< Yesaya 20 >
1 Mʼchaka chimene mkulu wankhondo wotumidwa ndi mfumu ya ku Asiriya, anabwera ku Asidodi ndi kuwuthira nkhondo ndi kuwulanda,
Idet Aar, da Tartan kom til Asdod, der Sargon, Kongen af Assyrien, sendte ham, og han stred imod Asdod og indtog den,
2 nthawi imeneyo Yehova anawuza Yesaya mwana wa Amozi kuti, “Pita kavule chiguduli ndi nsapato zako.” Ndipo iye anaterodi, ankangoyenda wamaliseche ndiponso wopanda nsapato.
paa den Tid talte Herren ved Esajas, Amoz's Søn, og sagde: Gak hen, og løs Sørgedragten af dine Lænder, og drag din Sko af din Fod; og han gjorde saa og gik nøgen og barfodet.
3 Kenaka Yehova anati, “Monga momwe mtumiki wanga Yesaya wakhala akuyendera wamaliseche ndiponso wopanda nsapato kwa zaka zitatu ngati chizindikiro ndi chenjezo kwa dziko la Igupto ndi Kusi,
Da sagde Herren: Ligesom min Tjener Esajas har gaaet nøgen og barfodet i tre Aar, til et Tegn og Forbillede over Ægypten og over Morland,
4 momwemonso mfumu ya ku Asiriya idzatenga ukapolo anthu a ku Igupto ndi a ku Kusi, anyamata ndi okalamba. Iwo adzakhala amaliseche ndi opanda nsapato, matako ali pa mtunda. Zimenezi zidzachititsa manyazi Igupto.
saaledes skal Kongen af Assyrien bortføre Ægyptens fangne og Morianernes landflygtige, unge og gamle, som nøgne og blottede paa Bagdelen, Ægypterne til Blusel.
5 Amene ankadalira Kusi, ndiponso amene ankadzitukumula chifukwa cha Igupto adzakhumudwa ndi kuchita manyazi.
Og de skulle forfærdes og beskæmmes over Morland, som de saa op til, og over Ægypten, som var deres Stolthed.
6 Tsiku limenelo anthu amene amakhala mʼmbali mwa nyanja adzati, ‘Taonani zomwe zawachitikira amene ife tinkawadalira, amene ife tinkathawirako kuti atithandize ndi kutipulumutsa kwa mfumu ya ku Asiriya! Nanga ife tidzapulumuka bwanji?’”
Og den, som bor paa denne Strand, skal sige paa den Dag: Se, saa er det gaaet den, som vi saa op til, til hvem vi tyede om Hjælp for at fries fra Kongen af Assyrien; og vi, hvorledes skulle vi undkomme?