< Yesaya 17 >

1 Uthenga wonena za Damasiko: “Taonani, mzinda wa Damasiko sudzakhalanso mzinda, koma udzasanduka bwinja.
Brzemię Damaszku. Oto Damaszek przestanie być miastem, a stanie się rumowiskiem.
2 Mizinda ya Aroeri idzakhala yopanda anthu ndipo idzakhala ya ziweto, zimene zidzagona pansi popanda wina woziopseza.
Miasta Aroeru [będą] opuszczone. Będą dla trzód, by się [tam] kładły, a nikt [ich] nie spłoszy.
3 Ku Efereimu sikudzakhalanso linga, ndipo ku Damasiko sikudzakhalanso ufumu; Otsalira a ku Siriya adzachotsedwa ulemu monga anthu a ku Israeli,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Nastąpi koniec twierdzy Efraima i królestwa Damaszku. A z resztką Syrii będzie jak z chwałą synów Izraela, mówi PAN zastępów.
4 “Tsiku limenelo ulemerero wa Yakobo udzazimirira; ndipo chuma chake chidzasanduka umphawi.
I stanie się w tym dniu tak, [że] chwała Jakuba zmaleje, a jego tłuste ciało schudnie.
5 Israeli adzakhala ngati munda wa tirigu umene anatsiriza kukolola. Adzakhalanso ngati munda wa mʼchigwa cha Refaimu anthu atatha kukunkha ngala za tirigu.
I będzie tak jak [wtedy], gdy żniwiarz zbiera zboże, a jego ramię ścina kłosy; będzie jak ten, co zbiera kłosy w dolinie Refaim.
6 Komabe Aisraeli ochepa okha ndiwo ati adzatsale monga mʼmene zimatsalira zipatso ziwiri kapena zitatu pa nthambi ya pamwamba penipeni kapena zipatso zisanu pa nthambi za mʼmunsi mwa mtengo wa olivi akawugwedeza,” akutero Yehova, Mulungu wa Israeli.
Pozostanie na nim jednak pokłosie, jak przy otrząsaniu drzewa oliwnego: dwie lub trzy oliwki [zostaną] na samym wierzchołku drzewa, a cztery lub pięć na urodzajnych gałęziach, mówi PAN, Bóg Izraela.
7 Tsiku limenelo anthu adzayangʼana Mlengi wawo ndipo adzatembenukira kwa Woyerayo wa Israeli.
W tym dniu człowiek spojrzy na swego Stwórcę i jego oczy będą spoglądać na Świętego Izraela.
8 Iwo sadzakhulupiriranso maguwa ansembe, ntchito ya manja awo, ndipo sadzadaliranso mitengo ya mafano a Asera, ndiponso maguwa ofukizirapo lubani amene manja awo anapanga.
A nie popatrzy [więcej] na ołtarze, dzieło swoich rąk, ani nie będzie patrzeć [na to], co uczyniły jego palce ani na gaje, ani na posągi.
9 Tsiku limenelo mizinda yawo yamphamvu, imene anasiya chifukwa cha Aisraeli, idzakhala ngati malo osiyidwa kuti awirire ndi kumera ziyangoyango. Ndipo yonse idzakhala mabwinja.
W tym dniu jego miasta warowne będą jak porzucony konar i sucha gałąź, które opuścili przed synami Izraela – i będzie spustoszenie.
10 Inu mwayiwalatu Mulungu Mpulumutsi wanu; simunakumbukire Thanthwe, linga lanu. Choncho, ngakhale munadzala mbewu zabwino, ndi kuyitanitsa kunja mitengo ya mpesa,
A ponieważ zapomniałeś o Bogu twojego zbawienia i nie pamiętałeś o skale twojej mocy, to [choć] zasadzasz rozkoszne sadzonki i sadzisz obce winorośle;
11 nimuyembekeza kuti zikule tsiku lomwelo ndi kuphukira maluwa mmawa mwake, komabe zimenezi sizidzakupindulirani pa tsiku la mavuto.
I w dniu sprawiasz, że sadzonka rośnie, i rano doprowadzasz swój siew do rozkwitu, w dniu żniwa będziesz żąć mnóstwo smutku i nieuleczalnej rozpaczy.
12 Aa, mkokomo wa anthu a mitundu yambiri, akusokosa ngati kukokoma kwa nyanja! Aa, phokoso la anthu a mitundu ina, akusokosa ngati mkokomo wa madzi amphamvu!
Biada tłumom licznych ludów, [które] huczą jak rozhukane morze, i zgiełkowi narodów, które szumią jak szum wód gwałtownych!
13 Ngakhale ankhondo a mitundu ina akubwera ndi mkokomo ngati wa madzi ambiri, koma adzathawira kutali Mulungu akadzawadzudzula. Yehova adzawapirikitsa ngati mankhusu owuluka ndi mphepo pa phiri, ndi ngati fumbi la kamvuluvulu asanayambe.
Narody szumią jak szum wielkich wód, ale PAN je zgromi i uciekną daleko gnane wiatrem jak plewy na górach i jak biegacz stepowy przed wichurą.
14 Pofika nthawi yamadzulo zoopsa zidzayamba kuchitika, ndipo zidzakhala zitatha pofika mmawa. Izi ndizo zidzachitikire anthu otilanda zinthu, gawo la amene amatibera zinthu zathu.
Oto w porze wieczornej trwoga, a nim nadejdzie poranek, już go nie [ma]. Taki jest dział tych, którzy nas łupią, i los tych, którzy nas plądrują.

< Yesaya 17 >