< Yesaya 19 >
1 Uthenga onena za Igupto: Taonani, Yehova wakwera pa mtambo waliwiro, ndipo akupita ku Igupto. Mafano a ku Igupto akunjenjemera pamaso pake, ndipo mitima ya Aigupto yachokamo ndi mantha.
Пророцтво про Єгипет. Ось на хмарі леге́нькій несеться Госпо́дь і прибу́де в Єгипет, — і затремтя́ть перед лицем Його бовва́ни Єгипту, і серце Єгипту розта́не посеред нього.
2 “Ine ndidzadzutsa Aigupto kuti amenyane okhaokha; mʼbale adzamenyana ndi mʼbale wake, mnansi ndi mnansi wake, mzinda ndi mzinda unzake, ndiponso ufumu ndi ufumu unzake.
І підбу́рю єги́птянина на єги́птянина, і будуть точи́ти війну кожен з братом своїм, і кожен із ближнім своїм, місто з містом, а царство із царством.
3 Aigupto adzataya mtima popeza ndidzalepheretsa zolinga zawo; adzapempha nzeru kwa mafano awo ndiponso kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa, kwa amawula ndi kwa oyankhula ndi mizimu.
І Єгипет на дусі пони́кне в своє́му нутрі́, а раду його Я поплу́таю, і вони будуть питати бовва́нів своїх, і заклиначі́в духів та духів померлих і своїх ворожби́тів.
4 Ndidzawapereka Aigupto kwa olamulira ankhanza, ndipo mfumu yoopsa idzawalamulira,” akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.
І віддам Я Єгипет у руку жорсто́кого пана, і цар лютий над ним запанує, говорить Господь, Господь Саваот!
5 Madzi a mu mtsinje wa Nailo adzaphwa, ndipo mʼmbali mwa mtsinje mudzangʼaluka ndi kuwuma.
І зникне із Моря вода, і висохне Річка, та й стане суха.
6 Ngalande zake zidzanunkha; ndipo mitsinje ya Igupto idzayamba kuchepa ndi kuwuma. Bango ndi dulu zidzafota,
І засмердя́ться річки́ та нужде́нними стануть, і повисиха́ють прито́ки Єгипту, пов'я́не коми́ш та очере́т.
7 ndiponso zomera za mʼmphepete mwa Nailo ndi ku mathiriro a mtsinjewo. Zonse zodzalidwa mʼmbali mwa Nailo zidzawuma, zidzawuluzika ndipo sizidzaonekanso.
Луги над рікою, над берегом річки, і все, що при рі́чці посіяне, повисиха́є, розвіється все, і не буде його.
8 Asodzi adzabuwula ndi kudandaula, onse amene amaponya mbedza mu Nailo; onse amene amaponya makoka mʼmadzi adzalira.
І заплачуть риба́лки, і будуть ридати всі ті, що гачка́ закида́ють до річки, а ті, що розтя́гують не́від на воду, стратять надію.
9 Amene amagwira ntchito yopota thonje adzataya mtima, anthu oluka nsalu zofewa zabafuta adzataya chiyembekezo.
А ті, що працюють при че́санім льоні та тчуть полотно́, засоро́мляться.
10 Akatswiri opanga nsalu adzangoti kakasi, ndipo anthu onse ogwira ntchito yolipidwa adzatheratu mphamvu.
І будуть осно́ви Єгипту розбиті, всі ж працю́ючі за плату на дусі впаду́ть.
11 Akuluakulu a ku Zowani ndi zitsiru; aphungu a nzeru a Farao amalangiza zopusa. Kodi mungathe kunena bwanji kwa Farao kuti, “Ine ndine mmodzi mwa anthu anzeru, wophunzira wa mafumu akale?”
Дійсно, вельмо́жі Цоа́ну безумні, і нерозумною стала рада мудрих фараонових ра́дників. І як фараонові скажете: Я син мудреці́в, я син давніх царів?
12 Iwe Farao, anthu ako anzeru ali kuti? Abweretu kuti akuwuze ndi kukudziwitsa zimene Yehova Wamphamvuzonse wakonza kuchitira dziko la Igupto.
Де ж вони, де твої мудреці? І хай розка́жуть тобі й хай пізна́ють, що порадив Госпо́дь Саваот на Єгипет.
13 Akuluakulu a ku Zowani asanduka zitsiru, atsogoleri a ku Mefisi anamizidwa; atsogoleri a dziko la Igupto asocheretsa anthu a dzikolo.
Стали немудрі вельможі Цоа́ну, вельможі Мемфісу обма́нені, учинили блудя́чим Єгипет головніші з племе́н його.
14 Yehova wasocheretsa anthu a ku Igupto. Iwo akuchita kudzandira pa zonse zimene akuchita, ngati chidakwa choterereka pa masanzi ake.
