< Yesaya 16 >
1 Anthu a ku Mowabu atumiza mphatso za ana ankhosa onenepa, kuchokera ku Sela kudutsa chipululu mpaka kukafika ku phiri la Ziyoni.
Envoyez l'agneau au Dominateur de la terre, envoyez-le du rocher du désert, à la montagne de la fille de Sion.
2 Monga momwe mbalame zimawulukira uku ndi uku akazimwaza mʼchisa, momwemonso akazi a ku Mowabu akuyendayenda ku madooko a Arinoni.
Car il arrivera que les filles de Moab seront au passage d'Arnon, comme un oiseau volant çà et là, [comme] une nichée chassée de son nid.
3 Amowabu aja anawuza a ku Yuda kuti, “Tiwuzeni chochita, gamulani zoti tichite. Inu mutiteteze kwa adani anthu. Mukhale ngati mthunzi wathu dzuwa lili pa liwombo. Mutibise, musatipereke ife othawa nkhondo kwa adani athu.
Mets en avant le conseil, fais l'ordonnance, sers d'ombre comme une nuit au milieu du midi; cache ceux qui ont été chassés, et ne décèle point ceux qui sont errants.
4 Lolani kuti anthu othawa nkhondo a ku Mowabu azikhala pakati panu; mukhale populumukira pawo kwa wowonongayo.” Nthawi idzafika ndipo wozunzayo sadzakhalaponso, kuwononga kudzaleka; waukaliyo adzachoka mʼdzikomo.
Que ceux de mon peuple qui ont été chassés séjournent chez toi, ô Moab! sois leur une retraite contre celui qui fait le dégât; car celui qui usait d'extorsion a cessé, le dégât a pris fin, ceux qui foulaient sont consumés de dessus la terre.
5 Mpando waufumu udzakhazikitsidwa mwachikondi; mmodzi mwa zidzukulu za Davide adzakhalapo mokhulupirika. Iyeyo poweruza adzatsata chilungamo ndipo adzalimbikitsa kuchita zachilungamo.
Et le trône sera établi par la gratuité; et sur ce trône sera assis en vérité, dans le tabernacle de David, un qui jugera, qui recherchera le droit, et qui se hâtera de faire justice.
6 Tinamva kuti Mowabu anadzikuza kwambiri. Kunyada kwawo ndi kunyogodola kwawo ndi kudzitama kwawo, zonse ndi zopanda phindu.
Nous avons entendu l'orgueil de Moab le très-orgueilleux, sa fierté, et son orgueil, et son arrogance; ceux sur qui il s'appuie ne sont rien de ferme.
7 Nʼchifukwa chake Amowabu akulira kwambiri; iwo akulirira dziko lawo. Akubuma momvetsa chisoni chifukwa cha makeke a mphesa a ku Kiri Hareseti.
C'est pourquoi Moab hurlera sur Moab, chacun hurlera; vous grommellerez pour les fondements de Kir-Haréseth; il n'y aura que des gens blessés à mort.
8 Minda ya ku Hesiboni yauma, minda ya mpesa ya ku Sibina yaguga. Atsogoleri a mitundu ina anapondaponda minda ya mpesa wabwino, imene nthambi zake zinakafika ku Yazeri, mpaka kutambalalira ku chipululu. Mizu yake inakafika mpaka ku tsidya la nyanja.
Car les guérets de Hesbon, et le vignoble de Sibma, languissent; les Seigneurs des nations ont foulé ses meilleurs plants, [qui] atteignaient jusques à Jahzer, ils couraient çà et là par le désert, et ses provins s'étendaient et passaient au delà de la mer.
9 Kotero Ine ndikulira, monga mmene akulirira anthu a ku Yazeri, chifukwa cha minda ya mpesa ya ku Sibima. Inu anthu a ku Hesiboni, inu anthu a ku Eleali, ndikukunyowetsani ndi misozi! Mwalephera kupeza zokolola, chifukwa cha nkhondo imene inawononga zokolola zonse.
C'est pourquoi je pleurerai du pleur de Jahzer, le vignoble de Sibma; je t'arroserai de mes larmes, ô Hesbon et Elhalé! car l'ennemi avec des cris s'est jeté sur tes fruits d'Eté, et sur ta moisson.
10 Chimwemwe ndi chisangalalo zalekeka ku minda yanu ya zipatso; palibe amene akuyimba kapena kufuwula mʼminda ya mpesa; palibe amene akupsinya vinyo ku malo opsinyira mphesa, pakuti ndathetsa kufuwula.
Et la joie et la gaieté s'est retirée du champ fertile; on ne se réjouira plus, et on ne s'égayera plus dans les vignes, celui qui foulait le vin ne le foulera plus dans les cuves, j'ai fait cesser la chanson de la vendange.
11 Chifukwa chake moyo wanga ukulira ngati pangwe kulirira Mowabu, mtima wanga ukubuwula chifukwa cha Kiri Hareseti.
C'est pourquoi mes entrailles mèneront du bruit comme une harpe sur Moab, et mon ventre sur Kir-Hérès.
12 Ngakhale anthu a ku Mowabu apite ku malo awo achipembedzo koma amangodzitopetsa ndi kutaya nthawi chabe chifukwa sizidzatheka.
Et il arrivera qu'on verra que Moab se lassera [pour aller] au haut lieu, et qu'il entrera en son saint lieu pour prier; mais il ne pourra rien obtenir.
13 Awa ndi mawu amene Yehova wayankhula kale zokhudza Mowabu.
C'est là la parole que l'Eternel a prononcée depuis longtemps sur Moab.
14 Koma tsopano Yehova akuti, “Zisanathe zaka zitatu, potsata mʼmene munthu waganyu amawerengera, ulemerero wa Mowabu udzakhala utatheratu ndipo anthu ake ambiri adzakhala atawonongeka, ndipo opulumuka ake adzakhala ochepa ndi ofowoka.”
Et maintenant l'Eternel a parlé, en disant; dans trois ans, tels que sont les ans d'un mercenaire, la gloire de Moab sera avilie, avec toute cette grande multitude; et le résidu sera petit, ce sera peu de chose, ce ne sera rien de considérable.