< Yesaya 2 >

1 Nazi zinthu zokhudza Yuda ndi Yerusalemu, zimene Yesaya mwana wa Amozi anaziona mʼmasomphenya:
Слово, що його бачив Іса́я, син Амо́сів, про Юдею та про Єрусалим:
2 Mʼmasiku otsiriza, phiri la Nyumba ya Yehova adzalikhazikitsa kukhala lalitali kuposa mapiri ena onse, lidzaonekera pamwamba pa mapiri ena onse, ndipo mayiko onse adzathamangira kumeneko.
І ста́неться на кінці днів, мі́цно поста́влена буде гора́ дому Господнього на шпилі́ гір, і пі́днята буде вона понад згі́р'я, — і поли́нуть до неї всі люди.
3 Anthu ambiri adzabwera ndikunena kuti, “Tiyeni tikwere ku phiri la Yehova, ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo. Iye adzatiphunzitsa njira zake, ndipo tidzayenda mʼnjira zakezo.” Malangizo adzachokera ku Ziyoni, mawu a Yehova adzachokera ku Yerusalemu.
І пі́дуть числе́нні наро́ди та й скажуть: „Ходіть та збері́мось на го́ру Господню, до дому Бога Якового, і доріг Своїх Він нас навчи́ть, і ми пі́демо стежка́ми Його! Бо ви́йде з Сіону Зако́н, і слово Господнє — з Єрусалиму“.
4 Iye adzaweruza pakati pa mayiko, ndipo adzathetsa kusamvana pakati pa anthu ambiri. Anthuwo adzasandutsa malupanga awo kukhala makasu ndiponso mikondo yawo kukhala zomwetera. Mtundu wina sudzatenganso lupanga kumenyana ndi mtundu wina, kapena kuphunziranso za nkhondo.
І Він бу́де судити між лю́дьми, і буде числе́нні наро́ди розсу́джувати. І мечі́ свої перекую́ть вони на лемеші́, а списи́ свої — на серпи́. Не піді́йме меча народ проти наро́ду, і більше не бу́дуть навча́тись війни́!
5 Inu nyumba ya Yakobo, bwerani, tiyeni tiyende mʼkuwala kwa Yehova.
Доме Яковів, — ідіть, і попросту́ємо в світлі Господньому!
6 Inu Yehova mwawakana anthu anu, nyumba ya Yakobo. Iwo adzaza ndi zamatsenga zochokera Kummawa; amawombeza mawula ngati Afilisti, ndipo amayanjana ndi anthu osapembedza Mulungu.
Бо Ти був покинув наро́да Свого, дім Яковів, — бо по́вні безла́ддя зо схо́ду вони, та ворожби́тів, немов филисти́мляни, і наклада́ють із ді́тьми чужи́нців.
7 Dziko lawo ndi lodzaza ndi siliva ndi golide; ndipo chuma chawo ndi chosatha. Dziko lawo ndi lodzaza ndi akavalo; ndipo magaleta awo ankhondo ngosawerengeka.
І напо́внився край його срі́блом та золотом, — і немає кінця́ його ска́рбам. І напо́внився край його кі́ньми, — і немає кінця колесни́цям його́.
8 Dziko lawo ndi lodzaza ndi mafano; iwo amapembedza ntchito ya manja awo, amagwadira zomwe anapanga ndi zala zawo.
І напо́внився край його і́долами, — він кла́няється ділу рук своїх, тому́, що зробили були́ Його па́льці, —
9 Tsono munthu aliyense adzachepetsedwa ndi kutsitsidwa. Inu Yehova musawakhululukire.
і поклонилась люди́на, і чоловік упокори́вся. А Ти їм не дару́й!
10 Lowani mʼmatanthwe, bisalani mʼmaenje, kuthawa kuopsa kwa Yehova ndi ulemerero wa ufumu wake!
Іди в скелю, і сховайся у по́рох від стра́ху Господнього, і від пишноти́ Його ве́личі!
11 Kudzikuza kwa anthu kudzatha, ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa; Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu pa tsiku limenelo.
Горді о́чі люди́ни поникнуть, і буде обни́жена лю́дська високість, — і буде високим Сам тільки Госпо́дь того дня!
12 Yehova Wamphamvuzonse wakonzeratu tsiku limene adzatsitse onse onyada ndi odzitama, ndipo adzagonjetsa onse amphamvu,
Бо настане день Господа Савао́та на все горде й високе, і на все ви́сунене, — і пони́жене буде воно,
13 tsiku la mikungudza yonse ya ku Lebanoni, yayitali ndi yoonekera patali, ndiponso la mitengo yonse ya thundu ya ku Basani,
і на всі ке́дри лива́нські, високі та ви́сунені, і на всіля́кі баша́нські дуби́,
14 tsiku la mapiri onse ataliatali ndiponso la zitunda zonse zazitali,
і на всі го́ри високі, і на всі згір'я підне́сені,
15 tsiku la nsanja zonse zazitali ndiponso malinga onse olimba,
і на всі ба́шти високі, і на всі му́ри стрімкі,
16 tsiku la sitima zapamadzi zonse za ku Tarisisi ndiponso la mabwato onse okongola.
і на всі кораблі із Таршішу, і на все, на що ди́вимося пожадли́во!
17 Kudzikuza kwa munthu kudzatha ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa, Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu tsiku limenelo,
І пони́зиться гордість люди́ни, й обни́жена буде високість люде́й, — і буде високим Сам тільки Госпо́дь того дня,
18 ndipo mafano onse adzatheratu.
а бо́жища зо́всім ми́нуться!
19 Anthu adzathawira mʼmapanga a matanthwe ndi mʼmaenje a nthaka, kuthawa mkwiyo wa Yehova, ndiponso ulemerero wa ufumu wake, pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.
І вони пі́дуть до ске́льних пече́р та до по́роху в ями від стра́ху Господнього і від пишноти́ Його ве́личі, коли при́йде Він о́страх збудити на землі!
20 Tsiku limenelo anthu adzatayira mfuko ndi mileme mafano awo asiliva ndi mafano awo agolide, amene anawapanga kuti aziwapembedza.
Покине люди́на того дня божкі́в своїх срібних і божкі́в своїх золотих, що собі нароби́ла була́, щоб вклоня́тись крота́м і кажана́м,
21 Adzathawira mʼmapanga a matanthwe ndiponso mʼmingʼalu ya nthaka kuthawa mkwiyo wa Yehova ndiponso ulemerero wa ufumu wake, pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.
щоб піти у пече́ри й розщілини ске́льні від стра́ху Господнього і від слави вели́ччя Його́, коли при́йде Він о́страх збуди́ти на землі!
22 Lekani kudalira munthu, amene moyo wake sukhalira kutha. Iye angathandize bwanji wina aliyense?
Відки́нься ж собі від люди́ни, що ві́ддих у носі її, бо за́що її поважа́ти?

< Yesaya 2 >