< Yesaya 20 >

1 Mʼchaka chimene mkulu wankhondo wotumidwa ndi mfumu ya ku Asiriya, anabwera ku Asidodi ndi kuwuthira nkhondo ndi kuwulanda,
In the year that Tharthan entered into Azotus, when Sargon the king of the Assyrians had sent him, and he had fought against Azotus, and had taken it:
2 nthawi imeneyo Yehova anawuza Yesaya mwana wa Amozi kuti, “Pita kavule chiguduli ndi nsapato zako.” Ndipo iye anaterodi, ankangoyenda wamaliseche ndiponso wopanda nsapato.
At that same time the Lord spoke by the hand of Isaias the son of Amos, saying: Go, and loose the sackcloth from off thy loins, and take off thy shoes from thy feet. And he did so, and went naked, and barefoot.
3 Kenaka Yehova anati, “Monga momwe mtumiki wanga Yesaya wakhala akuyendera wamaliseche ndiponso wopanda nsapato kwa zaka zitatu ngati chizindikiro ndi chenjezo kwa dziko la Igupto ndi Kusi,
And the Lord said: As my servant Isaias hath walked, naked and barefoot, it shall be a sign and a wonder of three years upon Egypt, and upon Ethiopia,
4 momwemonso mfumu ya ku Asiriya idzatenga ukapolo anthu a ku Igupto ndi a ku Kusi, anyamata ndi okalamba. Iwo adzakhala amaliseche ndi opanda nsapato, matako ali pa mtunda. Zimenezi zidzachititsa manyazi Igupto.
So shall the king of the Assyrians lead away the prisoners of Egypt, and the captivity of Ethiopia, young and old. naked and barefoot, with their buttocks uncovered to the shame of Egypt.
5 Amene ankadalira Kusi, ndiponso amene ankadzitukumula chifukwa cha Igupto adzakhumudwa ndi kuchita manyazi.
And they shall be afraid, and ashamed of Ethiopia their hope, and of Egypt their glory.
6 Tsiku limenelo anthu amene amakhala mʼmbali mwa nyanja adzati, ‘Taonani zomwe zawachitikira amene ife tinkawadalira, amene ife tinkathawirako kuti atithandize ndi kutipulumutsa kwa mfumu ya ku Asiriya! Nanga ife tidzapulumuka bwanji?’”
And the inhabitants of this isle shall say in that day: Lo this was our hope, to whom we fled for help, to deliver up from the face of the king of the Assyrians: and how shall we be able to escape?

< Yesaya 20 >