< Yesaya 2 >

1 Nazi zinthu zokhudza Yuda ndi Yerusalemu, zimene Yesaya mwana wa Amozi anaziona mʼmasomphenya:
KA olelo i hoikeia mai ia Isaia, ke keiki a Amosa, no ka Iuda, a me ko Ierusalema.
2 Mʼmasiku otsiriza, phiri la Nyumba ya Yehova adzalikhazikitsa kukhala lalitali kuposa mapiri ena onse, lidzaonekera pamwamba pa mapiri ena onse, ndipo mayiko onse adzathamangira kumeneko.
E hiki mai no keia i na la mahope, E kukulu paa ia ka puu o ka hale o Iehova maluna o na mauna, A e hookiekieia maluna o na puu; A e holo no iloko ona na lahuikanaka a pau.
3 Anthu ambiri adzabwera ndikunena kuti, “Tiyeni tikwere ku phiri la Yehova, ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo. Iye adzatiphunzitsa njira zake, ndipo tidzayenda mʼnjira zakezo.” Malangizo adzachokera ku Ziyoni, mawu a Yehova adzachokera ku Yerusalemu.
A e nui loa na kanaka e hele me ka olelo, E hele mai e pii kakou i ka mauna o Iehova, I ka hale hoi o ke Akua o Iakoba; Nana no e ao mai ia kakou i kona mau aoao, I hele ai kakou ma kona mau alanui. No ka mea, mai Ziona aku e laha aku ai ke kanawai, A o ka olelo a Iehova hoi, mai Ierusalema aku.
4 Iye adzaweruza pakati pa mayiko, ndipo adzathetsa kusamvana pakati pa anthu ambiri. Anthuwo adzasandutsa malupanga awo kukhala makasu ndiponso mikondo yawo kukhala zomwetera. Mtundu wina sudzatenganso lupanga kumenyana ndi mtundu wina, kapena kuphunziranso za nkhondo.
Nana no e hooponopono mawaena o ko na aina, E ao mai hoi i na lahuikanaka he nui loa. E kui lakou i ko lakou mau pahikaua i oo palau, A me ko lakou mau ihe hoi, i pahi paipai; Aole e hapai ko kekahi aina i ka pahikaua, e ka e i ko kekahi aina, Aole hoi lakou e ao hou i ke kaua.
5 Inu nyumba ya Yakobo, bwerani, tiyeni tiyende mʼkuwala kwa Yehova.
E ko ka hale o Iehova, e hele mai, E hele kakou ma ka malamalama o Iehova.
6 Inu Yehova mwawakana anthu anu, nyumba ya Yakobo. Iwo adzaza ndi zamatsenga zochokera Kummawa; amawombeza mawula ngati Afilisti, ndipo amayanjana ndi anthu osapembedza Mulungu.
He oiaio no, ua haalele oe i kou poe kanaka, I ko ka hale hoi o Iakoba; No ka mea, ua piha lakou i na mea mai ka hikina mai, I ka poe nana ao, e like me ko Pilisetia: A launa no hoi lakou i na keiki a na malihini.
7 Dziko lawo ndi lodzaza ndi siliva ndi golide; ndipo chuma chawo ndi chosatha. Dziko lawo ndi lodzaza ndi akavalo; ndipo magaleta awo ankhondo ngosawerengeka.
Ua piha ko lakou aina i ke kala, a me ke gula, Aole e pau i ka heluia ko lakou waiwai; Ua piha hoi ko lakou aina i na lio, Aole e pau i ka heluia na kaakaua o lakou.
8 Dziko lawo ndi lodzaza ndi mafano; iwo amapembedza ntchito ya manja awo, amagwadira zomwe anapanga ndi zala zawo.
Ua piha ko lakou aina i na'kua lapuwale; Kulou no lakou ilalo imua o ka hana a ko lakou mau lima, Imua hoi o ka mea a ko lakou mau manamana lima i hana'i.
