< Yesaya 19 >

1 Uthenga onena za Igupto: Taonani, Yehova wakwera pa mtambo waliwiro, ndipo akupita ku Igupto. Mafano a ku Igupto akunjenjemera pamaso pake, ndipo mitima ya Aigupto yachokamo ndi mantha.
La carga de Egipto. “He aquí que el Señor cabalga sobre una nube veloz y llega a Egipto. Los ídolos de Egipto temblarán ante su presencia, y el corazón de Egipto se derretirá en su interior.
2 “Ine ndidzadzutsa Aigupto kuti amenyane okhaokha; mʼbale adzamenyana ndi mʼbale wake, mnansi ndi mnansi wake, mzinda ndi mzinda unzake, ndiponso ufumu ndi ufumu unzake.
Yo incitaré a los egipcios contra los egipcios, y lucharán cada uno contra su hermano, y cada uno contra su vecino; ciudad contra ciudad, y reino contra reino.
3 Aigupto adzataya mtima popeza ndidzalepheretsa zolinga zawo; adzapempha nzeru kwa mafano awo ndiponso kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa, kwa amawula ndi kwa oyankhula ndi mizimu.
El espíritu de los egipcios fracasará dentro de ellos. Destruiré su consejo. Buscarán a los ídolos, a los encantadores, a los que tienen espíritus familiares y a los magos.
4 Ndidzawapereka Aigupto kwa olamulira ankhanza, ndipo mfumu yoopsa idzawalamulira,” akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.
Entregaré a los egipcios en manos de un señor cruel. Un rey feroz los gobernará”, dice el Señor, Yahvé de los Ejércitos.
5 Madzi a mu mtsinje wa Nailo adzaphwa, ndipo mʼmbali mwa mtsinje mudzangʼaluka ndi kuwuma.
Las aguas del mar faltarán, y el río se perderá y se secará.
6 Ngalande zake zidzanunkha; ndipo mitsinje ya Igupto idzayamba kuchepa ndi kuwuma. Bango ndi dulu zidzafota,
Los ríos se ensuciarán. Los arroyos de Egipto disminuirán y se secarán. Los juncos y las banderas se marchitarán.
7 ndiponso zomera za mʼmphepete mwa Nailo ndi ku mathiriro a mtsinjewo. Zonse zodzalidwa mʼmbali mwa Nailo zidzawuma, zidzawuluzika ndipo sizidzaonekanso.
Las praderas junto al Nilo, junto al borde del Nilo, y todos los campos sembrados del Nilo, se secarán, serán expulsados y ya no existirán.
8 Asodzi adzabuwula ndi kudandaula, onse amene amaponya mbedza mu Nailo; onse amene amaponya makoka mʼmadzi adzalira.
Los pescadores se lamentarán, y todos los que pescan en el Nilo se lamentarán, y los que tienden redes en las aguas languidecerán.
9 Amene amagwira ntchito yopota thonje adzataya mtima, anthu oluka nsalu zofewa zabafuta adzataya chiyembekezo.
Además, los que trabajan el lino peinado y los que tejen telas blancas se confundirán.
10 Akatswiri opanga nsalu adzangoti kakasi, ndipo anthu onse ogwira ntchito yolipidwa adzatheratu mphamvu.
Las columnas se romperán en pedazos. Todos los que trabajan por cuenta ajena tendrán el alma afligida.
11 Akuluakulu a ku Zowani ndi zitsiru; aphungu a nzeru a Farao amalangiza zopusa. Kodi mungathe kunena bwanji kwa Farao kuti, “Ine ndine mmodzi mwa anthu anzeru, wophunzira wa mafumu akale?”
Los príncipes de Zoán son completamente necios. El consejo de los más sabios consejeros del Faraón se ha vuelto estúpido. ¿Cómo dices al Faraón: “Yo soy hijo de sabios, hijo de reyes antiguos”?
12 Iwe Farao, anthu ako anzeru ali kuti? Abweretu kuti akuwuze ndi kukudziwitsa zimene Yehova Wamphamvuzonse wakonza kuchitira dziko la Igupto.
¿Dónde están, pues, tus sabios? Deja que ellos te lo digan ahora; y que sepan lo que el Señor de los Ejércitos ha dispuesto respecto a Egipto.
13 Akuluakulu a ku Zowani asanduka zitsiru, atsogoleri a ku Mefisi anamizidwa; atsogoleri a dziko la Igupto asocheretsa anthu a dzikolo.
Los príncipes de Zoán se han vuelto necios. Los príncipes de Menfis están engañados. Ellos han hecho que Egipto se extravíe, los que son la piedra angular de sus tribus.
14 Yehova wasocheretsa anthu a ku Igupto. Iwo akuchita kudzandira pa zonse zimene akuchita, ngati chidakwa choterereka pa masanzi ake.
