< Yesaya 16 >
1 Anthu a ku Mowabu atumiza mphatso za ana ankhosa onenepa, kuchokera ku Sela kudutsa chipululu mpaka kukafika ku phiri la Ziyoni.
And they will send ... to the mountain of the daughter of Zion.
2 Monga momwe mbalame zimawulukira uku ndi uku akazimwaza mʼchisa, momwemonso akazi a ku Mowabu akuyendayenda ku madooko a Arinoni.
For the daughters of Moab will be like wandering birds, like a place from which the young birds have gone in flight, at the ways across the Arnon.
3 Amowabu aja anawuza a ku Yuda kuti, “Tiwuzeni chochita, gamulani zoti tichite. Inu mutiteteze kwa adani anthu. Mukhale ngati mthunzi wathu dzuwa lili pa liwombo. Mutibise, musatipereke ife othawa nkhondo kwa adani athu.
Give wise directions, make a decision; let your shade be as night in full day: keep safe those who are in flight; do not give up the wandering ones.
4 Lolani kuti anthu othawa nkhondo a ku Mowabu azikhala pakati panu; mukhale populumukira pawo kwa wowonongayo.” Nthawi idzafika ndipo wozunzayo sadzakhalaponso, kuwononga kudzaleka; waukaliyo adzachoka mʼdzikomo.
Let those who have been forced out of Moab have a resting-place with you; be a cover to them from him who is making waste their land: till the cruel ones are cut off, and wasting has come to an end, and those who take pleasure in crushing the poor are gone from the land.
5 Mpando waufumu udzakhazikitsidwa mwachikondi; mmodzi mwa zidzukulu za Davide adzakhalapo mokhulupirika. Iyeyo poweruza adzatsata chilungamo ndipo adzalimbikitsa kuchita zachilungamo.
Then a king's seat will be based on mercy, and one will be seated on it in the tent of David for ever; judging uprightly, and quick to do righteousness.
6 Tinamva kuti Mowabu anadzikuza kwambiri. Kunyada kwawo ndi kunyogodola kwawo ndi kudzitama kwawo, zonse ndi zopanda phindu.
We have had word of the pride of Moab, how great it is; how he is lifted up in pride and passion: his high words about himself are false.
7 Nʼchifukwa chake Amowabu akulira kwambiri; iwo akulirira dziko lawo. Akubuma momvetsa chisoni chifukwa cha makeke a mphesa a ku Kiri Hareseti.
For this cause everyone in Moab will give cries of grief for Moab: crushed to the earth, they will be weeping for the men of Kir-hareseth.
8 Minda ya ku Hesiboni yauma, minda ya mpesa ya ku Sibina yaguga. Atsogoleri a mitundu ina anapondaponda minda ya mpesa wabwino, imene nthambi zake zinakafika ku Yazeri, mpaka kutambalalira ku chipululu. Mizu yake inakafika mpaka ku tsidya la nyanja.
For the fields of Heshbon are waste, the vine of Sibmah is dead; the lords of nations were overcome by the produce of her vines; her vine-plants went as far as Jazer, and came even to the waste land; her branches were stretched out to the sea.
9 Kotero Ine ndikulira, monga mmene akulirira anthu a ku Yazeri, chifukwa cha minda ya mpesa ya ku Sibima. Inu anthu a ku Hesiboni, inu anthu a ku Eleali, ndikukunyowetsani ndi misozi! Mwalephera kupeza zokolola, chifukwa cha nkhondo imene inawononga zokolola zonse.
For this cause my sorrow for the vine of Sibmah will be like the weeping for Jazer: my eyes are dropping water on you, O Heshbon and Elealeh! For they are sounding the war-cry over your summer fruits and the getting in of your grain;
10 Chimwemwe ndi chisangalalo zalekeka ku minda yanu ya zipatso; palibe amene akuyimba kapena kufuwula mʼminda ya mpesa; palibe amene akupsinya vinyo ku malo opsinyira mphesa, pakuti ndathetsa kufuwula.
And all joy is gone; no longer are they glad for the fertile field; and in the vine-gardens there are no songs or sounds of joy: the crushing of grapes has come to an end, and its glad cry has been stopped.
11 Chifukwa chake moyo wanga ukulira ngati pangwe kulirira Mowabu, mtima wanga ukubuwula chifukwa cha Kiri Hareseti.
For this cause the cords of my heart are sounding for Moab, and I am full of sorrow for Kir-heres.
12 Ngakhale anthu a ku Mowabu apite ku malo awo achipembedzo koma amangodzitopetsa ndi kutaya nthawi chabe chifukwa sizidzatheka.
And when Moab goes up to the high place, and makes prayer in the house of his god, it will have no effect.
13 Awa ndi mawu amene Yehova wayankhula kale zokhudza Mowabu.
This is the word which the Lord said about Moab in the past.
14 Koma tsopano Yehova akuti, “Zisanathe zaka zitatu, potsata mʼmene munthu waganyu amawerengera, ulemerero wa Mowabu udzakhala utatheratu ndipo anthu ake ambiri adzakhala atawonongeka, ndipo opulumuka ake adzakhala ochepa ndi ofowoka.”
But now the Lord has said, In three years, the years of a servant working for payment, the glory of Moab, all that great people, will be turned to shame, and the rest of Moab will be very small and without honour.