< Yesaya 15 >

1 Uthenga wonena za Mowabu: Popeza kuti mu usiku umodzi wokha mzinda wa Ari wa ku Mowabu wawonongedwa, wawonongedwa pa usiku umodzi wokha. Mzinda wa Kiri wawonongedwa, wawonongedwa pa usiku umodzi wokha.
وحی درباره موآب: زیرا که در شبی عار موآب خراب وهلاک شده است زیرا در شبی قیر موآب خراب وهلاک شده است.۱
2 Anthu a ku Diboni akupita ku nyumba ya milungu yawo, akupita ku malo awo achipembedzo kukalira; anthu a ku Mowabu akulirira mofuwula mzinda wa Nebo ndi wa Medeba. Mutu uliwonse wametedwa mpala, ndipo ndevu zonse zametedwa.
به بتکده و دیبون به مکان های بلند به جهت گریستن برآمده‌اند. موآب برای نبوو میدبا ولوله می‌کند. بر سر هریکی از ایشان گری است و ریشهای همه تراشیده شده است.۲
3 Mʼmisewu akuvala ziguduli; pa madenga ndi mʼmabwalo aliyense akulira mofuwula, misozi ili pupupu.
درکوچه های خود کمر خود را به پلاس می‌بندند وبر پشت بامها و در چهارسوهای خود هرکس ولوله می‌نماید و اشکها می‌ریزد.۳
4 Anthu a ku Hesiboni ndi Eleali akulira mofuwula, mawu awo akumveka mpaka ku Yahazi. Kotero asilikali a ku Mowabu akulira mofuwula, ndipo ataya mtima.
و حشبون والعاله فریاد برمی آورند. آواز ایشان تا یاهص مسموع می‌شود. بنابراین مسلحان موآب ناله می‌کنند و جان ایشان در ایشان می‌لرزد.۴
5 Inenso ndikulirira Mowabu; chifukwa othawa nkhondo ake akupita akulira ku chikweza cha Luluti mpaka ku Zowari ndi Egilati-Selisiya akupita akulira ku chikweza cha Luhiti, Akulira mosweka mtima pa njira yopita ku Horonaimu; akulira mosweka mtima chifukwa cha chiwonongeko chawo.
دل من به جهت موآب فریاد برمی آورد. فراریانش تا به صوغر و عجلت شلشیا نعره می‌زنند زیرا که ایشان به فراز لوحیت با گریه برمی آیند. زیرا که از راه حورونایم صدای هلاکت برمی آورند.۵
6 Madzi a ku Nimurimu aphwa ndipo udzu wauma; zomera zawonongeka ndipo palibe chomera chobiriwira chatsala.
زیرا که آبهای نمریم خراب شده، چونکه علف خشکیده و گیاه تلف شده و هیچ‌چیز سبز باقی نمانده است.۶
7 Kotero kuti chuma chomwe anachipeza ndi kuchisunga, achitenga kuti awoloke nacho chigwembe cha Misondozi.
بنابراین دولتی را که تحصیل نموده‌اند و اندوخته های خود را بر وادی بیدها می‌برند.۷
8 Kulira kwawo kukumveka mʼdziko lonse la Mowabu; kulira kwawo kosweka mtima kukumveka mpaka ku Egilaimu ndi Beeri-Elimu.
زیرا که فریادایشان حدود موآب را احاطه نموده و ولوله ایشان تا اجلایم و ولوله ایشان تا بئر ایلیم رسیده است.۸
9 Madzi a ku Dimoni afiira ndi magazi, komabe ndidzabweretsa zina zambiri pa Dimoni, mkango woti udzagwire aliyense othawa mu Mowabu ndi aliyense wotsala mʼdzikomo.
چونکه آبهای دیمون از خون پر شده زانرو که بر دیمون (بلایای ) زیاد خواهم آوردیعنی شیری را بر فراریان موآب و بر بقیه زمینش (خواهم گماشت ).۹

< Yesaya 15 >