< Yesaya 2 >

1 Nazi zinthu zokhudza Yuda ndi Yerusalemu, zimene Yesaya mwana wa Amozi anaziona mʼmasomphenya:
The word which he saw Isaiah [the] son of Amoz on Judah and Jerusalem.
2 Mʼmasiku otsiriza, phiri la Nyumba ya Yehova adzalikhazikitsa kukhala lalitali kuposa mapiri ena onse, lidzaonekera pamwamba pa mapiri ena onse, ndipo mayiko onse adzathamangira kumeneko.
And it will be - at [the] end of the days established it will be [the] mountain of [the] house of Yahweh [the] chief of the mountains and lifted up more than [the] hills and they will stream to it all the nations.
3 Anthu ambiri adzabwera ndikunena kuti, “Tiyeni tikwere ku phiri la Yehova, ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo. Iye adzatiphunzitsa njira zake, ndipo tidzayenda mʼnjira zakezo.” Malangizo adzachokera ku Ziyoni, mawu a Yehova adzachokera ku Yerusalemu.
And they will come peoples many and they will say come - so we may go up to [the] mountain of Yahweh to [the] house of [the] God of Jacob so he may teach us of ways his so we may walk in paths his for from Zion it will go forth instruction and [the] word of Yahweh from Jerusalem.
4 Iye adzaweruza pakati pa mayiko, ndipo adzathetsa kusamvana pakati pa anthu ambiri. Anthuwo adzasandutsa malupanga awo kukhala makasu ndiponso mikondo yawo kukhala zomwetera. Mtundu wina sudzatenganso lupanga kumenyana ndi mtundu wina, kapena kuphunziranso za nkhondo.
And he will judge between the nations and he will decide for peoples many and they will beat swords their plowshares and spears their pruning knives not it will lift up nation against nation sword and not they will learn again warfare.
5 Inu nyumba ya Yakobo, bwerani, tiyeni tiyende mʼkuwala kwa Yehova.
O house of Jacob come so let us walk in [the] light of Yahweh.
6 Inu Yehova mwawakana anthu anu, nyumba ya Yakobo. Iwo adzaza ndi zamatsenga zochokera Kummawa; amawombeza mawula ngati Afilisti, ndipo amayanjana ndi anthu osapembedza Mulungu.
For you have abandoned people your [the] house of Jacob for they are full from [the] east and soothsayers like the Philistines and with [the] children of foreigners they clap hands.
7 Dziko lawo ndi lodzaza ndi siliva ndi golide; ndipo chuma chawo ndi chosatha. Dziko lawo ndi lodzaza ndi akavalo; ndipo magaleta awo ankhondo ngosawerengeka.
And it has been filled land its silver and gold and there not [is] an end to treasures its and it has been filled land its horses and there not [is] an end to chariots its.
8 Dziko lawo ndi lodzaza ndi mafano; iwo amapembedza ntchito ya manja awo, amagwadira zomwe anapanga ndi zala zawo.
And it has been filled land its idols to [the] work of hands his they bow down to [that] which they have made fingers his.
9 Tsono munthu aliyense adzachepetsedwa ndi kutsitsidwa. Inu Yehova musawakhululukire.
And he has been humbled everyone and he has become low everyone and may not you forgive them.
10 Lowani mʼmatanthwe, bisalani mʼmaenje, kuthawa kuopsa kwa Yehova ndi ulemerero wa ufumu wake!
Go in the rock and hide yourself in the dust from before [the] dread of Yahweh and from [the] splendor of majesty his.
11 Kudzikuza kwa anthu kudzatha, ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa; Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu pa tsiku limenelo.
Eyes of haughtiness of a person it will become low and it will be humbled [the] pride of people and he will be exalted Yahweh to only him in the day that.
12 Yehova Wamphamvuzonse wakonzeratu tsiku limene adzatsitse onse onyada ndi odzitama, ndipo adzagonjetsa onse amphamvu,
For a day [belongs] to Yahweh of hosts on every proud [thing] and lofty [thing] and on every [thing] lifted up and [it will be] low.
13 tsiku la mikungudza yonse ya ku Lebanoni, yayitali ndi yoonekera patali, ndiponso la mitengo yonse ya thundu ya ku Basani,
And on all [the] cedars of Lebanon that are lofty and which are lifted up and on all [the] oaks of Bashan.
14 tsiku la mapiri onse ataliatali ndiponso la zitunda zonse zazitali,
And on all the mountains that are lofty and on all the hills that are lifted up.
15 tsiku la nsanja zonse zazitali ndiponso malinga onse olimba,
And on every tower high and on every wall fortified.
16 tsiku la sitima zapamadzi zonse za ku Tarisisi ndiponso la mabwato onse okongola.
And on all [the] ships of Tarshish and on all [the] ships of desire.
17 Kudzikuza kwa munthu kudzatha ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa, Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu tsiku limenelo,
And it will be humbled [the] haughtiness of humankind and it will become low [the] pride of people and he will be exalted Yahweh to only him in the day that.
18 ndipo mafano onse adzatheratu.
And the idols completely it will pass away.
19 Anthu adzathawira mʼmapanga a matanthwe ndi mʼmaenje a nthaka, kuthawa mkwiyo wa Yehova, ndiponso ulemerero wa ufumu wake, pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.
And people will go in caves of [the] rocks and in holes of [the] ground from before [the] dread of Yahweh and from [the] splendor of majesty his when arises he to terrify the earth.
20 Tsiku limenelo anthu adzatayira mfuko ndi mileme mafano awo asiliva ndi mafano awo agolide, amene anawapanga kuti aziwapembedza.
In the day that it will throw away humankind [the] idols of silver its and [the] idols of gold its which they made for himself to bow down to [the] digging of moles and to the bats.
21 Adzathawira mʼmapanga a matanthwe ndiponso mʼmingʼalu ya nthaka kuthawa mkwiyo wa Yehova ndiponso ulemerero wa ufumu wake, pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.
To go in [the] crevices of the rocks and in [the] clefts of the cliffs from before [the] dread of Yahweh and from [the] splendor of majesty his when arises he to terrify the earth.
22 Lekani kudalira munthu, amene moyo wake sukhalira kutha. Iye angathandize bwanji wina aliyense?
Cease yourselves from humankind whom breath [is] in nostril[s] his for how? to be accounted [is] he.

< Yesaya 2 >