< Yesaya 19 >

1 Uthenga onena za Igupto: Taonani, Yehova wakwera pa mtambo waliwiro, ndipo akupita ku Igupto. Mafano a ku Igupto akunjenjemera pamaso pake, ndipo mitima ya Aigupto yachokamo ndi mantha.
Пророчие ымпотрива Еӂиптулуй: Ятэ, Домнул кэлэреште пе ун нор репеде ши вине ын Еӂипт. Идолий Еӂиптулуй тремурэ ынаинтя Луй ши ли се ындоае инима еӂиптенилор ын ей.
2 “Ine ndidzadzutsa Aigupto kuti amenyane okhaokha; mʼbale adzamenyana ndi mʼbale wake, mnansi ndi mnansi wake, mzinda ndi mzinda unzake, ndiponso ufumu ndi ufumu unzake.
„Вой ынарма пе еӂиптень уний ымпотрива алтора ши се вор бате фрате ку фрате, приетен ку приетен, четате ку четате, ымпэрэцие ку ымпэрэцие.
3 Aigupto adzataya mtima popeza ndidzalepheretsa zolinga zawo; adzapempha nzeru kwa mafano awo ndiponso kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa, kwa amawula ndi kwa oyankhula ndi mizimu.
Духул еӂиптенилор ва пери дин ей ши ле вой нимичи сфатул; атунч вор ынтреба пе идоль ши пе врэжиторь, пе чей че кямэ морций ши пе гичиторь.
4 Ndidzawapereka Aigupto kwa olamulira ankhanza, ndipo mfumu yoopsa idzawalamulira,” akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.
Вой да Еӂиптул ын мыниле унуй стэпын аспру ши ун ымпэрат фэрэ милэ ва стэпыни песте ей”, зиче Домнул Думнезеул оштирилор.
5 Madzi a mu mtsinje wa Nailo adzaphwa, ndipo mʼmbali mwa mtsinje mudzangʼaluka ndi kuwuma.
Апеле мэрий вор сека ши рыул ва сека ши се ва уска,
6 Ngalande zake zidzanunkha; ndipo mitsinje ya Igupto idzayamba kuchepa ndi kuwuma. Bango ndi dulu zidzafota,
рыуриле се вор ымпуци, каналеле Еӂиптулуй вор фи гоале ши ускате, пипиригул ши трестииле се вор вештежи.
7 ndiponso zomera za mʼmphepete mwa Nailo ndi ku mathiriro a mtsinjewo. Zonse zodzalidwa mʼmbali mwa Nailo zidzawuma, zidzawuluzika ndipo sizidzaonekanso.
Ливезиле Нилулуй де ла ымбукэтура рыулуй ши тоате семэнэтуриле дин валя рыулуй се вор уска, се вор префаче ын цэрынэ ши вор пери.
8 Asodzi adzabuwula ndi kudandaula, onse amene amaponya mbedza mu Nailo; onse amene amaponya makoka mʼmadzi adzalira.
Вор ӂеме пескарий, се вор бочи тоць чей че арункэ ундица ын рыу ши чей че ынтинд мреже пе апе вор фи немынгыяць.
9 Amene amagwira ntchito yopota thonje adzataya mtima, anthu oluka nsalu zofewa zabafuta adzataya chiyembekezo.
Чей че лукрязэ инул дэрэчит ши чей че цес цесэтурь албе вор фи акопериць де рушине,
10 Akatswiri opanga nsalu adzangoti kakasi, ndipo anthu onse ogwira ntchito yolipidwa adzatheratu mphamvu.
стэпыниторий цэрий вор фи ынтристаць ши тоць симбриаший вор фи ку инима амэрытэ.
11 Akuluakulu a ku Zowani ndi zitsiru; aphungu a nzeru a Farao amalangiza zopusa. Kodi mungathe kunena bwanji kwa Farao kuti, “Ine ndine mmodzi mwa anthu anzeru, wophunzira wa mafumu akale?”
Ын адевэр, воевозий Цоанулуй ау ыннебунит, сфетничий ынцелепць ай луй Фараон с-ау простит. Кум ындрэзниць вой сэ спунець луй Фараон: „Ной сунтем фиий ынцелепцилор, фиий стрэвекилор ымпэраць”?
12 Iwe Farao, anthu ako anzeru ali kuti? Abweretu kuti akuwuze ndi kukudziwitsa zimene Yehova Wamphamvuzonse wakonza kuchitira dziko la Igupto.
Унде сунт ынцелепций тэй? Сэ-ць факэ дескоперирь думнезеешть ши сэ спунэ че а хотэрыт Домнул оштирилор ымпотрива Еӂиптулуй.
13 Akuluakulu a ku Zowani asanduka zitsiru, atsogoleri a ku Mefisi anamizidwa; atsogoleri a dziko la Igupto asocheretsa anthu a dzikolo.
Воевозий Цоанулуй ау ыннебунит, воевозий Нофулуй с-ау ыншелат, кэпетенииле семинциилор дук Еӂиптул ын рэтэчире:
14 Yehova wasocheretsa anthu a ku Igupto. Iwo akuchita kudzandira pa zonse zimene akuchita, ngati chidakwa choterereka pa masanzi ake.
