< Yesaya 20 >

1 Mʼchaka chimene mkulu wankhondo wotumidwa ndi mfumu ya ku Asiriya, anabwera ku Asidodi ndi kuwuthira nkhondo ndi kuwulanda,
Assyria lengpa Sargon in, a sepai jalam kaipa henga Philistine khopi Ashdod lo dinga thu apeh khum chun,
2 nthawi imeneyo Yehova anawuza Yesaya mwana wa Amozi kuti, “Pita kavule chiguduli ndi nsapato zako.” Ndipo iye anaterodi, ankangoyenda wamaliseche ndiponso wopanda nsapato.
Pakai in Amoz chapa Isaiah henga aseijin, “Na von chu sutlhan lang na kengchot teni jongchu koidoh in.” Isaiah in akisei bang chun abolin, sagoh keoleh kengkeo in avahlen ahi.
3 Kenaka Yehova anati, “Monga momwe mtumiki wanga Yesaya wakhala akuyendera wamaliseche ndiponso wopanda nsapato kwa zaka zitatu ngati chizindikiro ndi chenjezo kwa dziko la Igupto ndi Kusi,
Hichun Pakai in ahin seijin, “Ka sohpa Isaiah hi kumthum ahitai sagoh keo leh kengkeo va avalena hi. Hiche hi melchihna ahi-Egypt leh Ethiopia chunga hahsatna lentah kalhun sah ding vetsahna lim ahi.
4 momwemonso mfumu ya ku Asiriya idzatenga ukapolo anthu a ku Igupto ndi a ku Kusi, anyamata ndi okalamba. Iwo adzakhala amaliseche ndi opanda nsapato, matako ali pa mtunda. Zimenezi zidzachititsa manyazi Igupto.
Ajeh chu Assyria lengpan Egypt teleh Ethiopia te songkul tang dinga apui mang ding ahi. Sagoh keo leh kengchot beija avaleh sah ding, Egypt mite jumna dinga aneo alen atokeu uva alhat lesah ding ahi.
5 Amene ankadalira Kusi, ndiponso amene ankadzitukumula chifukwa cha Igupto adzakhumudwa ndi kuchita manyazi.
Chuteng Philistine te lung linglao a umdiu ahi. Ajehchu amahon Ethiopia thanei akisonpiu va, chuleh akisamkai piu Egypt a kiletsah piu ahi.
6 Tsiku limenelo anthu amene amakhala mʼmbali mwa nyanja adzati, ‘Taonani zomwe zawachitikira amene ife tinkawadalira, amene ife tinkathawirako kuti atithandize ndi kutipulumutsa kwa mfumu ya ku Asiriya! Nanga ife tidzapulumuka bwanji?’”
Hitia hi asei diu ahi, 'Hitobang hi Egypt te chunga ahunglhun theileh, eihon ipi agom kom phat inei diu ham? Assyria lengpa akona eihuhdoh dinguva Egypt te ina kisonpiu ahi.”

< Yesaya 20 >