< Yesaya 17 >
1 Uthenga wonena za Damasiko: “Taonani, mzinda wa Damasiko sudzakhalanso mzinda, koma udzasanduka bwinja.
Наложеното за Дамаск пророчество: - Ето, Дамаск не е вече град, А ще бъде грамада развалини.
2 Mizinda ya Aroeri idzakhala yopanda anthu ndipo idzakhala ya ziweto, zimene zidzagona pansi popanda wina woziopseza.
Градовете на Ароир са напуснати; Те ще служат за стада, Които ще лежат, и не ще има кой да ги плаши.
3 Ku Efereimu sikudzakhalanso linga, ndipo ku Damasiko sikudzakhalanso ufumu; Otsalira a ku Siriya adzachotsedwa ulemu monga anthu a ku Israeli,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Крепостта ще се махне от Ефрема, и царството от Дамаск, И останалото от Сирия ще бъде като славата на израилтяните, Казва Господ на Силите.
4 “Tsiku limenelo ulemerero wa Yakobo udzazimirira; ndipo chuma chake chidzasanduka umphawi.
И в оня ден славата на Якова ще се смали, И тлъстината на месата му ще измършавее;
5 Israeli adzakhala ngati munda wa tirigu umene anatsiriza kukolola. Adzakhalanso ngati munda wa mʼchigwa cha Refaimu anthu atatha kukunkha ngala za tirigu.
И ще бъде както, когато жетварят хване стръкове жито И пожъне класовете с мишцата си; Да! ще бъде както, когато събира някой класове в рафаимската долина.
6 Komabe Aisraeli ochepa okha ndiwo ati adzatsale monga mʼmene zimatsalira zipatso ziwiri kapena zitatu pa nthambi ya pamwamba penipeni kapena zipatso zisanu pa nthambi za mʼmunsi mwa mtengo wa olivi akawugwedeza,” akutero Yehova, Mulungu wa Israeli.
Но ще остане в него пабирък, Както при отръсването на маслината, - Две-три зърна на върха на по-високите клонове. Четири-пет на по-крайните клончета на някое плодородно дърво, Казва Господ Израилевият Бог.
7 Tsiku limenelo anthu adzayangʼana Mlengi wawo ndipo adzatembenukira kwa Woyerayo wa Israeli.
В оня ден човека ще погледни към Създателя си, И очите му ще се взрат в Светия Израилев;
8 Iwo sadzakhulupiriranso maguwa ansembe, ntchito ya manja awo, ndipo sadzadaliranso mitengo ya mafano a Asera, ndiponso maguwa ofukizirapo lubani amene manja awo anapanga.
Той не ще погледне към жертвениците, делото на ръцете си. Нито ще се взре в онова, което изработиха пръстите му. Нито в ашерите, нито в кумирите на слънцето.
9 Tsiku limenelo mizinda yawo yamphamvu, imene anasiya chifukwa cha Aisraeli, idzakhala ngati malo osiyidwa kuti awirire ndi kumera ziyangoyango. Ndipo yonse idzakhala mabwinja.
В оня ден укрепените му градове Ще бъдат като оставените места в гората на планинския връх, Които бидоха оставени по причина на израилтяните; И ще стане там запустение.
10 Inu mwayiwalatu Mulungu Mpulumutsi wanu; simunakumbukire Thanthwe, linga lanu. Choncho, ngakhale munadzala mbewu zabwino, ndi kuyitanitsa kunja mitengo ya mpesa,
Понеже си забравил Бога на спасението си, И не си спомнил силната си Канара, Затова насаждаш приятни садове, И насаденото е от чужди фиданки;
11 nimuyembekeza kuti zikule tsiku lomwelo ndi kuphukira maluwa mmawa mwake, komabe zimenezi sizidzakupindulirani pa tsiku la mavuto.
В деня, когато ги насадиш заграждаш ги с плет, И сутрин правиш семето ти да цъфти; А жетвата ще чезне в деня на скръб И на неизцелима печал.
12 Aa, mkokomo wa anthu a mitundu yambiri, akusokosa ngati kukokoma kwa nyanja! Aa, phokoso la anthu a mitundu ina, akusokosa ngati mkokomo wa madzi amphamvu!
Ах! шуменето на многото племена, Които бучат като бученето на моретата, - И смутът на народите, Които напират като напора на големи води!
13 Ngakhale ankhondo a mitundu ina akubwera ndi mkokomo ngati wa madzi ambiri, koma adzathawira kutali Mulungu akadzawadzudzula. Yehova adzawapirikitsa ngati mankhusu owuluka ndi mphepo pa phiri, ndi ngati fumbi la kamvuluvulu asanayambe.
Народите ще напират като напора на големите води; Но Бог ще ги смъмри и те ще бягат далеч И ще бъдат гонени като плява по планините пред вятъра, И като въртещ се прах пред вихрушката.
14 Pofika nthawi yamadzulo zoopsa zidzayamba kuchitika, ndipo zidzakhala zitatha pofika mmawa. Izi ndizo zidzachitikire anthu otilanda zinthu, gawo la amene amatibera zinthu zathu.
Привечер, ето смущение, И преди да съмне ги няма! Това е делът на тия, които ни обират, И съдбата на ония, които ни разграбват.