< Yesaya 22 >

1 Uthenga wonena za Chigwa cha Masomphenya: Kodi chachitika nʼchiyani, kuti nonsenu mukwere pa madenga?
Oracle contre la vallée de la Vision: "Qu’as-tu donc à monter tout entière sur les toits,
2 Iwe mzinda wodzaza ndi chisangalalo chodzaza tsaya, iwe mzinda waphokoso ndi wosokonekera? Anthu ako ophedwa aja sanaphedwe ndi lupanga, kapena kufera pa nkhondo.
ô ville pleine de rumeurs, tumultueuse cité, toujours si joyeuse? Tes morts n’ont pas péri par le glaive, n’ont pas succombé dans les combats.
3 Atsogoleri ako onse ngakhale anathawa limodzi; koma anagwidwa osadziteteza nʼkomwe. Inu munapezeka ndipo nonse pamodzi munatengedwa ukapolo, ngakhale munathawa pamene mdani akanali patali.
Tes chefs qui s’enfuient de concert sont pris sans être frappés par l’arc; ceux des tiens qui sont atteints sont capturés tous à la fois, tandis qu’ils se sauvent au loin.
4 Nʼchifukwa chake Ine ndinati, “Chokani pamaso panga; ndilekeni ndilire ndi mtima wowawa. Musayesere kunditonthoza chifukwa cha kuwonongeka kwa anthu anga.”
Aussi j’ai dit: "Laissez-moi, je veux répandre des larmes amères, ne vous mettez pas en peine pour me consoler du désastre de la fille de mon peuple.
5 Lero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse walola kuti tione mavuto ndi kugonjetsedwa ndiponso chisokonezo mʼChigwa cha Masomphenya. Malinga agumuka, komanso anthu akanalira mofuwula ku mapiri.
Car c’est un jour de trouble, de ruine et d’effarement qu’a décrété le Seigneur, Dieu-Cebaot, contre la vallée de la Vision: on abat les murailles et des cris résonnent dans les montagnes.
6 Ankhondo a ku Elamu anadza pa magaleta ndi akavalo ali ndi mivi mʼmanja. Ankhondo a ku Kiri anakonzeka ndi zishango.
Elam saisit le carquois, soutenu par des chars pleins de combattants et par des cavaliers, et Kir a mis à découvert son bouclier.
7 Zigwa zanu zachonde ndi zodzaza ndi magaleta, ndipo asilikali okwera pa akavalo ayikidwa pa zipata za mzinda;
Tes plus belles vallées sont envahies par des chars, et les cavaliers sont rangés près des portes.
8 zonse zoteteza Yuda zachotsedwa. Ndipo tsiku limenelo munayangʼanayangʼana zida zankhondo zomwe zinali mʼnyumba yaufumu ya nkhalango;
Et quand l’ennemi a enlevé ainsi le voile de Juda, tu mets alors ton espoir dans l’arsenal de la Maison de la Forêt.
9 inu munaona kuti makoma ambiri a mzinda wa Davide anali ndi malo ambiri ogumuka; munasunga madzi mu chidziwe chakumunsi.
Vous constatez les nombreuses brèches de la ville de David et emmagasinez les eaux de la Piscine inférieure.
10 Munawerenga nyumba zonse za mu Yerusalemu ndipo munagwetsa nyumba zina kuti mulimbitse linga logumuka lija.
Vous faites le recensement des maisons de Jérusalem, et abattez des maisons pour fortifier les remparts.
11 Pakati pa makoma awiri munamanga chitsime chosungiramo madzi ochokera ku dziwe lakale, koma inu simunadalire Mulungu amene anapanga zimenezi, kapena kusamalako za Iye amene anazilenga kale lomwe.
Vous établissez un réservoir entre les deux murs pour les eaux de la vieille Piscine; mais vous n’avez pas de regard pour Celui qui est cause de tout cela, et vous ne savez pas reconnaître Celui qui l’a préparé de loin.
12 Pa tsiku limenelo, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse anakuyitanani kuti mulire ndi kukhetsa misozi; kumeta mutu wanu mpala ndi kuvala ziguduli.
En ce jour, ce à quoi vous invite le Seigneur, Dieu-Cebaot, c’est à pleurer, à vous lamenter, à vous raser la tête, à ceindre le cilice.
13 Koma mʼmalo mwake inu munakondwa ndi kusangalala; munapha ngʼombe ndi nkhosa; munadya nyama ndi kumwa vinyo. Inu mumati, “Tiyeni tidye ndi kumwa pakuti mawa tifa!”
