< Yesaya 18 >
1 Tsoka kwa anthu a ku Kusi. Kumeneko kumamveka mkokomo wa mapiko a dzombe.
Горе тобі, дзвінкокри́лий ти кра́ю, що з дру́гого бо́ку річо́к етіо́пських,
2 Dziko limenelo limatumiza akazembe pa mtsinje wa Nailo, mʼmabwato amabango amene amayandama pa madzi, ndikunena kuti, “Pitani, inu amithenga aliwiro, kwa mtundu wa anthu ataliatali a khungu losalala, ndi woopedwa ndi anthu. Akazembe anatumidwa ku dziko la anthu amphamvu ndi logonjetsa anthu ena. Dziko lawo ndi logawikanagawikana ndi mitsinje.”
що морем послів посилаєш на човнах папі́русових по пове́рхні води! Ідіть, скорохо́дні посли, до наро́ду високого й блискучезбро́йного, до народу страшно́го відда́вна й аж досі, до люду преси́льного, що топче усе, що річки його землю поперетина́ли.
3 Inu nonse anthu a pa dziko lonse, inu amene mumakhala pa dziko lapansi, pamene mbendera yakwezedwa pa mapiri yangʼanani, ndipo pamene lipenga lilira mumvere.
Усі ме́шканці все́світу, що на землі пробува́єте, — дивіться, коли піднесе́ться прапор на гора́х, слухайте, чи не затру́блять у ріг.
4 Pakuti Yehova akunena kwa ine kuti, “Ndili chikhalire ku malo anga kuno, ndidzakhala chete, ndi kumangoyangʼana, monga momwe dzuwa limawalira nthawi yotentha, monganso momwe mame amagwera usiku pa nthawi yotentha yokolola.”
Бо Госпо́дь так промовив до мене: Я буду спокійний, і буду дивитися з місця Свого пробува́ння, — як тепло́ те при світлі ясно́му, як та хмара роси в спе́ку жнив!
5 Pakuti, anthu asanayambe kukolola, maluwa atayoyoka ndiponso mphesa zitayamba kupsa, Iye adzadula mphukira ndi mipeni yosadzira, ndipo adzadula ndi kuchotsa nthambi zotambalala.
Бо перед жнива́ми, як скі́нчиться цвіт, недозріле ж усе стане зрілими гро́знами, то Він зріже серпа́ми галу́ззя м'які́, а галу́зки, що сте́ляться, повідкидає, повідру́бує Він.
6 Mitembo ya anthu ankhondo adzasiyira mbalame zamʼmapiri zodya nyama ndiponso zirombo zakuthengo; mbalame zidzadya mitemboyo nthawi yonse ya chilimwe, ndipo zirombo zidzayidya pa nthawi yonse yachisanu.
Будуть вони позоста́влені ра́зом для хижого птаха гірсько́го й звіри́ни земно́ї, — і літо над ним проведе́ хижий птах, і вся зе́мна звіри́на над ним перези́мує.
7 Pa nthawi imeneyo anthu adzabwera ndi mphatso kwa Yehova Wamphamvuzonse, zochokera kwa anthu ataliatali ndi osalala, kuchokera kwa mtundu wa anthu woopedwa ndi anthu apafupi ndi akutali omwe, mtundu wa anthu amphamvu ndi a chiyankhulo chachilendo, anthu amene dziko lawo ndi logawikanagawikana ndi mitsinje. Adzabwera nazo mphatso ku Phiri la Ziyoni, ku malo a Dzina la Yehova Wamphamvuzonse.
Того ча́су прине́сений буде дару́нок для Господа Саваота від наро́ду високого й блискучезбро́йного, і від народу страшно́го відда́вна й аж досі, від люду преси́льного, що топче усе, що річки́ його землю поперетина́ли, до місця Йме́ння Господа Саваота па Сіонській горі.