< Yesaya 15 >
1 Uthenga wonena za Mowabu: Popeza kuti mu usiku umodzi wokha mzinda wa Ari wa ku Mowabu wawonongedwa, wawonongedwa pa usiku umodzi wokha. Mzinda wa Kiri wawonongedwa, wawonongedwa pa usiku umodzi wokha.
Le fardeau de Moab. Car en une nuit, Ar de Moab est dévasté et réduit à néant. Car en une nuit, Ar de Moab est dévasté et réduit à néant.
2 Anthu a ku Diboni akupita ku nyumba ya milungu yawo, akupita ku malo awo achipembedzo kukalira; anthu a ku Mowabu akulirira mofuwula mzinda wa Nebo ndi wa Medeba. Mutu uliwonse wametedwa mpala, ndipo ndevu zonse zametedwa.
Ils sont montés à Bayith et à Dibon, sur les hauts lieux, pour pleurer. Moab gémit sur Nebo et sur Medeba. La calvitie est sur toutes leurs têtes. Toute barbe est coupée.
3 Mʼmisewu akuvala ziguduli; pa madenga ndi mʼmabwalo aliyense akulira mofuwula, misozi ili pupupu.
Dans leurs rues, ils se revêtent de sacs. Dans leurs rues et sur leurs toits, tous gémissent et pleurent abondamment.
4 Anthu a ku Hesiboni ndi Eleali akulira mofuwula, mawu awo akumveka mpaka ku Yahazi. Kotero asilikali a ku Mowabu akulira mofuwula, ndipo ataya mtima.
Hesbon crie avec Élealé. Leur voix se fait entendre jusqu'à Jahaz. C'est pourquoi les hommes armés de Moab crient à haute voix. Leurs âmes tremblent au dedans d'eux.
5 Inenso ndikulirira Mowabu; chifukwa othawa nkhondo ake akupita akulira ku chikweza cha Luluti mpaka ku Zowari ndi Egilati-Selisiya akupita akulira ku chikweza cha Luhiti, Akulira mosweka mtima pa njira yopita ku Horonaimu; akulira mosweka mtima chifukwa cha chiwonongeko chawo.
Mon cœur pleure sur Moab! Ses nobles fuient vers Tsoar, vers Églath-Shelishiyah; car ils montent en pleurant par la montée de Luhith; car sur le chemin des Horonaïm, ils poussent des cris de destruction.
6 Madzi a ku Nimurimu aphwa ndipo udzu wauma; zomera zawonongeka ndipo palibe chomera chobiriwira chatsala.
Car les eaux de Nimrim seront désolées; car l'herbe s'est desséchée, l'herbe tendre se fane, il n'y a plus rien de vert.
7 Kotero kuti chuma chomwe anachipeza ndi kuchisunga, achitenga kuti awoloke nacho chigwembe cha Misondozi.
C'est pourquoi ils emporteront l'abondance qu'ils ont acquise, et ce qu'ils ont amassé, sur le ruisseau des saules.
8 Kulira kwawo kukumveka mʼdziko lonse la Mowabu; kulira kwawo kosweka mtima kukumveka mpaka ku Egilaimu ndi Beeri-Elimu.
Car le cri a fait le tour des frontières de Moab, son gémissement jusqu'à Églaïm, et sa plainte jusqu'à Beer Elim.
9 Madzi a ku Dimoni afiira ndi magazi, komabe ndidzabweretsa zina zambiri pa Dimoni, mkango woti udzagwire aliyense othawa mu Mowabu ndi aliyense wotsala mʼdzikomo.
Car les eaux de Dimon sont pleines de sang; car je fais venir encore sur Dimon, un lion sur ceux de Moab qui s'échappent, et sur le reste du pays.