Домнул а рэспындит ын мижлокул луй ун дух де амецялэ, ка сэ факэ пе еӂиптень сэ се клатине ын тоате фаптеле лор, кум се клатинэ ун ом бят ши варсэ,
15 Palibe chimene munthu wa mu Igupto angachite, mtsogoleri kapena wotsatira, nthambi ya kanjedza kapena bango.
ши Еӂиптул ну ва авя пе нимень каре сэ поатэ фаче чева, нич кап, нич коадэ, нич рамурэ де финик, нич трестие!
16 Tsiku limenelo Aigupto adzakhala ngati amayi. Adzanjenjemera ndi kuchita mantha akadzaona Yehova Wamphamvuzonse, atakweza dzanja lake kufuna kuwalanga.
Ын зиуа ачея, Еӂиптул ва фи ка о фемее: ва тремура ши се ва теме, вэзынд мишкаря мыний Домнулуй оштирилор, кынд о ва ридика ымпотрива луй.
17 Ndipo dziko la Yuda lidzaopsa dziko la Aigupto. Aliyense amene adzamve dzina la Yuda adzaopsedwa chifukwa cha zimene Yehova Wamphamvuzonse wakonzekera kuchitira dziko la Igupto.
Кяр ши цара луй Иуда ва фи о гроазэ пентру Еӂипт: кум и се ва ворби де еа, се ва ынгрози дин причина хотэрырий луате ымпотрива луй де Домнул оштирилор.
18 Tsiku limenelo ku dziko la Igupto kudzakhala mizinda isanu yoyankhula chiyankhulo cha Akanaani, ndipo anthu ake adzalumbira kwa Yehova Wamphamvuzonse kuti adzamutumikira. Umodzi mwa mizindayo udzatchedwa Mzinda Wachilungamo.
Ын время ачея, вор фи чинч четэць ын цара Еӂиптулуй, каре вор ворби лимба Канаанулуй ши вор жура пе Домнул оштирилор: уна дин еле се ва нуми „Четатя Нимичирий”!
19 Tsiku limenelo mʼkati mwa dziko la Igupto mudzakhala guwa lansembe la Yehova, ndipo mʼmalire mwake adzayikira Yehova mwala wachikumbutso.
Тот ын время ачея ва фи ун алтар пентру Домнул ын цара Еӂиптулуй ши ла хотар ва фи ун стылп де адучере аминте пентру Домнул.
20 Zimenezo zidzakhala umboni wozindikiritsa kuti Yehova Wamphamvuzonse alimo mʼdziko la Igupto. Pamene Aigupto adzalirira Yehova chifukwa cha owapondereza, Iye adzawatumizira mpulumutsi ndi mtetezi ndipo adzawalanditsa.
Ачеста ва фи пентру Домнул оштирилор ун семн ши о мэртурие ын цара Еӂиптулуй. Ей вор стрига кэтре Домнул дин причина асуприторилор, ши Ел ле ва тримите ун мынтуитор ши ун апэрэтор, каре сэ-й избэвяскэ.
21 Kotero Yehova adzadziulula yekha kwa Aigupto, ndipo tsiku limenelo adzadziwa Yehova. Adzapembedza Yehova popereka nsembe ndi popereka zopereka zachakudya; Adzalumbira kwa Yehova ndipo adzachita zimene alumbirazo.
Атунч, Домнул Се ва дескопери еӂиптенилор, ши еӂиптений вор куноаште пе Домнул ын зиуа ачея. Вор адуче жертфе ши дарурь де мынкаре, вор фаче журуинце Домнулуй ши ле вор ымплини.
22 Yehova adzakantha Aigupto ndi mliri. Iye adzawakanthadi ndipo kenaka adzawachiritsa. Aigupto adzatembenukira kwa Yehova ndipo Iye adzamva madandawulo awo ndi kuwachiritsa.
Астфел, Домнул ва лови пе еӂиптень, ый ва лови, дар ый ва тэмэдуи. Ей се вор ынтоарче ла Домнул, каре-й ва аскулта ши-й ва виндека.
23 Tsiku limenelo kudzakhala msewu waukulu wochoka ku Igupto kupita ku Asiriya. Aasiriya adzapita ku Igupto ndi Aigupto ku Asiriya. Aigupto ndi Aasiriya adzapembedza pamodzi.
Ын ачеяшь време, ва фи ун друм каре ва дуче дин Еӂипт ын Асирия: асириений се вор дуче ын Еӂипт ши еӂиптений, ын Асирия, ши еӂиптений ымпреунэ ку асириений вор служи Домнулуй.
24 Tsiku limenelo Israeli adzakhala pamodzi ndi Igupto ndi Asiriya, mayiko atatuwa adzakhala dalitso pa dziko lapansi.
Тот ын время ачея, Исраел ва фи ал трейля, унит ку Еӂиптул ши ку Асирия, ка о бинекувынтаре ын мижлокул пэмынтулуй.
25 Yehova Wamphamvuzonse adzawadalitsa, ndi mawu awa, “Adalitsike anthu anga Aigupto, Aasiriya, ntchito ya manja anga, ndi Aisraeli osankhidwa anga.”
Домнул оштирилор ый ва бинекувынта ши ва зиче: „Бинекувынтат сэ фие Еӂиптул, попорул Меу, ши Асирия, лукраря мынилор Меле, ши Исраел, моштениря Мя!”

< Yesaya 19 >