< Yesaya 15 >

1 Uthenga wonena za Mowabu: Popeza kuti mu usiku umodzi wokha mzinda wa Ari wa ku Mowabu wawonongedwa, wawonongedwa pa usiku umodzi wokha. Mzinda wa Kiri wawonongedwa, wawonongedwa pa usiku umodzi wokha.
Profeti imod Moab. I den Nat, da Ar-Moab blev forstyrret, gik det til Grunde; i den Nat, da Kir-Moab blev forstyrret, gik det til Grunde.
2 Anthu a ku Diboni akupita ku nyumba ya milungu yawo, akupita ku malo awo achipembedzo kukalira; anthu a ku Mowabu akulirira mofuwula mzinda wa Nebo ndi wa Medeba. Mutu uliwonse wametedwa mpala, ndipo ndevu zonse zametedwa.
Man gaar op til Afgudshuset og til Dibon, til Højene for at græde; paa Nebo og paa Medba hyler Moab, hvert Hoved der er skaldet, hvert Skæg er afskaaret.
3 Mʼmisewu akuvala ziguduli; pa madenga ndi mʼmabwalo aliyense akulira mofuwula, misozi ili pupupu.
Paa Gaderne derudi ombinde de sig med Sæk, paa Tagene og paa Gaderne derudi hyle de alle sammen og flyde hen i Graad.
4 Anthu a ku Hesiboni ndi Eleali akulira mofuwula, mawu awo akumveka mpaka ku Yahazi. Kotero asilikali a ku Mowabu akulira mofuwula, ndipo ataya mtima.
Og Hesbon og Eleale raabe, deres Røst høres indtil Jahaz; derfor skrige de bevæbnede i Moab, hvers Sjæl er modfalden.
5 Inenso ndikulirira Mowabu; chifukwa othawa nkhondo ake akupita akulira ku chikweza cha Luluti mpaka ku Zowari ndi Egilati-Selisiya akupita akulira ku chikweza cha Luhiti, Akulira mosweka mtima pa njira yopita ku Horonaimu; akulira mosweka mtima chifukwa cha chiwonongeko chawo.
Mit Hjerte raaber over Moab, hvis Flygtninge ty lige til Zoar, til Eglath-Selisia; thi man gaar op ad Lukits Opgang med Graad, og paa Vejen til Horonaim opløfter man et Fortvivlelsens Skrig.
6 Madzi a ku Nimurimu aphwa ndipo udzu wauma; zomera zawonongeka ndipo palibe chomera chobiriwira chatsala.
Thi Nimrims Vande blive til Ørk; thi Urterne ere hentørrede, Græsset er borte, der er intet grønt.
7 Kotero kuti chuma chomwe anachipeza ndi kuchisunga, achitenga kuti awoloke nacho chigwembe cha Misondozi.
Derfor bære de Levningen af det, som de have forhvervet sig, og hvad de have henlagt, over Pilebækken.
8 Kulira kwawo kukumveka mʼdziko lonse la Mowabu; kulira kwawo kosweka mtima kukumveka mpaka ku Egilaimu ndi Beeri-Elimu.
Thi Skriget omspænder Moabs Landemærke, dets Hyl naar indtil Eglajm, og dets Hyl til Beer-Elim.
9 Madzi a ku Dimoni afiira ndi magazi, komabe ndidzabweretsa zina zambiri pa Dimoni, mkango woti udzagwire aliyense othawa mu Mowabu ndi aliyense wotsala mʼdzikomo.
Thi Dimons Vande ere fulde af Blod, og jeg vil lade endnu mere komme over Dimon; jeg vil sende en Løve over de undkomne af Moab og over de overblevne i Landet.

< Yesaya 15 >