< Yesaya 18 >
1 Tsoka kwa anthu a ku Kusi. Kumeneko kumamveka mkokomo wa mapiko a dzombe.
Ah! le pays du bruissement des ailes, qui est au delà des fleuves de l'Éthiopie;
2 Dziko limenelo limatumiza akazembe pa mtsinje wa Nailo, mʼmabwato amabango amene amayandama pa madzi, ndikunena kuti, “Pitani, inu amithenga aliwiro, kwa mtundu wa anthu ataliatali a khungu losalala, ndi woopedwa ndi anthu. Akazembe anatumidwa ku dziko la anthu amphamvu ndi logonjetsa anthu ena. Dziko lawo ndi logawikanagawikana ndi mitsinje.”
qui envoie des ambassadeurs par la mer, dans des vaisseaux de papyrus sur les eaux, en disant: « Allez, messagers rapides, vers une nation grande et douce, vers un peuple redoutable dès son origine, une nation qui mesure et qui foule, dont le pays est divisé par les fleuves! ».
3 Inu nonse anthu a pa dziko lonse, inu amene mumakhala pa dziko lapansi, pamene mbendera yakwezedwa pa mapiri yangʼanani, ndipo pamene lipenga lilira mumvere.
Vous tous, habitants du monde, et vous, habitants de la terre, quand une bannière est levée sur les montagnes, regardez! Quand on sonne de la trompette, écoutez!
4 Pakuti Yehova akunena kwa ine kuti, “Ndili chikhalire ku malo anga kuno, ndidzakhala chete, ndi kumangoyangʼana, monga momwe dzuwa limawalira nthawi yotentha, monganso momwe mame amagwera usiku pa nthawi yotentha yokolola.”
Car l'Éternel m'a dit: « Je me tiendrai tranquille, et je verrai dans ma demeure, comme une chaleur claire au soleil, comme un nuage de rosée dans la chaleur de la moisson. »
5 Pakuti, anthu asanayambe kukolola, maluwa atayoyoka ndiponso mphesa zitayamba kupsa, Iye adzadula mphukira ndi mipeni yosadzira, ndipo adzadula ndi kuchotsa nthambi zotambalala.
Car avant la moisson, quand la floraison est terminée et que la fleur devient un raisin mûr, il coupera les brins avec des serpes, il abattra et enlèvera les branches étalées.
6 Mitembo ya anthu ankhondo adzasiyira mbalame zamʼmapiri zodya nyama ndiponso zirombo zakuthengo; mbalame zidzadya mitemboyo nthawi yonse ya chilimwe, ndipo zirombo zidzayidya pa nthawi yonse yachisanu.
On les laissera ensemble pour les oiseaux de proie des montagnes et pour les animaux de la terre. Les oiseaux de proie les mangeront en été, et tous les animaux de la terre les mangeront en hiver.
7 Pa nthawi imeneyo anthu adzabwera ndi mphatso kwa Yehova Wamphamvuzonse, zochokera kwa anthu ataliatali ndi osalala, kuchokera kwa mtundu wa anthu woopedwa ndi anthu apafupi ndi akutali omwe, mtundu wa anthu amphamvu ndi a chiyankhulo chachilendo, anthu amene dziko lawo ndi logawikanagawikana ndi mitsinje. Adzabwera nazo mphatso ku Phiri la Ziyoni, ku malo a Dzina la Yehova Wamphamvuzonse.
En ce temps-là, on apportera un présent à l'Éternel des armées, de la part d'un peuple grand et lisse, d'un peuple impressionnant dès son origine, d'une nation qui mesure et foule, dont le pays est partagé par les fleuves, au lieu du nom de l'Éternel des armées, la montagne de Sion.