< Yesaya 2 >
1 Nazi zinthu zokhudza Yuda ndi Yerusalemu, zimene Yesaya mwana wa Amozi anaziona mʼmasomphenya:
Sana, jonka Jesaja, Aamoksen poika, näki Juudasta ja Jerusalemista.
2 Mʼmasiku otsiriza, phiri la Nyumba ya Yehova adzalikhazikitsa kukhala lalitali kuposa mapiri ena onse, lidzaonekera pamwamba pa mapiri ena onse, ndipo mayiko onse adzathamangira kumeneko.
Aikojen lopussa on Herran temppelin vuori seisova vahvana, ylimmäisenä vuorista, kukkuloista korkeimpana, ja kaikki pakanakansat virtaavat sinne.
3 Anthu ambiri adzabwera ndikunena kuti, “Tiyeni tikwere ku phiri la Yehova, ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo. Iye adzatiphunzitsa njira zake, ndipo tidzayenda mʼnjira zakezo.” Malangizo adzachokera ku Ziyoni, mawu a Yehova adzachokera ku Yerusalemu.
Monet kansat lähtevät liikkeelle sanoen: "Tulkaa, nouskaamme Herran vuorelle, Jaakobin Jumalan temppeliin, että hän opettaisi meille teitänsä ja me vaeltaisimme hänen polkujansa; sillä Siionista lähtee laki, Jerusalemista Herran sana".
4 Iye adzaweruza pakati pa mayiko, ndipo adzathetsa kusamvana pakati pa anthu ambiri. Anthuwo adzasandutsa malupanga awo kukhala makasu ndiponso mikondo yawo kukhala zomwetera. Mtundu wina sudzatenganso lupanga kumenyana ndi mtundu wina, kapena kuphunziranso za nkhondo.
Ja hän tuomitsee pakanakansojen kesken, säätää oikeutta monille kansoille. Niin he takovat miekkansa vantaiksi ja keihäänsä vesureiksi; kansa ei nosta miekkaa kansaa vastaan, eivätkä he enää opettele sotimaan.
5 Inu nyumba ya Yakobo, bwerani, tiyeni tiyende mʼkuwala kwa Yehova.
Jaakobin heimo, tulkaa, vaeltakaamme Herran valkeudessa.
6 Inu Yehova mwawakana anthu anu, nyumba ya Yakobo. Iwo adzaza ndi zamatsenga zochokera Kummawa; amawombeza mawula ngati Afilisti, ndipo amayanjana ndi anthu osapembedza Mulungu.
Sillä sinä olet hyljännyt kansasi, Jaakobin heimon, koska he ovat täynnä Idän menoa, täynnä ennustelijoita niinkuin filistealaiset, ja lyövät kättä muukalaisten kanssa.
7 Dziko lawo ndi lodzaza ndi siliva ndi golide; ndipo chuma chawo ndi chosatha. Dziko lawo ndi lodzaza ndi akavalo; ndipo magaleta awo ankhondo ngosawerengeka.
Heidän maansa tuli täyteen hopeata ja kultaa, eikä heidän aarteillaan ole määrää; heidän maansa tuli täyteen hevosia, eikä heidän vaunuillaan ole määrää.
8 Dziko lawo ndi lodzaza ndi mafano; iwo amapembedza ntchito ya manja awo, amagwadira zomwe anapanga ndi zala zawo.
Heidän maansa tuli täyteen epäjumalia, he kumartavat kättensä tekoa, sitä, minkä heidän sormensa ovat tehneet.
9 Tsono munthu aliyense adzachepetsedwa ndi kutsitsidwa. Inu Yehova musawakhululukire.
Silloin ihminen masentuu ja mies painuu maahan, mutta älä anna heille anteeksi.
10 Lowani mʼmatanthwe, bisalani mʼmaenje, kuthawa kuopsa kwa Yehova ndi ulemerero wa ufumu wake!
Mene kallion kätköön, piiloudu maan peittoon Herran kauhua ja hänen valtansa kirkkautta pakoon.
11 Kudzikuza kwa anthu kudzatha, ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa; Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu pa tsiku limenelo.
Ihmisten ylpeät silmät painuvat maahan, miesten korskeus masentuu, ja sinä päivänä Herra yksinänsä on korkea.
12 Yehova Wamphamvuzonse wakonzeratu tsiku limene adzatsitse onse onyada ndi odzitama, ndipo adzagonjetsa onse amphamvu,
Sillä Herran Sebaotin päivä kohtaa kaikkea ylpeää ja korskeata ja kaikkea ylhäistä, niin että se maahan painuu,
13 tsiku la mikungudza yonse ya ku Lebanoni, yayitali ndi yoonekera patali, ndiponso la mitengo yonse ya thundu ya ku Basani,
kaikkia Libanonin setripuita, noita korkeita ja ylhäisiä, kaikkia Baasanin tammia,
14 tsiku la mapiri onse ataliatali ndiponso la zitunda zonse zazitali,
kaikkia korkeita vuoria ja kaikkia ylhäisiä kukkuloita,
15 tsiku la nsanja zonse zazitali ndiponso malinga onse olimba,
kaikkia korkeita torneja ja kaikkia vahvoja muureja,
16 tsiku la sitima zapamadzi zonse za ku Tarisisi ndiponso la mabwato onse okongola.
kaikkia Tarsiin-laivoja ja kaikkea kallista ja ihanaa.
17 Kudzikuza kwa munthu kudzatha ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa, Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu tsiku limenelo,
Silloin masentuu ihmisten ylpeys, ja miesten korskeus painuu maahan, ja sinä päivänä Herra yksinänsä on korkea.
18 ndipo mafano onse adzatheratu.
Mutta epäjumalat katoavat kaikki tyynni.
19 Anthu adzathawira mʼmapanga a matanthwe ndi mʼmaenje a nthaka, kuthawa mkwiyo wa Yehova, ndiponso ulemerero wa ufumu wake, pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.
Silloin mennään kallioluoliin ja maakuoppiin Herran kauhua ja hänen valtansa kirkkautta pakoon, kun hän nousee maata kauhistuttamaan.
20 Tsiku limenelo anthu adzatayira mfuko ndi mileme mafano awo asiliva ndi mafano awo agolide, amene anawapanga kuti aziwapembedza.
Sinä päivänä ihmiset viskaavat pois myyrille ja yököille hopea-ja kultajumalansa, jotka he ovat tehneet kumarrettaviksensa.
21 Adzathawira mʼmapanga a matanthwe ndiponso mʼmingʼalu ya nthaka kuthawa mkwiyo wa Yehova ndiponso ulemerero wa ufumu wake, pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.
Ja he menevät vuorenrotkoihin ja kallionkoloihin Herran kauhua ja hänen valtansa kirkkautta pakoon, kun hän nousee maata kauhistuttamaan.
22 Lekani kudalira munthu, amene moyo wake sukhalira kutha. Iye angathandize bwanji wina aliyense?
Luopukaa siis ihmisistä, joilla on vain henkäys sieraimissa, sillä minkä arvoiset he ovat!