El Señor ha mezclado un espíritu de perversidad en medio de ella, y han hecho que Egipto se extravíe en todas sus obras, como un borracho que se tambalea en su vómito.
15 Palibe chimene munthu wa mu Igupto angachite, mtsogoleri kapena wotsatira, nthambi ya kanjedza kapena bango.
No habrá obra alguna para Egipto, que pueda hacer cabeza o cola, rama de palma o junco.
16 Tsiku limenelo Aigupto adzakhala ngati amayi. Adzanjenjemera ndi kuchita mantha akadzaona Yehova Wamphamvuzonse, atakweza dzanja lake kufuna kuwalanga.
En aquel día los egipcios serán como mujeres. Temerán y se estremecerán a causa del temblor de la mano de Yahvé de los Ejércitos, que sacude sobre ellos.
17 Ndipo dziko la Yuda lidzaopsa dziko la Aigupto. Aliyense amene adzamve dzina la Yuda adzaopsedwa chifukwa cha zimene Yehova Wamphamvuzonse wakonzekera kuchitira dziko la Igupto.
La tierra de Judá se convertirá en un terror para Egipto. Todo aquel a quien se le mencione tendrá miedo, a causa de los planes del Señor de los Ejércitos, que él determina contra ella.
18 Tsiku limenelo ku dziko la Igupto kudzakhala mizinda isanu yoyankhula chiyankhulo cha Akanaani, ndipo anthu ake adzalumbira kwa Yehova Wamphamvuzonse kuti adzamutumikira. Umodzi mwa mizindayo udzatchedwa Mzinda Wachilungamo.
En ese día, habrá cinco ciudades en la tierra de Egipto que hablen la lengua de Canaán y juren a Yahvé de los Ejércitos. Una se llamará “La ciudad de la destrucción”.
19 Tsiku limenelo mʼkati mwa dziko la Igupto mudzakhala guwa lansembe la Yehova, ndipo mʼmalire mwake adzayikira Yehova mwala wachikumbutso.
En ese día, habrá un altar a Yahvé en medio de la tierra de Egipto, y una columna a Yahvé en su frontera.
20 Zimenezo zidzakhala umboni wozindikiritsa kuti Yehova Wamphamvuzonse alimo mʼdziko la Igupto. Pamene Aigupto adzalirira Yehova chifukwa cha owapondereza, Iye adzawatumizira mpulumutsi ndi mtetezi ndipo adzawalanditsa.
Será para señal y para testimonio del Señor de los Ejércitos en la tierra de Egipto; porque clamarán al Señor a causa de los opresores, y él les enviará un salvador y un defensor, y los librará.
21 Kotero Yehova adzadziulula yekha kwa Aigupto, ndipo tsiku limenelo adzadziwa Yehova. Adzapembedza Yehova popereka nsembe ndi popereka zopereka zachakudya; Adzalumbira kwa Yehova ndipo adzachita zimene alumbirazo.
Yahvé será conocido en Egipto, y los egipcios conocerán a Yahvé en ese día. Sí, adorarán con sacrificios y ofrendas, y harán un voto a Yahvé, y lo cumplirán.
22 Yehova adzakantha Aigupto ndi mliri. Iye adzawakanthadi ndipo kenaka adzawachiritsa. Aigupto adzatembenukira kwa Yehova ndipo Iye adzamva madandawulo awo ndi kuwachiritsa.
Yahvé golpeará a Egipto, golpeando y sanando. Volverán a Yahvé, y él se dejará implorar por ellos, y los sanará.
23 Tsiku limenelo kudzakhala msewu waukulu wochoka ku Igupto kupita ku Asiriya. Aasiriya adzapita ku Igupto ndi Aigupto ku Asiriya. Aigupto ndi Aasiriya adzapembedza pamodzi.
En aquel día habrá una carretera de Egipto a Asiria, y el asirio entrará en Egipto, y el egipcio en Asiria; y los egipcios adorarán con los asirios.
24 Tsiku limenelo Israeli adzakhala pamodzi ndi Igupto ndi Asiriya, mayiko atatuwa adzakhala dalitso pa dziko lapansi.
En ese día, Israel será el tercero con Egipto y con Asiria, una bendición dentro de la tierra;
25 Yehova Wamphamvuzonse adzawadalitsa, ndi mawu awa, “Adalitsike anthu anga Aigupto, Aasiriya, ntchito ya manja anga, ndi Aisraeli osankhidwa anga.”
porque el Señor de los Ejércitos los ha bendecido, diciendo: “Bendito sea Egipto, mi pueblo, Asiria, obra de mis manos, e Israel, mi herencia.”

< Yesaya 19 >