< Yesaya 22 >

1 Uthenga wonena za Chigwa cha Masomphenya: Kodi chachitika nʼchiyani, kuti nonsenu mukwere pa madenga?
Kolrhawk ham olrhuh, na imphu tom ah na yoeng thil na taengkah olphong te melae?
2 Iwe mzinda wodzaza ndi chisangalalo chodzaza tsaya, iwe mzinda waphokoso ndi wosokonekera? Anthu ako ophedwa aja sanaphedwe ndi lupanga, kapena kufera pa nkhondo.
Pang ol loh khopuei ah a bae la khorha te hue a sak thil. Na rhok neh aka yalpo te cunghang kah a ngawn pawt tih caemtloek kah a duek sak moenih a?
3 Atsogoleri ako onse ngakhale anathawa limodzi; koma anagwidwa osadziteteza nʼkomwe. Inu munapezeka ndipo nonse pamodzi munatengedwa ukapolo, ngakhale munathawa pamene mdani akanali patali.
Na rhalboei rhoek te lii om kolla rhenten boeih yong uh coeng. Nang aka hmu rhoek te boeih a khih uh coeng. Khohla kah aka yong rhoek te rhenten a khih uh coeng.
4 Nʼchifukwa chake Ine ndinati, “Chokani pamaso panga; ndilekeni ndilire ndi mtima wowawa. Musayesere kunditonthoza chifukwa cha kuwonongeka kwa anthu anga.”
Te dongah, “Kai taeng lamloh mangthong uh laeh. Rhah nen khaw ka phaep uh mai eh. Ka pilnam tanu kah rhoelrhanah dongah kai hloep hamla taholh uh thae boeh.
5 Lero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse walola kuti tione mavuto ndi kugonjetsedwa ndiponso chisokonezo mʼChigwa cha Masomphenya. Malinga agumuka, komanso anthu akanalira mofuwula ku mapiri.
Ka Boeipa caempuei Yahovah taengkah soekloeknah, tilnoinah neh tingtongnah khohnin, kolrhawk kah olphong dongah tah pangbueng te a phuet tih tlang te a o.
6 Ankhondo a ku Elamu anadza pa magaleta ndi akavalo ali ndi mivi mʼmanja. Ankhondo a ku Kiri anakonzeka ndi zishango.
Elam loh liva neh marhang caem hlang leng hang khuen tih Kir loh photling a dul.
7 Zigwa zanu zachonde ndi zodzaza ndi magaleta, ndipo asilikali okwera pa akavalo ayikidwa pa zipata za mzinda;
Na tuikol hmuennaep aka om khaw leng loh a baetawt thil marhang caem loh vongka ah tawn la tawn uh coeng.
8 zonse zoteteza Yuda zachotsedwa. Ndipo tsiku limenelo munayangʼanayangʼana zida zankhondo zomwe zinali mʼnyumba yaufumu ya nkhalango;
Judah kah himbaiyan te a lim coeng. Tekah khohnin ah duup im kah lungpok haica te na paelki coeng.
9 inu munaona kuti makoma ambiri a mzinda wa Davide anali ndi malo ambiri ogumuka; munasunga madzi mu chidziwe chakumunsi.
David khopuei kah a ueth hma na hmuh te yet coeng dae tuibuem dang kah tui te na coi.
10 Munawerenga nyumba zonse za mu Yerusalemu ndipo munagwetsa nyumba zina kuti mulimbitse linga logumuka lija.
Jerusalem kah im te khaw na tae uh tih vongtung na tuung ham im te na phil uh.
11 Pakati pa makoma awiri munamanga chitsime chosungiramo madzi ochokera ku dziwe lakale, koma inu simunadalire Mulungu amene anapanga zimenezi, kapena kusamalako za Iye amene anazilenga kale lomwe.
Tuibuem rhuem kah tui ham te vongtung laklo ah tui-im na saii uh. Tedae te aka saii te na paelki uh pawh. Te aka hlinsai daengrhae te na hmu uh pawh.
12 Pa tsiku limenelo, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse anakuyitanani kuti mulire ndi kukhetsa misozi; kumeta mutu wanu mpala ndi kuvala ziguduli.
Rhah ham neh rhaengsae ham khaw, lungawng la tlamhni yil ham khaw tekah khohnin ah ka Boeipa caempuei Yahovah a khue coeng.
13 Koma mʼmalo mwake inu munakondwa ndi kusangalala; munapha ngʼombe ndi nkhosa; munadya nyama ndi kumwa vinyo. Inu mumati, “Tiyeni tidye ndi kumwa pakuti mawa tifa!”
