< Yesaya 16 >

1 Anthu a ku Mowabu atumiza mphatso za ana ankhosa onenepa, kuchokera ku Sela kudutsa chipululu mpaka kukafika ku phiri la Ziyoni.
Овечки пошліть власникові землі, із Сели на пустиню, на го́ру Сіонської дочки́.
2 Monga momwe mbalame zimawulukira uku ndi uku akazimwaza mʼchisa, momwemonso akazi a ku Mowabu akuyendayenda ku madooko a Arinoni.
І станеться, мов те споло́шене пта́ство, з кубла́ повиго́нене, будуть до́чки Моавські при бро́дах Арнону:
3 Amowabu aja anawuza a ku Yuda kuti, “Tiwuzeni chochita, gamulani zoti tichite. Inu mutiteteze kwa adani anthu. Mukhale ngati mthunzi wathu dzuwa lili pa liwombo. Mutibise, musatipereke ife othawa nkhondo kwa adani athu.
„Подай раду, зроби при́суд, учини нічну тінь свою повного полудня, сховай ви́гнаних, біженця не видавай.
4 Lolani kuti anthu othawa nkhondo a ku Mowabu azikhala pakati panu; mukhale populumukira pawo kwa wowonongayo.” Nthawi idzafika ndipo wozunzayo sadzakhalaponso, kuwononga kudzaleka; waukaliyo adzachoka mʼdzikomo.
Нехай ме́шкають в тебе вигна́нці Моаву, стань їм за́хистом перед грабі́жником, бо не стало наси́льника, скінчи́вся грабу́нок, загинув топта́ч із землі.
5 Mpando waufumu udzakhazikitsidwa mwachikondi; mmodzi mwa zidzukulu za Davide adzakhalapo mokhulupirika. Iyeyo poweruza adzatsata chilungamo ndipo adzalimbikitsa kuchita zachilungamo.
І буде утве́рджений милістю трон, і сяде на ньому у правді в наметі Давида суддя́, що дбатиме за правосу́ддя та буде в справедливості вправний.
6 Tinamva kuti Mowabu anadzikuza kwambiri. Kunyada kwawo ndi kunyogodola kwawo ndi kudzitama kwawo, zonse ndi zopanda phindu.
Ми чули про гордість Моава, що гордий він дуже, про сваво́лю його й його гордість, про лю́тість його, про неслушні його нісені́тниці“.
7 Nʼchifukwa chake Amowabu akulira kwambiri; iwo akulirira dziko lawo. Akubuma momvetsa chisoni chifukwa cha makeke a mphesa a ku Kiri Hareseti.
Буде тому́ голоси́ти Моав над Моавом, увесь голосити він буде! За паляни́цями з грон Кір-Харесету плакати бу́дуть насправді побиті,
8 Minda ya ku Hesiboni yauma, minda ya mpesa ya ku Sibina yaguga. Atsogoleri a mitundu ina anapondaponda minda ya mpesa wabwino, imene nthambi zake zinakafika ku Yazeri, mpaka kutambalalira ku chipululu. Mizu yake inakafika mpaka ku tsidya la nyanja.
бо посохли хешбо́нські поля́, і виноградник Сівми; володарі наро́дів понищили гро́зна добі́рні, які до Язеру сяга́ли й зникали в пустині; галу́зки ж його розтяга́лися, і море вони перейшли́.
9 Kotero Ine ndikulira, monga mmene akulirira anthu a ku Yazeri, chifukwa cha minda ya mpesa ya ku Sibima. Inu anthu a ku Hesiboni, inu anthu a ku Eleali, ndikukunyowetsani ndi misozi! Mwalephera kupeza zokolola, chifukwa cha nkhondo imene inawononga zokolola zonse.
Тому́ то язе́рським плаче́м буду плакати за виногра́дину Сівми. Сльозою своєю тебе орошу́, о Хешбо́не й Ел'а́ле, бо крик бо́ю напав на твій збір та на жни́во твоє.
10 Chimwemwe ndi chisangalalo zalekeka ku minda yanu ya zipatso; palibe amene akuyimba kapena kufuwula mʼminda ya mpesa; palibe amene akupsinya vinyo ku malo opsinyira mphesa, pakuti ndathetsa kufuwula.
І буде за́брана радість та втіха із са́ду, а по виноградниках пісні не бу́де й не зді́йметься окрик. Вина по чави́лах не буде топта́ти чави́льник, — окрик радости Я припини́в!
11 Chifukwa chake moyo wanga ukulira ngati pangwe kulirira Mowabu, mtima wanga ukubuwula chifukwa cha Kiri Hareseti.
Тому́ то в жало́бі звучать про Моав мої ну́трощі, мов би та арфа, а ну́тро моє — про Кір-Херес.
12 Ngakhale anthu a ku Mowabu apite ku malo awo achipembedzo koma amangodzitopetsa ndi kutaya nthawi chabe chifukwa sizidzatheka.
І буде, як ви́явиться, що змучивсь на взгі́р'ї Моав, і вві́йде молитись у святиню свою, та він не ося́гне нічо́го.
13 Awa ndi mawu amene Yehova wayankhula kale zokhudza Mowabu.
Оце слово, яке говорив був віддавна Госпо́дь про Моава.
14 Koma tsopano Yehova akuti, “Zisanathe zaka zitatu, potsata mʼmene munthu waganyu amawerengera, ulemerero wa Mowabu udzakhala utatheratu ndipo anthu ake ambiri adzakhala atawonongeka, ndipo opulumuka ake adzakhala ochepa ndi ofowoka.”
А тепер Господь каже, говорячи: За три ро́ки, одна́кові з лі́тами на́ймита, буде знева́жена слава Моава з усім велелю́ддям його, а позосталість — мала та дрібна, невелика!

< Yesaya 16 >