< Yesaya 15 >

1 Uthenga wonena za Mowabu: Popeza kuti mu usiku umodzi wokha mzinda wa Ari wa ku Mowabu wawonongedwa, wawonongedwa pa usiku umodzi wokha. Mzinda wa Kiri wawonongedwa, wawonongedwa pa usiku umodzi wokha.
Breme Moába. Ker je ponoči Ar Moáb opustošen in priveden v tišino, ker je ponoči Kir Moáb opustošen in priveden v tišino;
2 Anthu a ku Diboni akupita ku nyumba ya milungu yawo, akupita ku malo awo achipembedzo kukalira; anthu a ku Mowabu akulirira mofuwula mzinda wa Nebo ndi wa Medeba. Mutu uliwonse wametedwa mpala, ndipo ndevu zonse zametedwa.
odšel je gor do Bajita in do Dibóna, visoka kraja, da bi jokal. Moáb bo tulil nad Nebójem in nad Médebo, na vseh njihovih glavah bo plešavost in vsaka brada bo odrezana.
3 Mʼmisewu akuvala ziguduli; pa madenga ndi mʼmabwalo aliyense akulira mofuwula, misozi ili pupupu.
Na njihovih ulicah se bodo opasovali z vrečevino, na vrhovih njihovih hiš in na njihovih ulicah bo vsakdo tulil, obilno jokajoč.
4 Anthu a ku Hesiboni ndi Eleali akulira mofuwula, mawu awo akumveka mpaka ku Yahazi. Kotero asilikali a ku Mowabu akulira mofuwula, ndipo ataya mtima.
Hešbón bo vpil in Elalé. Njun glas bo slišati celó do Jahaca, zato bodo oboroženi moábski vojaki zavpili, njegovo življenje mu bo mučno.
5 Inenso ndikulirira Mowabu; chifukwa othawa nkhondo ake akupita akulira ku chikweza cha Luluti mpaka ku Zowari ndi Egilati-Selisiya akupita akulira ku chikweza cha Luhiti, Akulira mosweka mtima pa njira yopita ku Horonaimu; akulira mosweka mtima chifukwa cha chiwonongeko chawo.
Moje srce bo vpilo zaradi Moába, njegovi ubežniki bodo bežali do Coarja, telica starosti treh let, kajti ob vzpenjanju Luhíta bodo jokajoč šli gor, kajti na poti Horonájima bodo vzdignili krik pogube.
6 Madzi a ku Nimurimu aphwa ndipo udzu wauma; zomera zawonongeka ndipo palibe chomera chobiriwira chatsala.
Kajti vode Nimríma bodo zapuščene, kajti seno je propadlo, trava je posušena, tam ni nobene zelene stvari.
7 Kotero kuti chuma chomwe anachipeza ndi kuchisunga, achitenga kuti awoloke nacho chigwembe cha Misondozi.
Zato bodo obilje, ki so ga dobili in to, kar so nakopičili, odnesli proč k vrbovemu potoku.
8 Kulira kwawo kukumveka mʼdziko lonse la Mowabu; kulira kwawo kosweka mtima kukumveka mpaka ku Egilaimu ndi Beeri-Elimu.
Kajti vpitje je šlo naokoli Moábovih mej, njihovo tuljenje do Eglájima in njihovo tuljenje do Beêr Elíma.
9 Madzi a ku Dimoni afiira ndi magazi, komabe ndidzabweretsa zina zambiri pa Dimoni, mkango woti udzagwire aliyense othawa mu Mowabu ndi aliyense wotsala mʼdzikomo.
Kajti vode Dimóna bodo polne krvi, kajti privedel bom več nad Dimón, leve nad tiste, ki pobegnejo iz Moába in nad preostanek dežele.

< Yesaya 15 >