< Yesaya 2 >

1 Nazi zinthu zokhudza Yuda ndi Yerusalemu, zimene Yesaya mwana wa Amozi anaziona mʼmasomphenya:
Parole qu’a vue Isaïe, fils d’Amos, touchant Juda et Jérusalem.
2 Mʼmasiku otsiriza, phiri la Nyumba ya Yehova adzalikhazikitsa kukhala lalitali kuposa mapiri ena onse, lidzaonekera pamwamba pa mapiri ena onse, ndipo mayiko onse adzathamangira kumeneko.
Et il arrivera dans les derniers jours que la montagne préparée pour la demeure du Seigneur sera établie sur le sommet des montagnes, et elle sera élevée au-dessus des collines, et tous les peuples y afflueront.
3 Anthu ambiri adzabwera ndikunena kuti, “Tiyeni tikwere ku phiri la Yehova, ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo. Iye adzatiphunzitsa njira zake, ndipo tidzayenda mʼnjira zakezo.” Malangizo adzachokera ku Ziyoni, mawu a Yehova adzachokera ku Yerusalemu.
Et beaucoup de peuples iront et diront: Venez, et montons à la montagne du Seigneur, et à la maison du Dieu de Jacob, et il nous enseignera ses voies, et nous marcherons dans ses sentiers; parce que de Sion sortira la loi, et la parole du Seigneur de Jérusalem.
4 Iye adzaweruza pakati pa mayiko, ndipo adzathetsa kusamvana pakati pa anthu ambiri. Anthuwo adzasandutsa malupanga awo kukhala makasu ndiponso mikondo yawo kukhala zomwetera. Mtundu wina sudzatenganso lupanga kumenyana ndi mtundu wina, kapena kuphunziranso za nkhondo.
Et il jugera les nations, et il convaincra beaucoup de peuples; et de leurs glaives ils forgeront des socs de charrue, et de leurs lances des faux; une nation ne lèvera pas le glaive contre une autre nation, elles ne s’exerceront plus au combat.
5 Inu nyumba ya Yakobo, bwerani, tiyeni tiyende mʼkuwala kwa Yehova.
Maison de Jacob, venez, et marchons à la lumière du Seigneur.
6 Inu Yehova mwawakana anthu anu, nyumba ya Yakobo. Iwo adzaza ndi zamatsenga zochokera Kummawa; amawombeza mawula ngati Afilisti, ndipo amayanjana ndi anthu osapembedza Mulungu.
Car vous avez rejeté votre peuple, la maison de Jacob; parce qu’ils ont été remplis comme autrefois, qu’ils ont eu des augures comme les Philistins, et qu’ils se sont attachés à des enfants étrangers.
7 Dziko lawo ndi lodzaza ndi siliva ndi golide; ndipo chuma chawo ndi chosatha. Dziko lawo ndi lodzaza ndi akavalo; ndipo magaleta awo ankhondo ngosawerengeka.
Sa terre est remplie d’argent et d’or; et il n’y a pas de bornes à ses trésors;
8 Dziko lawo ndi lodzaza ndi mafano; iwo amapembedza ntchito ya manja awo, amagwadira zomwe anapanga ndi zala zawo.
Et sa terre est remplie de chevaux, et ses quadriges sont innombrables. Et sa terre est remplie d’idoles; ils ont adoré l’ouvrage de leurs mains, l’ouvrage qu’ont fait leurs doigts.
9 Tsono munthu aliyense adzachepetsedwa ndi kutsitsidwa. Inu Yehova musawakhululukire.
Et l’homme du peuple s’est courbé, et l’homme de condition est humilié; ne leur pardonnez donc point.
10 Lowani mʼmatanthwe, bisalani mʼmaenje, kuthawa kuopsa kwa Yehova ndi ulemerero wa ufumu wake!
Entre dans la pierre, et cache-toi dans les creux de la terre, par la crainte du Seigneur et de la gloire de sa majesté.
11 Kudzikuza kwa anthu kudzatha, ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa; Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu pa tsiku limenelo.
Les yeux altiers de l’homme du peuple ont été humiliés, et la fierté des hommes de condition sera abaissée; mais le Seigneur seul sera exalté en ce jour-là.
12 Yehova Wamphamvuzonse wakonzeratu tsiku limene adzatsitse onse onyada ndi odzitama, ndipo adzagonjetsa onse amphamvu,
Parce que le jour du Seigneur des armées éclatera sur tout esprit superbe et hautain et sur tout arrogant; et ils seront humiliés;
13 tsiku la mikungudza yonse ya ku Lebanoni, yayitali ndi yoonekera patali, ndiponso la mitengo yonse ya thundu ya ku Basani,
Et sur tous les cèdres du Liban, grands et élevés, et sur tous les chênes de Basan;
14 tsiku la mapiri onse ataliatali ndiponso la zitunda zonse zazitali,
Et sur toutes les montagnes les plus hautes, et sur toutes les collines les plus élevées;
15 tsiku la nsanja zonse zazitali ndiponso malinga onse olimba,
Et sur toute tour la plus élevée et sur toute muraille fortifiée;
16 tsiku la sitima zapamadzi zonse za ku Tarisisi ndiponso la mabwato onse okongola.
Et sur tous les vaisseaux de Tharsis, et sur tout ce qui est beau à voir.
17 Kudzikuza kwa munthu kudzatha ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa, Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu tsiku limenelo,
Et l’orgueil des hommes du peuple sera abaissé, et la hauteur des hommes de condition sera humiliée, et le Seigneur seul sera élevé en ce jour-là;
18 ndipo mafano onse adzatheratu.
Et les idoles seront entièrement brisées;
19 Anthu adzathawira mʼmapanga a matanthwe ndi mʼmaenje a nthaka, kuthawa mkwiyo wa Yehova, ndiponso ulemerero wa ufumu wake, pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.
Et ils entreront dans les creux des rochers, dans les antres de la terre, par la frayeur du Seigneur, et à cause de la gloire de sa majesté, lorsqu’il se lèvera pour frapper la terre.
20 Tsiku limenelo anthu adzatayira mfuko ndi mileme mafano awo asiliva ndi mafano awo agolide, amene anawapanga kuti aziwapembedza.
En ce jour-là l’homme rejettera ses idoles d’argent et ses simulacres d’or, qu’il s’était faits pour les adorer, les taupes et les chauves-souris.
21 Adzathawira mʼmapanga a matanthwe ndiponso mʼmingʼalu ya nthaka kuthawa mkwiyo wa Yehova ndiponso ulemerero wa ufumu wake, pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.
Et il entrera dans les fentes des pierres, et dans les cavernes des roches par la frayeur du Seigneur, et à cause de la gloire de sa majesté, lorsqu’il se lèvera pour frapper la terre.
22 Lekani kudalira munthu, amene moyo wake sukhalira kutha. Iye angathandize bwanji wina aliyense?
Laissez donc l’homme dont le souffle est dans ses narines, parce qu’il a été réputé pour le Très-Haut.

< Yesaya 2 >