< Yesaya 19 >

1 Uthenga onena za Igupto: Taonani, Yehova wakwera pa mtambo waliwiro, ndipo akupita ku Igupto. Mafano a ku Igupto akunjenjemera pamaso pake, ndipo mitima ya Aigupto yachokamo ndi mantha.
Detta är tungen öfver Egypti land: Si, Herren skall fara uti enom snarom sky, och komma in uti Egypten; då skola de afgudar uti Egypten bäfva för honom, och de Egyptiers hjerta skall gifva sig i dem.
2 “Ine ndidzadzutsa Aigupto kuti amenyane okhaokha; mʼbale adzamenyana ndi mʼbale wake, mnansi ndi mnansi wake, mzinda ndi mzinda unzake, ndiponso ufumu ndi ufumu unzake.
Och jag skall hetsa, de Egyptier på hvarannan, att en broder skall strida emot den andra, en vän emot den andra, en stad emot den andra, ett rike emot det andra.
3 Aigupto adzataya mtima popeza ndidzalepheretsa zolinga zawo; adzapempha nzeru kwa mafano awo ndiponso kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa, kwa amawula ndi kwa oyankhula ndi mizimu.
Och de Egyptiers mod skall förgås i dem, och jag skall göra deras anslag omintet; så skola de då fråga deras afgudar och Prester, och spåmän och tecknatydare.
4 Ndidzawapereka Aigupto kwa olamulira ankhanza, ndipo mfumu yoopsa idzawalamulira,” akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.
Men jag skall gifva de Egyptier uti grufveliga herrars händer; och en hård Konung skall råda öfver dem, säger den rådandes Herren Zebaoth.
5 Madzi a mu mtsinje wa Nailo adzaphwa, ndipo mʼmbali mwa mtsinje mudzangʼaluka ndi kuwuma.
Och vattnet i hafvet skall uttorkas; dertill skola ock strömmarna, bortsjunka och försvinna.
6 Ngalande zake zidzanunkha; ndipo mitsinje ya Igupto idzayamba kuchepa ndi kuwuma. Bango ndi dulu zidzafota,
Älfverna skola utlöpa, så att dammsjöarna skola förminskas och torre varda; rör och säf förvissna.
7 ndiponso zomera za mʼmphepete mwa Nailo ndi ku mathiriro a mtsinjewo. Zonse zodzalidwa mʼmbali mwa Nailo zidzawuma, zidzawuluzika ndipo sizidzaonekanso.
Och gräset vid bäckerna, och all säd vid vattnet skall förfalna, förderfvas och till intet varda.
8 Asodzi adzabuwula ndi kudandaula, onse amene amaponya mbedza mu Nailo; onse amene amaponya makoka mʼmadzi adzalira.
Och fiskarena skola sörja, och alle de, som fiskakrok kasta i vattnet, skola beklaga sig; och de, som nät utkasta i vattnet, skola bedröfvade varda.
9 Amene amagwira ntchito yopota thonje adzataya mtima, anthu oluka nsalu zofewa zabafuta adzataya chiyembekezo.
De skola afgå med skam, som god garn göra, och nät binda.
10 Akatswiri opanga nsalu adzangoti kakasi, ndipo anthu onse ogwira ntchito yolipidwa adzatheratu mphamvu.
Och de som fiskakistor hafva, med alla dem som dammar för lön göra, skola ångse varda.
11 Akuluakulu a ku Zowani ndi zitsiru; aphungu a nzeru a Farao amalangiza zopusa. Kodi mungathe kunena bwanji kwa Farao kuti, “Ine ndine mmodzi mwa anthu anzeru, wophunzira wa mafumu akale?”
De Förstar i Zoan äro dårar, Pharaos vise rådgifvare äro i deras råd galne vordne. Hvi sägen I dock om Pharao: Jag är visamannabarn, och är af gamla Konungar kommen?
12 Iwe Farao, anthu ako anzeru ali kuti? Abweretu kuti akuwuze ndi kukudziwitsa zimene Yehova Wamphamvuzonse wakonza kuchitira dziko la Igupto.
Hvar äro då nu dine vise? Låt dem förkunna, och undervisa dig, hvad Herren Zebaoth öfver Egypten beslutit hafver.
13 Akuluakulu a ku Zowani asanduka zitsiru, atsogoleri a ku Mefisi anamizidwa; atsogoleri a dziko la Igupto asocheretsa anthu a dzikolo.
Men de Förstar i Zoan äro vordne till dårar; de Förstar i Noph äro bedragne; de förföra samt med Egypten hörnstenen för slägten.
14 Yehova wasocheretsa anthu a ku Igupto. Iwo akuchita kudzandira pa zonse zimene akuchita, ngati chidakwa choterereka pa masanzi ake.