Or, voilà que chez vous tout est plaisir, allégresse, tuerie de bœufs, égorgement de moutons, mangerie de viandes, beuverie de vin: "Mangeons et buvons, dites-vous, car demain nous mourrons."
14 Yehova Wamphamvuzonse wandiwululira mondinongʼoneza kuti, “Tchimo limeneli sindidzakhululuka mpaka tsiku la kufa kwanu,” akutero Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse.
Mais l’arrêt de l’Eternel-Cebaot a été révélé à mes oreilles: "Ah! je le jure, ce péché ne vous sera point pardonné, jusqu’à votre mort," telle est la déclaration du Seigneur, Dieu-Cebaot.
15 Chimene Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Pita, ukanene kwa Sabina kapitawo, amene amayangʼanira nyumba yaufumu:
Ainsi parla le Seigneur, Dieu-Cebaot: "Va, transporte-toi auprès de ce haut dignitaire, auprès de Chebna, intendant du palais pour lui dire:
16 Kodi ukuchita chiyani kuno, nanga ndani anakupatsa chilolezo kuti udzikumbire manda kuno, kudzikumbira manda pa phiri ndi kudzisemera malo opumulira mʼthanthwe?
Que possèdes-tu à toi en ces lieux, qui t’appartient ici, pour t’y creuser un sépulcre? II ose se creuser un sépulcre sur les hauteurs, se tailler une demeure dans le roc!
17 “Samalira, Yehova watsala pangʼono kukugwira zolimba ndi kukuponya mwamphamvu, iwe munthu wamphamvu.
Voici, l’Eternel va t’empoigner avec vigueur, te faire tourner sur toi-même;
18 Iye adzakukulunga kwambiri ngati mpira ndipo adzakuponyera mʼdziko lalikulu. Kumeneko ndiko ukafere ndipo kumeneko ndiko kudzatsalire magaleta ako. Ndipo udzasanduka wochititsa manyazi nyumba ya mbuye wako.
il te roulera comme une pelote, te lancera comme une boule vers un pays aux vastes espaces. Là, tu mourras, là iront tes chars somptueux, ô toi, honte de la maison de ton maître.
19 Ine ndidzakuchotsa pa ukapitawo wako ndipo ndidzakutsitsa pa udindo wako.
Ainsi je te précipiterai de ton poste et te culbuterai de ta place."
20 “Tsiku limenelo ndidzayitanitsa mtumiki wanga, Eliyakimu mwana wa Hilikiya.
En ce jour, je ferai appel à mon serviteur Eliakim, fils de Hilkyyâhou.
21 Ndidzamuveka mkanjo wako ndi kumangira lamba wako mʼchiwuno mwake ndi kumupatsa ulamuliro wako. Iye adzakhala kholo la amene amakhala mu Yerusalemu ndiponso a fuko la Yuda.
Je le revêtirai de ta tunique, fixerai autour de lui ta ceinture et remettrai ton pouvoir entre ses mains; il sera un père pour les habitants de Jérusalem et la maison de Juda.
22 Ndidzamupatsa ulamuliro wa banja la Davide. Adzatsekula ndipo palibe adzatseke, adzatseka popanda wina kutsekula.
Je poserai la clef de la maison de David sur son épaule: il ouvrira et personne ne fermera, il fermera et personne n’ouvrira.
23 Ufumu wake udzakhala wokhazikika ngati chikhomo chokhomedwa pa malo olimba. Anthu adzalemekeza nyumba ya abale ake chifukwa cha iye.
Je le planterai solidement comme un clou dans un mur résistant, et il deviendra un trône de gloire pour la maison de son père.
24 Ana ndi abale a nyumba ya abambo ake adzakhala ngati katundu pa iye ngati ziwiya zopanda ntchito zimene zapachikidwa pa chikhomo.
Tout l’honneur de la maison de son père sera suspendu à lui les rejetons directs comme les branches éloignées, les plus petits ustensiles, depuis les bassins de métal jusqu’aux vases d’argile.
25 “Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti, ‘Tsiku limeneli chikhomo chokhomedwa kwambiri chija sichidzalimbanso; chidzazuka ndipo chidzagwa ndipo zonse zopachikidwa zidzawonongedwa.’” Yehova wayankhula chomwechi.
En ce jour, dit l’Eternel-Cebaot, le clou planté dans un endroit solide cédera, il sera abattu et tombera, et avec lui sera ruinée toute la charge qu’il supporte. C’Est l’Eternel qui a parlé.

< Yesaya 22 >