< Yesaya 20 >

1 Mʼchaka chimene mkulu wankhondo wotumidwa ndi mfumu ya ku Asiriya, anabwera ku Asidodi ndi kuwuthira nkhondo ndi kuwulanda,
Roku, którego Tartan przyciągnął do Azotu, posłany będąc od Sargona, króla Assyryjskiego, i walczył przeciw Azotowi, i dobył go;
2 nthawi imeneyo Yehova anawuza Yesaya mwana wa Amozi kuti, “Pita kavule chiguduli ndi nsapato zako.” Ndipo iye anaterodi, ankangoyenda wamaliseche ndiponso wopanda nsapato.
Onegoż czasu rzekł Pan przez Izajasza, syna Amosowego, mówiąc: Idź, a rozwiąż wór z biódr twoich, a bóty twoje zzuj z nóg twoich; i uczynił tak, i chodził nago i boso.
3 Kenaka Yehova anati, “Monga momwe mtumiki wanga Yesaya wakhala akuyendera wamaliseche ndiponso wopanda nsapato kwa zaka zitatu ngati chizindikiro ndi chenjezo kwa dziko la Igupto ndi Kusi,
I rzekł Pan: Jako chodzi sługa mój Izajasz nago i boso, na znak i na cud tego, co się ma stać trzeciego roku Egiptowi i Murzyńskiej ziemi:
4 momwemonso mfumu ya ku Asiriya idzatenga ukapolo anthu a ku Igupto ndi a ku Kusi, anyamata ndi okalamba. Iwo adzakhala amaliseche ndi opanda nsapato, matako ali pa mtunda. Zimenezi zidzachititsa manyazi Igupto.
Tak powiedzie król Assyryjski więźniów Egipskich, i pojmanych Murzyńskich, młodych i starych, nagich i bosych, z obnażonemi zadkami na hańbę Egipczyków.
5 Amene ankadalira Kusi, ndiponso amene ankadzitukumula chifukwa cha Igupto adzakhumudwa ndi kuchita manyazi.
I przelękną się, i wstydzić się będą za Murzynów, na których się oglądali, i za Egipczanów, z których się chlubili.
6 Tsiku limenelo anthu amene amakhala mʼmbali mwa nyanja adzati, ‘Taonani zomwe zawachitikira amene ife tinkawadalira, amene ife tinkathawirako kuti atithandize ndi kutipulumutsa kwa mfumu ya ku Asiriya! Nanga ife tidzapulumuka bwanji?’”
Tedy rzecze dnia onego obywatel tej wyspy: Oto toć jest ucieczka nasza, do którejśmy uciekali o pomoc, abyśmy wyswobodzeni byli z mocy króla Assyryjskiego; jakożbyśmy tedy ujść mogli?

< Yesaya 20 >