< Yesaya 20 >

1 Mʼchaka chimene mkulu wankhondo wotumidwa ndi mfumu ya ku Asiriya, anabwera ku Asidodi ndi kuwuthira nkhondo ndi kuwulanda,
Iti tawen nga immay ni Tartan idiay Asdod, idi imbaon isuna ni Sargon nga ari ti Asiria, nakiranget isuna iti Asdod ket sinakupna daytoy.
2 nthawi imeneyo Yehova anawuza Yesaya mwana wa Amozi kuti, “Pita kavule chiguduli ndi nsapato zako.” Ndipo iye anaterodi, ankangoyenda wamaliseche ndiponso wopanda nsapato.
Iti dayta a tiempo, nagsao ni Yahweh babaen kenni Isaias a putot ni Amos a kinunana, “Mapanka ket ikkatem ti nakersang a lupot iti siketmo ken ikkatem dagita sandaliasmo.” Kasta ngarud ti inaramidna, nagnagna a lamolamo ken sakasaka.
3 Kenaka Yehova anati, “Monga momwe mtumiki wanga Yesaya wakhala akuyendera wamaliseche ndiponso wopanda nsapato kwa zaka zitatu ngati chizindikiro ndi chenjezo kwa dziko la Igupto ndi Kusi,
Kinuna ni Yahweh, “Kas iti adipenko a ni Isaias a nagna a lamolamo ken sakasaka iti las-ud ti tallo a tawen, pagilasinan ken ballaag daytoy maipapan iti Egipto ken maipapan ti Etiopia-
4 momwemonso mfumu ya ku Asiriya idzatenga ukapolo anthu a ku Igupto ndi a ku Kusi, anyamata ndi okalamba. Iwo adzakhala amaliseche ndi opanda nsapato, matako ali pa mtunda. Zimenezi zidzachititsa manyazi Igupto.
iti kastoy a wagas nga ipanawto ti ari ti Asiria dagiti natiliw a kas balud a taga-Egipto ken dagiti naipanaw a kas balud a taga-Etiopia, ubing ken nataengan, lamolamo ken sakasaka ken saan a naabbongan dagiti patongda, a pakaibabainan ti Egipto.
5 Amene ankadalira Kusi, ndiponso amene ankadzitukumula chifukwa cha Igupto adzakhumudwa ndi kuchita manyazi.
Maupay ken maibabaindanto, gapu ta ti Etiopia ti namnamada ken ti Egipto ti dayagda.
6 Tsiku limenelo anthu amene amakhala mʼmbali mwa nyanja adzati, ‘Taonani zomwe zawachitikira amene ife tinkawadalira, amene ife tinkathawirako kuti atithandize ndi kutipulumutsa kwa mfumu ya ku Asiriya! Nanga ife tidzapulumuka bwanji?’”
Dagiti agnanaed kadagitoy nga igid ti baybay ket ibagadanto iti dayta nga aldaw, 'Pudno, daytoy ti nagtaudan ti namnamatayo, a nagkamangantayo tapno maispaltayo manipud iti Ari ti Asiria, ket ita, kasanotayo ngay a makalibas?’”

< Yesaya 20 >