< Yesaya 2 >

1 Nazi zinthu zokhudza Yuda ndi Yerusalemu, zimene Yesaya mwana wa Amozi anaziona mʼmasomphenya:
Beseda, ki jo je Izaija, Amócov sin, videl glede Juda in Jeruzalema.
2 Mʼmasiku otsiriza, phiri la Nyumba ya Yehova adzalikhazikitsa kukhala lalitali kuposa mapiri ena onse, lidzaonekera pamwamba pa mapiri ena onse, ndipo mayiko onse adzathamangira kumeneko.
Zgodilo se bo v poslednjih dneh, da bo gora Gospodove hiše osnovana na vrhu gora in povišana bo nad hribe. In vsi narodi se bodo stekali k njej.
3 Anthu ambiri adzabwera ndikunena kuti, “Tiyeni tikwere ku phiri la Yehova, ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo. Iye adzatiphunzitsa njira zake, ndipo tidzayenda mʼnjira zakezo.” Malangizo adzachokera ku Ziyoni, mawu a Yehova adzachokera ku Yerusalemu.
Mnogo ljudstva bo šlo in reklo: »Pridite in pojdimo gor na Gospodovo goro, k hiši Jakobovega Boga. Učil nas bo svojih poti in hodili bomo po njegovih stezah, kajti iz Siona bo izšla postava in Gospodova beseda iz Jeruzalema.«
4 Iye adzaweruza pakati pa mayiko, ndipo adzathetsa kusamvana pakati pa anthu ambiri. Anthuwo adzasandutsa malupanga awo kukhala makasu ndiponso mikondo yawo kukhala zomwetera. Mtundu wina sudzatenganso lupanga kumenyana ndi mtundu wina, kapena kuphunziranso za nkhondo.
Sodil bo med narodi, oštel bo mnoga ljudstva. Svoje meče bodo prekovali v lemeže in svoje sulice v obrezovalne kavlje. Narod ne bo vzdignil meča zoper narod niti se ne bodo več učili bojevanja.
5 Inu nyumba ya Yakobo, bwerani, tiyeni tiyende mʼkuwala kwa Yehova.
Oh Jakobova hiša, pridite in hodímo v Gospodovi svetlobi.
6 Inu Yehova mwawakana anthu anu, nyumba ya Yakobo. Iwo adzaza ndi zamatsenga zochokera Kummawa; amawombeza mawula ngati Afilisti, ndipo amayanjana ndi anthu osapembedza Mulungu.
Zatorej si zapustil svoje ljudstvo, Jakobovo hišo, ker so bili izpolnjeni od vzhoda in so napovedovalci usode kakor Filistejci in sebi ugajajo v otrocih tujcev.
7 Dziko lawo ndi lodzaza ndi siliva ndi golide; ndipo chuma chawo ndi chosatha. Dziko lawo ndi lodzaza ndi akavalo; ndipo magaleta awo ankhondo ngosawerengeka.
Njihova dežela je polna srebra in zlata niti tam ni konca njihovih zakladov. Njihova dežela je polna konj niti tam ni konca njihovih bojnih voz.
8 Dziko lawo ndi lodzaza ndi mafano; iwo amapembedza ntchito ya manja awo, amagwadira zomwe anapanga ndi zala zawo.
Njihova dežela je polna malikov, obožujejo delo svojih lastnih rok, to, kar so naredili njihovi lastni prsti.
9 Tsono munthu aliyense adzachepetsedwa ndi kutsitsidwa. Inu Yehova musawakhululukire.
Zloben človek se priklanja in velik človek se ponižuje, zato jim ne odpusti.
10 Lowani mʼmatanthwe, bisalani mʼmaenje, kuthawa kuopsa kwa Yehova ndi ulemerero wa ufumu wake!
Vstopi v skalo in se skrij v prahu zaradi strahu pred Gospodom in zaradi slave njegovega veličanstva.
11 Kudzikuza kwa anthu kudzatha, ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa; Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu pa tsiku limenelo.
Človekovi vzvišeni pogledi bodo ponižani in oholost ljudi bo upognjena in sam Gospod bo na ta dan povišan.
12 Yehova Wamphamvuzonse wakonzeratu tsiku limene adzatsitse onse onyada ndi odzitama, ndipo adzagonjetsa onse amphamvu,
Kajti dan Gospoda nad bojevniki bo nad vsakim, ki je ponosen in vzvišen in nad vsakim, ki je povzdignjen, in ta bo ponižan;
13 tsiku la mikungudza yonse ya ku Lebanoni, yayitali ndi yoonekera patali, ndiponso la mitengo yonse ya thundu ya ku Basani,
in nad vsemi libanonskimi cedrami, ki so visoke in povzdignjene in nad vsemi bašánskimi hrasti
14 tsiku la mapiri onse ataliatali ndiponso la zitunda zonse zazitali,
in nad vsemi visokimi gorami in nad vsemi hribi, ki so povzdignjeni,
15 tsiku la nsanja zonse zazitali ndiponso malinga onse olimba,
in nad vsakim visokim stolpom in nad vsakim utrjenim zidom,
16 tsiku la sitima zapamadzi zonse za ku Tarisisi ndiponso la mabwato onse okongola.
in na vseh ladjah iz Taršíša in na vseh prijetnih slikah.
17 Kudzikuza kwa munthu kudzatha ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa, Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu tsiku limenelo,
Nadutost človeka bo upognjena in oholost ljudi bo ponižana. Samo Gospod bo povišan na ta dan.
18 ndipo mafano onse adzatheratu.
Malike bo popolnoma odpravil.
19 Anthu adzathawira mʼmapanga a matanthwe ndi mʼmaenje a nthaka, kuthawa mkwiyo wa Yehova, ndiponso ulemerero wa ufumu wake, pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.
Šli bodo v skalne luknje in v zemeljske votline zaradi strahu pred Gospodom in zaradi slave njegovega veličanstva, ko se on vzdiguje, da strašno strese zemljo.
20 Tsiku limenelo anthu adzatayira mfuko ndi mileme mafano awo asiliva ndi mafano awo agolide, amene anawapanga kuti aziwapembedza.
Na tisti dan bo človek vrgel svoje malike iz srebra in svoje malike iz zlata, ki so si jih naredili, vsakdo za oboževanje, krtom in netopirjem,
21 Adzathawira mʼmapanga a matanthwe ndiponso mʼmingʼalu ya nthaka kuthawa mkwiyo wa Yehova ndiponso ulemerero wa ufumu wake, pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.
da bo šel v skalne razpoke in na vrhove razdrapanih skal, zaradi strahu pred Gospodom in zaradi slave njegovega veličanstva, ko se bo vzdigoval, da strašno strese zemljo.
22 Lekani kudalira munthu, amene moyo wake sukhalira kutha. Iye angathandize bwanji wina aliyense?
Odvrnite se od človeka, katerega dih je v njegovih nosnicah, kajti v čem je ta cenjen?

< Yesaya 2 >