munawerenga nyumba zonse za mu Yerusalemu ndipo munagwetsa nyumba zina kuti mulimbitse linga logumuka lija.
و خانه های اورشلیم را خواهید شمرد وخانه‌ها را به جهت حصاربندی دیوارها خراب خواهید نمود.۱۰
11 Pakati pa makoma awiri munamanga chitsime chosungiramo madzi ochokera ku dziwe lakale, koma inu simunadalire Mulungu amene anapanga zimenezi, kapena kusamalako za Iye amene anazilenga kale lomwe.
و درمیان دو دیوار حوضی برای آب برکه قدیم خواهید ساخت اما به صانع آن نخواهید نگریست و به آنکه آن را از ایام پیشین ساخته است نگران نخواهید شد.۱۱
12 Pa tsiku limenelo, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse anakuyitanani kuti mulire ndi kukhetsa misozi; kumeta mutu wanu mpala ndi kuvala ziguduli.
و در آن روزخداوند یهوه صبایوت (شما را) به گریستن و ماتم کردن و کندن مو و پوشیدن پلاس خواهدخواند.۱۲
13 Koma mʼmalo mwake inu munakondwa ndi kusangalala; munapha ngʼombe ndi nkhosa; munadya nyama ndi kumwa vinyo. Inu mumati, “Tiyeni tidye ndi kumwa pakuti mawa tifa!”
و اینک شادمانی و خوشی و کشتن گاوان و ذبح کردن گوسفندان و خوردن گوشت ونوشیدن شراب خواهد بود که بخوریم و بنوشیم زیرا که فردا می‌میریم.۱۳
14 Yehova Wamphamvuzonse wandiwululira mondinongʼoneza kuti, “Tchimo limeneli sindidzakhululuka mpaka tsiku la kufa kwanu,” akutero Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse.
و یهوه صبایوت درگوش من اعلام کرده است که این گناه شما تابمیرید هرگز کفاره نخواهد شد. خداوند یهوه صبایوت این را گفته است.۱۴
15 Chimene Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Pita, ukanene kwa Sabina kapitawo, amene amayangʼanira nyumba yaufumu:
خداوند یهوه صبایوت چنین می‌گوید: «برو و نزد این خزانه‌دار یعنی شبنا که ناظر خانه است داخل شو و به او بگو:۱۵
16 Kodi ukuchita chiyani kuno, nanga ndani anakupatsa chilolezo kuti udzikumbire manda kuno, kudzikumbira manda pa phiri ndi kudzisemera malo opumulira mʼthanthwe?
تو را در اینجا چه‌کار است و در اینجا که را داری که در اینجا قبری برای خود کنده‌ای؟ ای کسی‌که قبر خود را درمکان بلند می‌کنی و مسکنی برای خویشتن درصخره می‌تراشی.»۱۶
17 “Samalira, Yehova watsala pangʼono kukugwira zolimba ndi kukuponya mwamphamvu, iwe munthu wamphamvu.
اینک‌ای مرد، خداوند البته تو را دورخواهد انداخت و البته تو را خواهد پوشانید.۱۷
18 Iye adzakukulunga kwambiri ngati mpira ndipo adzakuponyera mʼdziko lalikulu. Kumeneko ndiko ukafere ndipo kumeneko ndiko kudzatsalire magaleta ako. Ndipo udzasanduka wochititsa manyazi nyumba ya mbuye wako.
والبته تو را مثل گوی سخت خواهد پیچید و به زمین وسیع تو را خواهد افکند و در آنجا خواهی مرد و در آنجا ارابه های شوکت تو رسوایی خانه آقایت خواهد شد.۱۸
19 Ine ndidzakuchotsa pa ukapitawo wako ndipo ndidzakutsitsa pa udindo wako.
و تو را از منصبت خواهم راند و از مکانت به زیر افکنده خواهی شد.۱۹
20 “Tsiku limenelo ndidzayitanitsa mtumiki wanga, Eliyakimu mwana wa Hilikiya.
و در آن روز واقع خواهد شد که بنده خویش الیاقیم بن حلقیا را دعوت خواهم نمود.۲۰
21 Ndidzamuveka mkanjo wako ndi kumangira lamba wako mʼchiwuno mwake ndi kumupatsa ulamuliro wako. Iye adzakhala kholo la amene amakhala mu Yerusalemu ndiponso a fuko la Yuda.
و او را به‌جامه تو ملبس ساخته به کمربندت محکم خواهم ساخت و اقتدار تو را به‌دست اوخواهم داد و او ساکنان اورشلیم و خاندان یهودارا پدر خواهد بود.۲۱
22 Ndidzamupatsa ulamuliro wa banja la Davide. Adzatsekula ndipo palibe adzatseke, adzatseka popanda wina kutsekula.
و کلید خانه داود را بر دوش وی خواهم نهاد و چون بگشاید احدی نخواهدبست و چون ببندد، احدی نخواهد گشاد.۲۲
23 Ufumu wake udzakhala wokhazikika ngati chikhomo chokhomedwa pa malo olimba. Anthu adzalemekeza nyumba ya abale ake chifukwa cha iye.
و او را در جای محکم مثل میخ خواهم دوخت و برای خاندان پدر خود کرسی جلال خواهد بود.۲۳
24 Ana ndi abale a nyumba ya abambo ake adzakhala ngati katundu pa iye ngati ziwiya zopanda ntchito zimene zapachikidwa pa chikhomo.
وتمامی جلال خاندان پدرش را از اولاد و احفاد وهمه ظروف کوچک را از ظروف کاسه‌ها تا ظروف تنگها بر او خواهند آویخت.۲۴
25 “Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti, ‘Tsiku limeneli chikhomo chokhomedwa kwambiri chija sichidzalimbanso; chidzazuka ndipo chidzagwa ndipo zonse zopachikidwa zidzawonongedwa.’” Yehova wayankhula chomwechi.
و یهوه صبایوت می‌گوید که در آن روز آن میخی که در مکان محکم دوخته شده متحرک خواهد گردید و قطع شده، خواهد افتاد و باری که بر آن است، تلف خواهد شد زیرا خداوند این راگفته است.۲۵

< Yesaya 22 >