Господь влив у нього дух о́дуру, і вони вчинили блудя́чим Єгипет в усякому чині його, як блу́дить п'яни́ця в блюво́ті своїй.
15 Palibe chimene munthu wa mu Igupto angachite, mtsogoleri kapena wotsatira, nthambi ya kanjedza kapena bango.
І Єгипет не матиме ді́ла, що вміли б вчинити його голова або хвіст, пальмо́ва галу́зка чи очерети́на.
16 Tsiku limenelo Aigupto adzakhala ngati amayi. Adzanjenjemera ndi kuchita mantha akadzaona Yehova Wamphamvuzonse, atakweza dzanja lake kufuna kuwalanga.
Того дня стане Єгипет, немов ті жінки́, і тремтітиме, і буде лякатись по́маху руки Господа Саваота, що Він нею над ним помаха́є.
17 Ndipo dziko la Yuda lidzaopsa dziko la Aigupto. Aliyense amene adzamve dzina la Yuda adzaopsedwa chifukwa cha zimene Yehova Wamphamvuzonse wakonzekera kuchitira dziko la Igupto.
І стане юдейська земля для Єгипту за по́страх: кожен, кому пригадають про неї, злякається перед за́думом Господа Саваота, якого повзяв Він на нього.
18 Tsiku limenelo ku dziko la Igupto kudzakhala mizinda isanu yoyankhula chiyankhulo cha Akanaani, ndipo anthu ake adzalumbira kwa Yehova Wamphamvuzonse kuti adzamutumikira. Umodzi mwa mizindayo udzatchedwa Mzinda Wachilungamo.
Того дня буде п'ять міст в єгипетськім кра́ї, що говоритимуть ханаанською мовою й присягатимуть Господом Саваотом. Одне буде зватися Ір-Гахерес.
19 Tsiku limenelo mʼkati mwa dziko la Igupto mudzakhala guwa lansembe la Yehova, ndipo mʼmalire mwake adzayikira Yehova mwala wachikumbutso.
Того дня серед кра́ю єгипетського буде же́ртівник Господу, і стовп при границі його Господе́ві.
20 Zimenezo zidzakhala umboni wozindikiritsa kuti Yehova Wamphamvuzonse alimo mʼdziko la Igupto. Pamene Aigupto adzalirira Yehova chifukwa cha owapondereza, Iye adzawatumizira mpulumutsi ndi mtetezi ndipo adzawalanditsa.
І він буде в єгипетськім кра́ї ознакою й свідком для Господа Саваота, — коли будуть взивати до Господа перед гноби́телями, то пошле їм спасителя та оборо́нця, який їх спасе.
21 Kotero Yehova adzadziulula yekha kwa Aigupto, ndipo tsiku limenelo adzadziwa Yehova. Adzapembedza Yehova popereka nsembe ndi popereka zopereka zachakudya; Adzalumbira kwa Yehova ndipo adzachita zimene alumbirazo.
І стане знаний Господь для Єгипту, і того дня позна́ють єги́птяни Господа, і будуть служити жертвою й жертвою хлі́бною, і присягну́ть обі́тницю Господе́ві, і ви́повнять.
22 Yehova adzakantha Aigupto ndi mliri. Iye adzawakanthadi ndipo kenaka adzawachiritsa. Aigupto adzatembenukira kwa Yehova ndipo Iye adzamva madandawulo awo ndi kuwachiritsa.
І вра́зить єги́птян Господь, буде бити їх та лікувати, і до Господа зве́рнуться, і Він дасться їм ублагати Себе, і їх вилікує.
23 Tsiku limenelo kudzakhala msewu waukulu wochoka ku Igupto kupita ku Asiriya. Aasiriya adzapita ku Igupto ndi Aigupto ku Asiriya. Aigupto ndi Aasiriya adzapembedza pamodzi.
Того дня буде бита дорога з Єгипту в Асирію, і при́йдуть асирі́йці до єги́птян, а єги́птяни до асирі́йців, і будуть служити єгиптяни з асирійцями Господе́ві.
24 Tsiku limenelo Israeli adzakhala pamodzi ndi Igupto ndi Asiriya, mayiko atatuwa adzakhala dalitso pa dziko lapansi.
Того дня буде Ізраїль третім краєм побіч Єгипту й Асирії, благослове́нням серед землі,
25 Yehova Wamphamvuzonse adzawadalitsa, ndi mawu awa, “Adalitsike anthu anga Aigupto, Aasiriya, ntchito ya manja anga, ndi Aisraeli osankhidwa anga.”
бо Господь Саваот його поблагослови́в та й сказав: Благословенний наро́д мій Єгипет, і Ашшу́р, чин Моїх рук, та Ізраїль, спа́дщина Моя!