Saelhung top ham neh boiva ngawn ham, maeh caak ham neh misurtui ok ham tah omngaihnah neh kohoenah la, “Ca sih lamtah o sih, thangvuen kah ham tah n'duek uh hae pawn ni he,” na tiuh.
14 Yehova Wamphamvuzonse wandiwululira mondinongʼoneza kuti, “Tchimo limeneli sindidzakhululuka mpaka tsiku la kufa kwanu,” akutero Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse.
caempuei BOEIPA loh ka hna dongah han dueh coeng. Nangmih kah thaesainah he na duek uh duela han dawth mahpawh. Ka Boeipa caempuei Yahovah loh a thui coeng.
15 Chimene Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Pita, ukanene kwa Sabina kapitawo, amene amayangʼanira nyumba yaufumu:
Ka Boeipa caempuei Yahovah loh he ni a thui. Cet lamtah im kah hmaiben lah Shebna te paan laeh.
16 Kodi ukuchita chiyani kuno, nanga ndani anakupatsa chilolezo kuti udzikumbire manda kuno, kudzikumbira manda pa phiri ndi kudzisemera malo opumulira mʼthanthwe?
Nang taengkah he balae? Na taengkah he u bang nim? Namah ham tah he ah he phuel na vueh tih, anih kah phuel tah hmuensang ah na vueh pah aih. Anih ham tah pohmuen khaw thaelpang dongah na tarhit pah.
17 “Samalira, Yehova watsala pangʼono kukugwira zolimba ndi kukuponya mwamphamvu, iwe munthu wamphamvu.
BOEIPA tah nang aka hut tih hlang aka hlak neh nang aka buem la aka buem ham om coeng.
18 Iye adzakukulunga kwambiri ngati mpira ndipo adzakuponyera mʼdziko lalikulu. Kumeneko ndiko ukafere ndipo kumeneko ndiko kudzatsalire magaleta ako. Ndipo udzasanduka wochititsa manyazi nyumba ya mbuye wako.
Nang te palung hluem bangla n'kolong la, n'kolong ni. Khohmuen kah khocaeh dangka ah hnap na duek vetih na thangpomnah leng neh na boeipa kah im te yahpohnah om ni.
19 Ine ndidzakuchotsa pa ukapitawo wako ndipo ndidzakutsitsa pa udindo wako.
Nang te na rhaltawt hmuen lamloh kan thaek vetih na ngolhmuen lamloh nang kan koengloeng ni.
20 “Tsiku limenelo ndidzayitanitsa mtumiki wanga, Eliyakimu mwana wa Hilikiya.
Tekah khohnin a pha vaengah Hilkiah capa Eliakim te ka sal la ka khue ni.
21 Ndidzamuveka mkanjo wako ndi kumangira lamba wako mʼchiwuno mwake ndi kumupatsa ulamuliro wako. Iye adzakhala kholo la amene amakhala mu Yerusalemu ndiponso a fuko la Yuda.
Na angkidung te anih ka bai sak vetih na lamko neh anih ka talong ni. Na khohung te anih kut dongah ka paek vetih Jerusalem kah khosa ham neh Judah imkhui kah a napa la om ni.
22 Ndidzamupatsa ulamuliro wa banja la Davide. Adzatsekula ndipo palibe adzatseke, adzatseka popanda wina kutsekula.
David im kah cabi te anih kah laengpang dongah ka paek ni. A ong vetih kalh voel mahpawh, a khaih coeng te tah ong uh mahpawh.
23 Ufumu wake udzakhala wokhazikika ngati chikhomo chokhomedwa pa malo olimba. Anthu adzalemekeza nyumba ya abale ake chifukwa cha iye.
Anih te hmuen cak ah ciphuem neh ka khing vetih a napa im ham thangpomnah ngolkhoel la om ni.
24 Ana ndi abale a nyumba ya abambo ake adzakhala ngati katundu pa iye ngati ziwiya zopanda ntchito zimene zapachikidwa pa chikhomo.
A napa im kah thangpomnah boeih, cadil cahma neh a rhuirhong, hnopai a dikhnawn boeih, baeldung neh umam, tuitang neh baelyak boeih te anih a oi sak ni.
25 “Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti, ‘Tsiku limeneli chikhomo chokhomedwa kwambiri chija sichidzalimbanso; chidzazuka ndipo chidzagwa ndipo zonse zopachikidwa zidzawonongedwa.’” Yehova wayankhula chomwechi.
Te khohnin ah caempuei BOEIPA kah olphong loh, amah hmuen ah khak a khing hlingcong tah phoek pawn ni. Tlawt bal vetih colh pawn ni. Te vaengah a pum dongkah hnorhih a hal ni. BOEIPA loh a thui ngawn coeng.

< Yesaya 22 >