< Yesaya 15 >
1 Uthenga wonena za Mowabu: Popeza kuti mu usiku umodzi wokha mzinda wa Ari wa ku Mowabu wawonongedwa, wawonongedwa pa usiku umodzi wokha. Mzinda wa Kiri wawonongedwa, wawonongedwa pa usiku umodzi wokha.
Beszéd Móábról. Bizony éjjel pusztíttatott el Ár-Móáb, megsemmisült; bizony éjjel pusztítatott el Kír-Móáb, megsemmisült.
2 Anthu a ku Diboni akupita ku nyumba ya milungu yawo, akupita ku malo awo achipembedzo kukalira; anthu a ku Mowabu akulirira mofuwula mzinda wa Nebo ndi wa Medeba. Mutu uliwonse wametedwa mpala, ndipo ndevu zonse zametedwa.
Fölment Bájit meg Díbón a magaslatokra sírásra; Nebó fölött és Médeba fölött jajgat Móáb, minden fején kopaszság, minden szakáll levágva.
3 Mʼmisewu akuvala ziguduli; pa madenga ndi mʼmabwalo aliyense akulira mofuwula, misozi ili pupupu.
Utcáin zsákot kötöttek föl, háztetőin és piacain mindnyája jajgat, sírásban folyik szét.
4 Anthu a ku Hesiboni ndi Eleali akulira mofuwula, mawu awo akumveka mpaka ku Yahazi. Kotero asilikali a ku Mowabu akulira mofuwula, ndipo ataya mtima.
Kiáltott Chesbón és Eleálé, Jáhaczig hallatszott hangjuk; ezért felriadnak Móáb fegyveresei, lelke megremegett őbenne.
5 Inenso ndikulirira Mowabu; chifukwa othawa nkhondo ake akupita akulira ku chikweza cha Luluti mpaka ku Zowari ndi Egilati-Selisiya akupita akulira ku chikweza cha Luhiti, Akulira mosweka mtima pa njira yopita ku Horonaimu; akulira mosweka mtima chifukwa cha chiwonongeko chawo.
Szívem Móábért kiált, szökevényei egész Czóarig, Eglat-Selísíjáig; mert Lúchit hágóján sírással mennek fel, mert Chórónájim felé vészkiáltást keltenek.
6 Madzi a ku Nimurimu aphwa ndipo udzu wauma; zomera zawonongeka ndipo palibe chomera chobiriwira chatsala.
Mert Nimrim vizei puszta helyekké lesznek; mert elszáradt a fű, eltűnt a pázsit, nincs zöld többé.
7 Kotero kuti chuma chomwe anachipeza ndi kuchisunga, achitenga kuti awoloke nacho chigwembe cha Misondozi.
Ezért a vagyont, melyet szereztek, és tulajdonukat a fűzfák patakján viszik át.
8 Kulira kwawo kukumveka mʼdziko lonse la Mowabu; kulira kwawo kosweka mtima kukumveka mpaka ku Egilaimu ndi Beeri-Elimu.
Mert körülvette a kiáltás Móáb határát, egész Eglájimig a jajgatása; Beér-Élímig a jajgatása.
9 Madzi a ku Dimoni afiira ndi magazi, komabe ndidzabweretsa zina zambiri pa Dimoni, mkango woti udzagwire aliyense othawa mu Mowabu ndi aliyense wotsala mʼdzikomo.
Mert Dímón vizei megteltek vérrel, mert Dímón ellen még többet hozok, Móáb menekült része ellen oroszlánt, meg a föld maradéka ellen.