< Yesaya 16 >

1 Anthu a ku Mowabu atumiza mphatso za ana ankhosa onenepa, kuchokera ku Sela kudutsa chipululu mpaka kukafika ku phiri la Ziyoni.
Тримитець мей кырмуиторулуй цэрий, тримитеци-й дин Села, прин пустиу, ла мунтеле фийчей Сионулуй!
2 Monga momwe mbalame zimawulukira uku ndi uku akazimwaza mʼchisa, momwemonso akazi a ku Mowabu akuyendayenda ku madooko a Arinoni.
Ка о пасэре фугарэ, згорнитэ дин куйб, аша вор фи фийчеле Моабулуй ла тречеря Арнонулуй.
3 Amowabu aja anawuza a ku Yuda kuti, “Tiwuzeni chochita, gamulani zoti tichite. Inu mutiteteze kwa adani anthu. Mukhale ngati mthunzi wathu dzuwa lili pa liwombo. Mutibise, musatipereke ife othawa nkhondo kwa adani athu.
Ши вор зиче: ‘Сфэтуеште, мижлочеште, акоперэ-не зиуа-н амяза маре ку умбра та ка ноаптя нягрэ, аскунде пе чей че сунт урмэриць, ну да пе фацэ пе чей фуӂиць!
4 Lolani kuti anthu othawa nkhondo a ku Mowabu azikhala pakati panu; mukhale populumukira pawo kwa wowonongayo.” Nthawi idzafika ndipo wozunzayo sadzakhalaponso, kuwononga kudzaleka; waukaliyo adzachoka mʼdzikomo.
Ласэ сэ локуяскэ пентру о време ла тине чей гониць дин Моаб, фий ун лок де скэпаре пентру ей ымпотрива пустииторулуй!’ Кэч апэсаря ва ынчета, пустииря се ва сфырши, чел че калкэ цара ын пичоаре ва пери.
5 Mpando waufumu udzakhazikitsidwa mwachikondi; mmodzi mwa zidzukulu za Davide adzakhalapo mokhulupirika. Iyeyo poweruza adzatsata chilungamo ndipo adzalimbikitsa kuchita zachilungamo.
Ши атунч, ун скаун де домние се ва ынтэри прин ындураре ши се ва ведя шезынд ку крединчошие, ын каса луй Давид, ун жудекэтор, приетен ал дрептулуй ши плин де рывнэ пентру дрептате. –
6 Tinamva kuti Mowabu anadzikuza kwambiri. Kunyada kwawo ndi kunyogodola kwawo ndi kudzitama kwawo, zonse ndi zopanda phindu.
‘Аузим ынгымфаря мындрулуй Моаб, фудулия ши фала луй, труфия ши лэудэрошия луй.’
7 Nʼchifukwa chake Amowabu akulira kwambiri; iwo akulirira dziko lawo. Akubuma momvetsa chisoni chifukwa cha makeke a mphesa a ku Kiri Hareseti.
Де ачея ӂеме Моабул пентру Моаб, тоць ӂем; суспинаць пе дэрымэтуриле Кир-Харесетулуй, адынк мыхниць,
8 Minda ya ku Hesiboni yauma, minda ya mpesa ya ku Sibina yaguga. Atsogoleri a mitundu ina anapondaponda minda ya mpesa wabwino, imene nthambi zake zinakafika ku Yazeri, mpaka kutambalalira ku chipululu. Mizu yake inakafika mpaka ku tsidya la nyanja.
кэч кымпииле Хесбонулуй лынчезеск; стэпыний нямурилор ау сфэрымат бутучий вией дин Сибма, каре се ынтиндяу пынэ ла Иаезер ши се ынкылчяу прин пустиу: млэдицеле ей се ынтиндяу ши тречяу динколо де маре.
9 Kotero Ine ndikulira, monga mmene akulirira anthu a ku Yazeri, chifukwa cha minda ya mpesa ya ku Sibima. Inu anthu a ku Hesiboni, inu anthu a ku Eleali, ndikukunyowetsani ndi misozi! Mwalephera kupeza zokolola, chifukwa cha nkhondo imene inawononga zokolola zonse.
Де ачея плынг пентру вия дин Сибма ка пентру Иаезер; вэ уд ку лакримиле меле, Хесбонуле ши Елеале! Кэч песте кулесул роаделор воастре ши песте сечеришул востру а кэзут ун стригэт де рэзбой!
10 Chimwemwe ndi chisangalalo zalekeka ku minda yanu ya zipatso; palibe amene akuyimba kapena kufuwula mʼminda ya mpesa; palibe amene akupsinya vinyo ku malo opsinyira mphesa, pakuti ndathetsa kufuwula.
С-а дус букурия ши веселия дин кымпий! Ши ын вий ну май сунт кынтече, ну май сунт веселий! Нимень ну май калкэ винул ын тяскурь. Ам фэкут сэ ынчетезе стригэтеле де букурие ла кулес.
11 Chifukwa chake moyo wanga ukulira ngati pangwe kulirira Mowabu, mtima wanga ukubuwula chifukwa cha Kiri Hareseti.
Де ачея ымь плынӂе суфлетул пентру Моаб ка о харпэ ши инима, пентру Кир-Харес.
12 Ngakhale anthu a ku Mowabu apite ku malo awo achipembedzo koma amangodzitopetsa ndi kutaya nthawi chabe chifukwa sizidzatheka.
Ши, кынд се ва арэта Моабул, обосинду-се пе ынэлцимь, ши ва интра ын локашул сэу чел сфынт сэ се роаӂе, ну ва путя сэ капете нимик!”
13 Awa ndi mawu amene Yehova wayankhula kale zokhudza Mowabu.
Ачеста есте кувынтул пе каре л-а ростит Домнул де мултэ време асупра Моабулуй.
14 Koma tsopano Yehova akuti, “Zisanathe zaka zitatu, potsata mʼmene munthu waganyu amawerengera, ulemerero wa Mowabu udzakhala utatheratu ndipo anthu ake ambiri adzakhala atawonongeka, ndipo opulumuka ake adzakhala ochepa ndi ofowoka.”
Яр акум Домнул ворбеште ши зиче: „Ын трей ань, ка аний унуй симбриаш, слава Моабулуй ва фи диспрецуитэ, ымпреунэ ку тоатэ ачастэ маре мулциме, ши че ва рэмыне ва фи пуцин лукру, апроапе нимик.”

< Yesaya 16 >