< Yesaya 16 >

1 Anthu a ku Mowabu atumiza mphatso za ana ankhosa onenepa, kuchokera ku Sela kudutsa chipululu mpaka kukafika ku phiri la Ziyoni.
Thumelani iwundlu kumbusi welizwe lilisusa eSela lisiya enkangala, entabeni yendodakazi yeZiyoni.
2 Monga momwe mbalame zimawulukira uku ndi uku akazimwaza mʼchisa, momwemonso akazi a ku Mowabu akuyendayenda ku madooko a Arinoni.
Ngoba kuzakuthi, njengenyoni ezulazulayo exotshwe esidlekeni, azakuba njalo amadodakazi akoMowabi emazibukweni eArinoni.
3 Amowabu aja anawuza a ku Yuda kuti, “Tiwuzeni chochita, gamulani zoti tichite. Inu mutiteteze kwa adani anthu. Mukhale ngati mthunzi wathu dzuwa lili pa liwombo. Mutibise, musatipereke ife othawa nkhondo kwa adani athu.
Lethani iseluleko, lenze isinqumo; wenze isithunzi sakho sibe njengobusuku phakathi kwemini, ufihle abaxotshiweyo, ungavezi obalekayo.
4 Lolani kuti anthu othawa nkhondo a ku Mowabu azikhala pakati panu; mukhale populumukira pawo kwa wowonongayo.” Nthawi idzafika ndipo wozunzayo sadzakhalaponso, kuwononga kudzaleka; waukaliyo adzachoka mʼdzikomo.
Abaxotshiweyo bami kabahlale njengabezizwe phakathi kwakho, Mowabi; ube yisiphephelo kibo ebusweni bomchithi; ngoba umcindezeli usekucineni, ukuchitheka sekunyamalele, lonyathezela phansi usephelile elizweni.
5 Mpando waufumu udzakhazikitsidwa mwachikondi; mmodzi mwa zidzukulu za Davide adzakhalapo mokhulupirika. Iyeyo poweruza adzatsata chilungamo ndipo adzalimbikitsa kuchita zachilungamo.
Njalo kuzamiswa isihlalo sobukhosi ngomusa, njalo ahlale kiso ngobuqotho ethenteni likaDavida, esahlulela, lodinga isahlulelo, lophangisisa ukulunga.
6 Tinamva kuti Mowabu anadzikuza kwambiri. Kunyada kwawo ndi kunyogodola kwawo ndi kudzitama kwawo, zonse ndi zopanda phindu.
Sizwile ngokuziphakamisa kukaMowabi, uyazigqaja kakhulu; ukuzikhukhumeza kwakhe, lokuziqhenya kwakhe, lolaka lwakhe, ukuwumana kwakhe kakunjalo.
7 Nʼchifukwa chake Amowabu akulira kwambiri; iwo akulirira dziko lawo. Akubuma momvetsa chisoni chifukwa cha makeke a mphesa a ku Kiri Hareseti.
Ngakho uMowabi uzaqhinqela uMowabi isililo, bonke baqhinqe isililo; libubulele izisekelo zeKiri-Haresethi; isibili batshayiwe.
8 Minda ya ku Hesiboni yauma, minda ya mpesa ya ku Sibina yaguga. Atsogoleri a mitundu ina anapondaponda minda ya mpesa wabwino, imene nthambi zake zinakafika ku Yazeri, mpaka kutambalalira ku chipululu. Mizu yake inakafika mpaka ku tsidya la nyanja.
Ngoba amasimu eHeshiboni ayabuna, ivini leSibima; amakhosi ezizwe atshayele phansi amahlukuzo evini awo; afinyelele eJazeri, azulazule enkangala, ingatsha zawo zeluliwe, zachapha ulwandle.
9 Kotero Ine ndikulira, monga mmene akulirira anthu a ku Yazeri, chifukwa cha minda ya mpesa ya ku Sibima. Inu anthu a ku Hesiboni, inu anthu a ku Eleali, ndikukunyowetsani ndi misozi! Mwalephera kupeza zokolola, chifukwa cha nkhondo imene inawononga zokolola zonse.
Ngenxa yalokho ngizakhala inyembezi ngokukhala kweJazeri ngevini leSibima; ngikuthambise ngezinyembezi zami, Heshiboni, lawe Eleyale; ngoba ukujabulela izithelo zakho zehlobo lesivuno sakho sekuwile.
10 Chimwemwe ndi chisangalalo zalekeka ku minda yanu ya zipatso; palibe amene akuyimba kapena kufuwula mʼminda ya mpesa; palibe amene akupsinya vinyo ku malo opsinyira mphesa, pakuti ndathetsa kufuwula.
Intokozo lenjabulo sekususiwe ensimini ethelayo, lezivinini kakuhlatshelwa ngoma; kakulakumemeza; kakulamnyatheli onyathela iwayini ezikhamelweni zewayini; ngimisile ukumemeza kwenjabulo.
11 Chifukwa chake moyo wanga ukulira ngati pangwe kulirira Mowabu, mtima wanga ukubuwula chifukwa cha Kiri Hareseti.
Ngenxa yalokho imibilini yami iyakhala njengechacho ngoMowabi, lengaphakathi yami ngeKiri-Haresi.
12 Ngakhale anthu a ku Mowabu apite ku malo awo achipembedzo koma amangodzitopetsa ndi kutaya nthawi chabe chifukwa sizidzatheka.
Kuzakuthi sekubonakele ukuthi uMowabi uzidinisile endaweni ephakemeyo, khona ezangena endlini yakhe engcwele ukukhuleka, kodwa kayikuphumelela.
13 Awa ndi mawu amene Yehova wayankhula kale zokhudza Mowabu.
Leli yilizwi iNkosi elikhulume ngoMowabi kusukela kulesosikhathi.
14 Koma tsopano Yehova akuti, “Zisanathe zaka zitatu, potsata mʼmene munthu waganyu amawerengera, ulemerero wa Mowabu udzakhala utatheratu ndipo anthu ake ambiri adzakhala atawonongeka, ndipo opulumuka ake adzakhala ochepa ndi ofowoka.”
Kodwa khathesi iNkosi ikhuluma isithi: Phakathi kweminyaka emithathu, njengeminyaka yoqhatshiweyo, udumo lukaMowabi luzadelelwa, elaleloxuku lonke elikhulu; lensali izakuba nlutshwana, incane, ingelamandla.

< Yesaya 16 >