< Yesaya 22 >

1 Uthenga wonena za Chigwa cha Masomphenya: Kodi chachitika nʼchiyani, kuti nonsenu mukwere pa madenga?
Umthwalo wesigodi sombono. Kutheni kuwe khathesi, ukuthi ngulowo lalowo wakho akhwele empahleni zezindlu?
2 Iwe mzinda wodzaza ndi chisangalalo chodzaza tsaya, iwe mzinda waphokoso ndi wosokonekera? Anthu ako ophedwa aja sanaphedwe ndi lupanga, kapena kufera pa nkhondo.
Wena ogcwele imisindo, muzi oxokozelayo, dolobho elilentokozo, ababuleweyo bakho kababulawanga ngenkemba, kabafelanga empini.
3 Atsogoleri ako onse ngakhale anathawa limodzi; koma anagwidwa osadziteteza nʼkomwe. Inu munapezeka ndipo nonse pamodzi munatengedwa ukapolo, ngakhale munathawa pamene mdani akanali patali.
Bonke ababusi bakho babaleke kanyekanye, babotshwe ngabatshoki, bonke abatholakala kuwe, babotshiwe kanyekanye, babaleke besuka khatshana.
4 Nʼchifukwa chake Ine ndinati, “Chokani pamaso panga; ndilekeni ndilire ndi mtima wowawa. Musayesere kunditonthoza chifukwa cha kuwonongeka kwa anthu anga.”
Ngenxa yalokhu ngathi: Susani amehlo kimi; kangikhale kabuhlungu; ungaphangisi ukungiduduza ngenxa yokuchitheka kwendodakazi yabantu bakithi.
5 Lero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse walola kuti tione mavuto ndi kugonjetsedwa ndiponso chisokonezo mʼChigwa cha Masomphenya. Malinga agumuka, komanso anthu akanalira mofuwula ku mapiri.
Ngoba kulusuku lokusanganiseka, lolokunyathelela phansi, lolokuphithizela kweNkosi uJehova wamabandla esigodini sombono, lokudilizela phansi umduli, lolokuhlaba umkhosi kuze kube sentabeni.
6 Ankhondo a ku Elamu anadza pa magaleta ndi akavalo ali ndi mivi mʼmanja. Ankhondo a ku Kiri anakonzeka ndi zishango.
IElamu yathatha-ke isikhwama semitshoko, kanye lenqola, abantu, abagadi bamabhiza; leKiri yembula isihlangu.
7 Zigwa zanu zachonde ndi zodzaza ndi magaleta, ndipo asilikali okwera pa akavalo ayikidwa pa zipata za mzinda;
Kuzakuthi-ke izigodi zakho ezikhethekileyo zigcwala izinqola, labagadi bamabhiza bazihlele lokuzihlela ngasesangweni.
8 zonse zoteteza Yuda zachotsedwa. Ndipo tsiku limenelo munayangʼanayangʼana zida zankhondo zomwe zinali mʼnyumba yaufumu ya nkhalango;
Njalo yena uzakwembula isimbombozo sakoJuda; langalolosuku wena uzakhangela izikhali zendlu yehlathi.
9 inu munaona kuti makoma ambiri a mzinda wa Davide anali ndi malo ambiri ogumuka; munasunga madzi mu chidziwe chakumunsi.
Njalo lizabona imikenke yomuzi kaDavida, ukuthi minengi, liqoqe amanzi echibini elingaphansi.
10 Munawerenga nyumba zonse za mu Yerusalemu ndipo munagwetsa nyumba zina kuti mulimbitse linga logumuka lija.
Lizabala izindlu zeJerusalema, lidilize izindlu ukuze liqinise umduli.
11 Pakati pa makoma awiri munamanga chitsime chosungiramo madzi ochokera ku dziwe lakale, koma inu simunadalire Mulungu amene anapanga zimenezi, kapena kusamalako za Iye amene anazilenga kale lomwe.
Lizakwenza ichibi phakathi kwemiduli yomibili lisenzela amanzi omgodi omdala. Kodwa kaliyikukhangela kowakwenzayo, kalimnanzanga owakubumbayo kudala.
12 Pa tsiku limenelo, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse anakuyitanani kuti mulire ndi kukhetsa misozi; kumeta mutu wanu mpala ndi kuvala ziguduli.
Langalolosuku iNkosi uJehova wamabandla izamemezela ukulila, lokukhala, lokuphucwa kwamakhanda, lokugqokwa kwesaka.
13 Koma mʼmalo mwake inu munakondwa ndi kusangalala; munapha ngʼombe ndi nkhosa; munadya nyama ndi kumwa vinyo. Inu mumati, “Tiyeni tidye ndi kumwa pakuti mawa tifa!”
