< Yesaya 15 >

1 Uthenga wonena za Mowabu: Popeza kuti mu usiku umodzi wokha mzinda wa Ari wa ku Mowabu wawonongedwa, wawonongedwa pa usiku umodzi wokha. Mzinda wa Kiri wawonongedwa, wawonongedwa pa usiku umodzi wokha.
Umthwalo kaMowabi. Ngoba ngobusuku iAri kaMowabi ichithekile, iqunyiwe; ngoba ngobusuku iKiri kaMowabi ichithekile, iqunyiwe.
2 Anthu a ku Diboni akupita ku nyumba ya milungu yawo, akupita ku malo awo achipembedzo kukalira; anthu a ku Mowabu akulirira mofuwula mzinda wa Nebo ndi wa Medeba. Mutu uliwonse wametedwa mpala, ndipo ndevu zonse zametedwa.
Wenyukela eBayiti leDiboni, indawo eziphakemeyo, ukuyalila; uMowabi uzaqhinqa isililo ngeNebo langeMedeba; kulempabanga kuwo wonke amakhanda abo, zonke indevu zigeliwe;
3 Mʼmisewu akuvala ziguduli; pa madenga ndi mʼmabwalo aliyense akulira mofuwula, misozi ili pupupu.
ezitaladeni zabo bazibhinca ngamasaka; empahleni zezindlu zabo lezitaladeni zabo wonke uqhinqa isililo, besehla bekhala inyembezi.
4 Anthu a ku Hesiboni ndi Eleali akulira mofuwula, mawu awo akumveka mpaka ku Yahazi. Kotero asilikali a ku Mowabu akulira mofuwula, ndipo ataya mtima.
LeHeshiboni leEleyale kuzakhala; ilizwi labo lizwakale kuze kube seJahazi; ngenxa yalokhu abahlomileyo bakoMowabi bayamemeza; umphefumulo wakhe uyathuthumela kuye.
5 Inenso ndikulirira Mowabu; chifukwa othawa nkhondo ake akupita akulira ku chikweza cha Luluti mpaka ku Zowari ndi Egilati-Selisiya akupita akulira ku chikweza cha Luhiti, Akulira mosweka mtima pa njira yopita ku Horonaimu; akulira mosweka mtima chifukwa cha chiwonongeko chawo.
Inhliziyo yami iyamkhalela uMowabi; ababalekayo bakhe bafinyelele eZowari, ithokazi elileminyaka emithathu; ngoba umqanso weLuhithi, bawenyuka bekhala inyembezi; ngoba endleleni yeHoronayimi baphakamisa ukukhala kwencithakalo.
6 Madzi a ku Nimurimu aphwa ndipo udzu wauma; zomera zawonongeka ndipo palibe chomera chobiriwira chatsala.
Ngoba amanzi eNimirimi azakuba zincithakalo; ngoba utshani buyoma, uhlaza luyaphela, kakukho okuluhlaza.
7 Kotero kuti chuma chomwe anachipeza ndi kuchisunga, achitenga kuti awoloke nacho chigwembe cha Misondozi.
Ngenxa yalokhu ukwanda abakwenzileyo lempahla yabo bazakuthwalela esifuleni seminyezane.
8 Kulira kwawo kukumveka mʼdziko lonse la Mowabu; kulira kwawo kosweka mtima kukumveka mpaka ku Egilaimu ndi Beeri-Elimu.
Ngoba ukukhala kuzabhoda umngcele kaMowabi, ukuqhinqa kwakhe isililo kufinyelela eEgilayimi, yebo, ukuqhinqa kwakhe isililo kufinyelela eBeri-Elimi.
9 Madzi a ku Dimoni afiira ndi magazi, komabe ndidzabweretsa zina zambiri pa Dimoni, mkango woti udzagwire aliyense othawa mu Mowabu ndi aliyense wotsala mʼdzikomo.
Ngoba amanzi eDiboni agcwele igazi; ngoba ngizamisela iDiboni okunye futhi, isilwane kulabo abaphunyukileyo bakoMowabi lakunsali yelizwe.

< Yesaya 15 >