< Yesaya 21 >
1 Uthenga wonena za chipululu cha mʼmbali mwa Nyanja. Ankhondo a ku Elamu ndi Mediya adzabwera ngati kamvuluvulu amene akuwomba modutsa mʼmbali ya nyanja, kuchokera ku chipululu, dziko lochititsa mantha.
Isiphrofethi mayelana leNkangala engasoLwandle: Njengesivunguzane sidlula eNegebi, umhlaseli uvela enkangala evelela elizweni elesabekayo.
2 Ine ndaona zinthu zoopsa mʼmasomphenya: Wonyenga akunyenga, wofunkha akufunkha komanso owononga akuwononga. Elamu, yambani nkhondo! Mediya, zingani mzinda! Ine ndidzathetsa mavuto onse amene anayambitsa Ababuloni.
Ngitshengiswe umbono owesabekayo. Umthengisi uyathengisa, umkhuthuzi uthatha impahla. Elamu, hlasela! Mediya, vimbezela! Mina ngizakuqeda konke ukububula akudalileyo.
3 Chifukwa cha zimenezi thupi langa likunjenjemera ndi mantha, ndikumva ululu ngati wa mayi amene akubereka; ndikuvutika kwambiri ndi zimene ndikumva, ndathedwa nzeru ndi zimene ndikuziona.
Ngalokhu umzimba wami uyafuthelwa, ngiphethwe yibuhlungu obufana lobowesifazane ehelelwa. Ngithithibaliswa yilokhu engikuzwayo, ngidideka ngalokhu engikubonayo.
4 Mtima wanga ukugunda, ndipo ndikunjenjemera ndi mantha; chisisira chimene ndakhala ndikuchifuna chasanduka chinthu choopsa kwa ine.
Inhliziyo yami iphela amandla, ukwesaba kungenza ngiqhaqhazele; ukuhlwa engibe ngikufisa, sekusesabeka kimi.
5 Ankhondo a ku Elamu ndi Mediya akukonza matebulo, akuyala mphasa, akudya komanso kumwa! Mwadzidzidzi anamva mawu akuti, “Dzukani inu ankhondo, pakani mafuta zishango zanu!”
Itafula bayilungisile, bendlala amalembu bayadla, bayanatha. Sukumani lina zikhulu, ligcobe amahawu!
6 Zimene Ambuye akunena kwa ine ndi izi; “Pita, kayike mlonda kuti azinena zimene akuziona.
Lokhu yikho uThixo akutshoyo kimi: “Hamba uyefaka umlindi ukuze abike akubonayo.
7 Taonani, anthu akubwera ali pa akavalo ndipo akuyenda awiriawiri, okwera pa bulu kapena okwera pa ngamira, mlondayo akhale tcheru kwambiri.”
Angabona izinqola zempi, kulemihlambi yamabhiza, abagadi phezu kwabobabhemi loba abagadi phezu kwamakamela, kaqaphele; aqaphelisise sibili.”
8 Ndipo mlondayo anafuwula kuti, “Ambuye anga, tsiku ndi tsiku ndimakhala pa nsanja yolondera; Usiku uliwonse ndimakhala pa malo anga olondera.
Umlindi wasememeza esithi, “Nkosi yami, usuku ngosuku ngiyema phezu komphotshongo wokulinda; ubusuku ngabunye ngihlala ensikeni yami.
9 Taonani, uyo munthu akubwera atakwera pa galeta ali ndi gulu la akavalo. Mmodzi wa iwo akuti, ‘Babuloni wagwa, wagwa! Mafano onse a milungu yake agwa pansi ndipo aphwanyika!’”
Khangela, nangu umuntu esiza esenqoleni yempi lomhlambi wamabhiza. Uphendula esithi, ‘IBhabhiloni isidilikile, isidilikile! Zonke izifanekiso zezithombe zayo zihlakazekele phansi!’”
10 Inu anthu anga opunthidwa ndi kupetedwa ngati tirigu, ine ndikukuwuzani zimene ndamva ndikukuwuzani Uthenga wochokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli.
Awu bantu bami elibhulelwe esizeni, ngilitshela engikuzwileyo kuvela Thixo uSomandla, uNkulunkulu ka-Israyeli.
11 Uthenga wonena za Duma: Munthu wina akundiyitana kuchokera ku Seiri kuti, “Iwe mlonda, usikuwu utha liti? Iwe mlonda, utha liti kodi usikuwu?”
Isiphrofethi esimayelana leDuma: Umuntu othile uyangimemeza eseSeyiri, esithi, “Mlindi, kuyini okwebusuku okusaseleyo? Mlindi, kuyini okwebusuku okusaseleyo?”
12 Mlonda akuyankha kuti, “Kukucha, koma kudanso. Ngati ukufuna kufunsa, funsa tsopano; ndipo ubwerenso udzafunse.”
Umlindi uphendula esithi, “Ukusa kuyeza, kodwa lobusuku buyeza. Nxa ufuna ukubuza, buza; uphinde ubuye futhi.”
13 Uthenga wonena za Arabiya: Inu anthu amalonda a ku Dedani, amene usiku mumagona mʼzithukuluzi za ku Arabiya,
Isiphrofethi esimayelana le-Arabhiya: Lina zindwendwe zabakoDedani ezimise emahlabathini ase-Arabhiya,
14 perekani madzi kwa anthu aludzu. Inu anthu a ku Tema perekani chakudya kwa anthu othawa nkhondo.
lethelani abomileyo amanzi; lina elihlala eThema, lethelani ababalekayo ukudla.
15 Iwo akuthawa malupanga, lupanga losololedwa, akuthawa uta wokokakoka ndiponso nkhondo yoopsa.
Babalekela inkemba, inkemba eqhatshisiweyo, babalekela idandili eligotshiweyo, lokutshisa kwempi.
16 Zimene Ambuye akunena kwa ine ndi izi: “Chaka chimodzi chisanathe, potsata mmene amawerengera munthu waganyu, ulemerero wonse wa Kedara udzatheratu.
Lokhu yikho uThixo akutshoyo kimi ukuthi: “Phakathi komnyaka owodwa nje, njengendlela isisebenzi esiqhatshiweyo esingawubala ngayo, lonke udumo lweKhedari luzaphela.
17 Mwa anthu okoka uta, ankhondo a ku Kedara opulumuka adzakhala owerengeka.” Wayankhula ndi Yehova Mulungu wa Israeli.
Abasindayo kwabemitshoko, amabutho aseKhedari, bazakuba balutshwana.” UThixo, uNkulunkulu ka-Israyeli, usekhulumile.