Kodwa khangela, injabulo lokuthaba, ukubulawa kwenkomo, lokuhlatshwa kwezimvu, ukudliwa kwenyama, lokunathwa kwewayini; lathi: Asidleni sinathe, ngoba kusasa sizakufa.
14 Yehova Wamphamvuzonse wandiwululira mondinongʼoneza kuti, “Tchimo limeneli sindidzakhululuka mpaka tsiku la kufa kwanu,” akutero Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse.
Kodwa iNkosi yamabandla yembula endlebeni zami isithi: Isibili lesisono kaliyikusenzelwa inhlawulo yokuthula lize life, kutsho iNkosi uJehova wamabandla.
15 Chimene Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Pita, ukanene kwa Sabina kapitawo, amene amayangʼanira nyumba yaufumu:
Itsho njalo iNkosi uJehova wamabandla: Hamba uye kulo umphathi, kuShebina, ophezu kwendlu, uthi:
16 Kodi ukuchita chiyani kuno, nanga ndani anakupatsa chilolezo kuti udzikumbire manda kuno, kudzikumbira manda pa phiri ndi kudzisemera malo opumulira mʼthanthwe?
Ulani lapha, njalo ulobani lapha, ukuthi uzigebhele ingcwaba lapha, njengozigebhela ingcwaba lakhe phezulu, ozigubhela indawo yokuhlala edwaleni?
17 “Samalira, Yehova watsala pangʼono kukugwira zolimba ndi kukuponya mwamphamvu, iwe munthu wamphamvu.
Khangela, iNkosi izakujikijela khatshana ngokujika kwendoda; izakugoqela ngokukugoqela,
18 Iye adzakukulunga kwambiri ngati mpira ndipo adzakuponyera mʼdziko lalikulu. Kumeneko ndiko ukafere ndipo kumeneko ndiko kudzatsalire magaleta ako. Ndipo udzasanduka wochititsa manyazi nyumba ya mbuye wako.
ikuthandele lokukuthandela njengebhola eligoqelwayo; njengebhola izakuphosela elizweni elibanzi; lalapho uzafela, lalapho izinqola zodumo lwakho zizakuba lihlazo, olwendlu yenkosi yakho!
19 Ine ndidzakuchotsa pa ukapitawo wako ndipo ndidzakutsitsa pa udindo wako.
Njalo ngizakusunduza usuke esikhundleni sakho, ikuwise ekumeni kwakho.
20 “Tsiku limenelo ndidzayitanitsa mtumiki wanga, Eliyakimu mwana wa Hilikiya.
Kuzakuthi-ke ngalolosuku ngibize inceku yami uEliyakhimi indodana kaHilikhiya;
21 Ndidzamuveka mkanjo wako ndi kumangira lamba wako mʼchiwuno mwake ndi kumupatsa ulamuliro wako. Iye adzakhala kholo la amene amakhala mu Yerusalemu ndiponso a fuko la Yuda.
ngizamgqokisa isigqoko sakho, ngimqinise ngebhanti lakho, nginikeze umbuso wakho esandleni sakhe; njalo yena uzakuba nguyise kubahlali beJerusalema lendlini yakoJuda.
22 Ndidzamupatsa ulamuliro wa banja la Davide. Adzatsekula ndipo palibe adzatseke, adzatseka popanda wina kutsekula.
Ngizabeka-ke isihluthulelo sendlu kaDavida ehlombe lakhe; yena uzavula kungavali muntu, avale kungavuli muntu.
23 Ufumu wake udzakhala wokhazikika ngati chikhomo chokhomedwa pa malo olimba. Anthu adzalemekeza nyumba ya abale ake chifukwa cha iye.
Ngizambethela njengesikhonkwane endaweni eqinileyo; njalo uzakuba yisihlalo sobukhosi esilodumo endlini kayise.
24 Ana ndi abale a nyumba ya abambo ake adzakhala ngati katundu pa iye ngati ziwiya zopanda ntchito zimene zapachikidwa pa chikhomo.
Njalo bazaphanyeka phezu kwakhe udumo lonke lwendlu kayise, inzalo lembewu, zonke izitsha ezincinyane, kusukela ezitsheni zenkezo kusiya kuzo zonke izitsha zeziphiso.
25 “Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti, ‘Tsiku limeneli chikhomo chokhomedwa kwambiri chija sichidzalimbanso; chidzazuka ndipo chidzagwa ndipo zonse zopachikidwa zidzawonongedwa.’” Yehova wayankhula chomwechi.
Ngalolosuku, itsho iNkosi yamabandla, isikhonkwane esabethelwa endaweni eqinileyo sizasuswa, siganyulwe siwe; lomthwalo obuphezu kwaso uzaqunywa; ngoba iNkosi ikhulumile.

< Yesaya 22 >