9 Tsono munthu aliyense adzachepetsedwa ndi kutsitsidwa. Inu Yehova musawakhululukire.
Nolaila, e kulou no ke kanaka uuku, E hoohaahaaia no hoi ke kanaka nui; Aole nae oe e kala mai ia lakou.
10 Lowani mʼmatanthwe, bisalani mʼmaenje, kuthawa kuopsa kwa Yehova ndi ulemerero wa ufumu wake!
E komo oe iloko o ka pohaku, e pee hoi iloko o ka lepo, No ka makau ia Iehova, a no ka nani hoi o kona hanohano.
11 Kudzikuza kwa anthu kudzatha, ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa; Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu pa tsiku limenelo.
E kulou auanei na maka kiekie o kanaka, A e hoohaahaaia ko kanaka lana haakei, O Iehova wale no ke hookiekieia i kela la.
12 Yehova Wamphamvuzonse wakonzeratu tsiku limene adzatsitse onse onyada ndi odzitama, ndipo adzagonjetsa onse amphamvu,
E kau mai no ka la o Iehova o na kaua, Maluna o na mea hanohano a kehakeha a pau, Maluna hoi o kela mea keia mea i hookiekieia, a e hoohaahaaia no oia;
13 tsiku la mikungudza yonse ya ku Lebanoni, yayitali ndi yoonekera patali, ndiponso la mitengo yonse ya thundu ya ku Basani,
Maluna o na laau kedera a pau o Lebanona, na mea loloa a kiekie, A maluna hoi o na laau oka a pau o Basana;
14 tsiku la mapiri onse ataliatali ndiponso la zitunda zonse zazitali,
Maluna o na kuahiwi kiekie a pau, A me na puu a pau i hookiekieia:
15 tsiku la nsanja zonse zazitali ndiponso malinga onse olimba,
Maluna o na halekiai kiekie a pau, A me na pa kaua kiekie a pau:
16 tsiku la sitima zapamadzi zonse za ku Tarisisi ndiponso la mabwato onse okongola.
Maluna o na moku a pau o Taresisa, A me na mea milimili a pau i mahaloia.
17 Kudzikuza kwa munthu kudzatha ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa, Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu tsiku limenelo,
E kulou no ilalo ko ke kanaka haaheo, E hoohaahaaia hoi ka manao kiekie o ke kanaka; O Iehova wale no ke hookiekieia i kela la.
18 ndipo mafano onse adzatheratu.
A e nalowale loa na akua lapuwale.
19 Anthu adzathawira mʼmapanga a matanthwe ndi mʼmaenje a nthaka, kuthawa mkwiyo wa Yehova, ndiponso ulemerero wa ufumu wake, pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.
E komo hoi na kanaka iloko o na ana pohaku a me na lua o ka lepo, No ka makau ia Iehova, a no ka nani hoi o kona hanohano. Ia ia e ku ai iluna, e hoonaueue ai i ka honua.
20 Tsiku limenelo anthu adzatayira mfuko ndi mileme mafano awo asiliva ndi mafano awo agolide, amene anawapanga kuti aziwapembedza.
Ia la la e kiola aku no ke kanaka i kona mau akua kala, A me kona mau akua gula, ana i hana'i i mea hoomana, E lilo i na iole a me na opeapea.
21 Adzathawira mʼmapanga a matanthwe ndiponso mʼmingʼalu ya nthaka kuthawa mkwiyo wa Yehova ndiponso ulemerero wa ufumu wake, pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.
A hele lakou iloko o na ana pohaku, Iloko hoi o na lua ma ka pali paa, No ka makau ia Iehova, A no ka nani hoi o kona hanohano, Ia ia e ku ai iluna e hoonaueue ai i ka honua.
22 Lekani kudalira munthu, amene moyo wake sukhalira kutha. Iye angathandize bwanji wina aliyense?
Mai hilinai aku oukou i ke kanaka, Nona ka hanu ma kona mau pukaihu, No ka mea, heaha ia, i manaoia'i oia?

< Yesaya 2 >