Ty Herren hafver utgjutit en villoanda ibland dem, att de skola förföra Egypten uti allt det de göra, såsom en drucken ragar, då han spyr.
15 Palibe chimene munthu wa mu Igupto angachite, mtsogoleri kapena wotsatira, nthambi ya kanjedza kapena bango.
Och Egypten skall ingen hafva, den der för hufvud eller stjert, bål eller gren är.
16 Tsiku limenelo Aigupto adzakhala ngati amayi. Adzanjenjemera ndi kuchita mantha akadzaona Yehova Wamphamvuzonse, atakweza dzanja lake kufuna kuwalanga.
På den tiden skall Egypten vara såsom qvinnor, och frukta sig, och förskräckas, då Herren Zebaoth veftar handena öfver dem.
17 Ndipo dziko la Yuda lidzaopsa dziko la Aigupto. Aliyense amene adzamve dzina la Yuda adzaopsedwa chifukwa cha zimene Yehova Wamphamvuzonse wakonzekera kuchitira dziko la Igupto.
Och Egypten skall frukta sig för Juda lande, så att den der tänker uppå, han skall förskräckas öfver Herrans Zebaoths råd, som han öfver det beslutit hafver.
18 Tsiku limenelo ku dziko la Igupto kudzakhala mizinda isanu yoyankhula chiyankhulo cha Akanaani, ndipo anthu ake adzalumbira kwa Yehova Wamphamvuzonse kuti adzamutumikira. Umodzi mwa mizindayo udzatchedwa Mzinda Wachilungamo.
Uti den tiden skola fem städer uti Egypti land tala efter Canaans mål, och svärja vid Herran Zebaoth; en af dem skall heta Irheres.
19 Tsiku limenelo mʼkati mwa dziko la Igupto mudzakhala guwa lansembe la Yehova, ndipo mʼmalire mwake adzayikira Yehova mwala wachikumbutso.
På den samma tiden skall Herrans Zebaoths altare vara midt uti Egypti land, och en Herrans vårdsten i gränsone;
20 Zimenezo zidzakhala umboni wozindikiritsa kuti Yehova Wamphamvuzonse alimo mʼdziko la Igupto. Pamene Aigupto adzalirira Yehova chifukwa cha owapondereza, Iye adzawatumizira mpulumutsi ndi mtetezi ndipo adzawalanditsa.
Den ett tecken och vittne vara skall Herranom Zebaoth uti Egypti land; ty de skola ropa till Herran, för sina plågares skull, och han skall sända dem en Frälsare och mästare, som dem hjelpa skall.
21 Kotero Yehova adzadziulula yekha kwa Aigupto, ndipo tsiku limenelo adzadziwa Yehova. Adzapembedza Yehova popereka nsembe ndi popereka zopereka zachakudya; Adzalumbira kwa Yehova ndipo adzachita zimene alumbirazo.
Ty Herren skall af, de Egyptier känd varda; och de Egyptier skola känna Herran på den tiden, och skola tjena honom med offer och spisoffer, och skola göra Herranom löfte, och hålla det.
22 Yehova adzakantha Aigupto ndi mliri. Iye adzawakanthadi ndipo kenaka adzawachiritsa. Aigupto adzatembenukira kwa Yehova ndipo Iye adzamva madandawulo awo ndi kuwachiritsa.
Och Herren skall slå de Egyptier, och hela dem; ty de skola omvända sig till Herran, och han skall låta bedja sig, och hela dem.
23 Tsiku limenelo kudzakhala msewu waukulu wochoka ku Igupto kupita ku Asiriya. Aasiriya adzapita ku Igupto ndi Aigupto ku Asiriya. Aigupto ndi Aasiriya adzapembedza pamodzi.
På den tiden skall en väg vara ifrån Egypten in uti Assyrien, så att de Assyrier skola komma in uti Egypten, och de Egyptier in uti Assyrien, och både Egyptier och Assyrier Gudi tjena.
24 Tsiku limenelo Israeli adzakhala pamodzi ndi Igupto ndi Asiriya, mayiko atatuwa adzakhala dalitso pa dziko lapansi.
På samma tiden skall Israel vara sjelf tredje, med de Egyptier och Assyrier, genom den välsignelse, som på jordene vara skall.
25 Yehova Wamphamvuzonse adzawadalitsa, ndi mawu awa, “Adalitsike anthu anga Aigupto, Aasiriya, ntchito ya manja anga, ndi Aisraeli osankhidwa anga.”
Ty Herren Zebaoth skall välsigna dem, och säga: Välsignad äst du Egypten, mitt folk, och du Assur, mina händers verk, och du Israel, mitt arf.

< Yesaya 19 >