< Yesaya 20 >
1 Mʼchaka chimene mkulu wankhondo wotumidwa ndi mfumu ya ku Asiriya, anabwera ku Asidodi ndi kuwuthira nkhondo ndi kuwulanda,
L'année où Tartan s'avança sur Asdod, envoyé par Sargon, roi d'Assyrie, et où il assiégea et prit Asdod,
2 nthawi imeneyo Yehova anawuza Yesaya mwana wa Amozi kuti, “Pita kavule chiguduli ndi nsapato zako.” Ndipo iye anaterodi, ankangoyenda wamaliseche ndiponso wopanda nsapato.
en ce temps-là l'Éternel parla par l'intermédiaire d'Ésaïe, fils d'Amots, et dit: Va, et détache le cilice de tes reins, et ôte tes souliers de tes pieds. Et il fit ainsi, et alla sans manteau et nu-pieds.
3 Kenaka Yehova anati, “Monga momwe mtumiki wanga Yesaya wakhala akuyendera wamaliseche ndiponso wopanda nsapato kwa zaka zitatu ngati chizindikiro ndi chenjezo kwa dziko la Igupto ndi Kusi,
Alors l'Éternel dit: De même que mon serviteur Ésaïe va sans manteau et nu-pieds, pendant trois ans signe et présage pour l'Egypte et pour l'Éthiopie,
4 momwemonso mfumu ya ku Asiriya idzatenga ukapolo anthu a ku Igupto ndi a ku Kusi, anyamata ndi okalamba. Iwo adzakhala amaliseche ndi opanda nsapato, matako ali pa mtunda. Zimenezi zidzachititsa manyazi Igupto.
de même le roi d'Assyrie emmènera les captifs de l'Egypte et les captifs de l'Ethiopie, jeunes hommes et vieillards, sans manteau et nu-pieds et le dos découvert, opprobre pour l'Egypte.
5 Amene ankadalira Kusi, ndiponso amene ankadzitukumula chifukwa cha Igupto adzakhumudwa ndi kuchita manyazi.
Alors ils seront consternés, et auront honte de l'Ethiopie qui avait leur confiance, et de l'Egypte dont ils se glorifiaient.
6 Tsiku limenelo anthu amene amakhala mʼmbali mwa nyanja adzati, ‘Taonani zomwe zawachitikira amene ife tinkawadalira, amene ife tinkathawirako kuti atithandize ndi kutipulumutsa kwa mfumu ya ku Asiriya! Nanga ife tidzapulumuka bwanji?’”
Et les habitants de cette côte diront en ce jour: Voilà où en sont ceux qui avaient notre confiance, vers qui nous fuyions, pour être secourus, pour être délivrés du roi d'Assyrie! et nous, comment pourrions-nous échapper?